< Numbers 34 >

1 And the Lord spoke to Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Instruct the sons of Israel, and you shall say to them: When you will have entered into the land of Canaan, and it has fallen into your possession by lot, it shall be bound by these limits:
“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
3 The southern part shall begin from the wilderness of Sin, which is next to Edom, and it shall have the Sea of Salt as a limit to the east.
“‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
4 It shall circle on the south side along the ascent of the Scorpion, by this way crossing into Senna, and passing through, from the south, as far as Kadesh-barnea, from which its confines shall go out to the town called Adar, and extend even to Azmon.
Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
5 And its limits shall go around from Azmon to the Torrent of Egypt, and shall end at the shore of the Great Sea.
kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
6 Then the western region shall begin from the Great Sea, and the same shall be its end.
“‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
7 Furthermore, toward the northern region, its limits shall begin from the Great Sea, passing through even to the highest mountain.
“‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
8 From there, it limits shall advance into Hamath, as far as the limits of Zedad.
ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
9 And its confines shall go all the way to Ziphron, and to the village of Enan. These shall be the limits on the northern side.
ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
10 From there, its limits shall be measured, facing the east side, from the village of Enan as far as Shepham.
“‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
11 And from Shepham, the boundaries shall descend into Riblah, opposite the fountain of Daphnis. From there, the boundaries shall pass through, opposite the east, to the Sea of Chinnereth,
Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
12 and shall extend as far as the Jordan, and, at the furthest extent, shall be enclosed by the Sea of Salt. You shall have this land, with its borders all around.”
Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
13 And Moses instructed the sons of Israel, saying: “This shall be the land which you shall possess by lot, and which the Lord has ordered to be given to the nine tribes, and to the half tribe.
Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
14 For the tribe of the sons of Ruben, by their families, and the tribe of the sons of Gad, according to the number of their kinships, and also one half of the tribe of Manasseh,
chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
15 that is, two and a half tribes, have received their portion across the Jordan, opposite Jericho, toward the eastern side.”
Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
16 And the Lord said to Moses:
Yehova anawuza Mose kuti,
17 “These are the names of the men, who shall divide the land for you: Eleazar the priest, and Joshua the son of Nun,
“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
18 and one leader from each tribe,
Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
19 whose names are these: from the tribe of Judah, Caleb the son of Jephunneh;
Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
20 from the tribe of Simeon, Samuel the son of Ammihud;
Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
21 from the tribe of Benjamin, Elidad the son of Chislon;
Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
22 from the tribe of the sons of Dan, Bukki the son of Jogli;
Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
23 of the sons of Joseph, from the tribe of Manasseh, Hanniel the son of Ephod;
Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
24 from the tribe of Ephraim, Kemuel the son of Shiphtan;
Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
25 from the tribe of Zebulon, Elizaphan the son of Parnach;
Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
26 from the tribe of Issachar, Paltiel the leader, the son of Azzan;
Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
27 from the tribe of Asher, Ahihud the son of Shelomi;
Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
28 from the tribe of Naphtali, Pedahel the son of Ammihud.”
Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
29 These are the ones that the Lord has ordered to divide the land of Canaan to the sons of Israel.
Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.

< Numbers 34 >