< Nehemiah 1 >

1 The words of Nehemiah, the son of Hacaliah. And it happened that, in the month of Chislev, in the twentieth year, I was in the capital city of Susa.
Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya: Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa,
2 And Hanani, one of my brothers, arrived, he and some men of Judah. And I questioned them about the Jews who had remained and were left behind from the captivity, and about Jerusalem.
Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.
3 And they said to me: “Those who have remained and have been left behind from the captivity, there in the province, are in great affliction and in disgrace. And the wall of Jerusalem has been broken apart, and its gates have been burned with fire.”
Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”
4 And when I had heard this manner of words, I sat down, and I wept and mourned for many days. I fasted and prayed before the face of the God of heaven.
Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba.
5 And I said: “I beg you, O Lord, God of heaven, strong, great, and terrible, who keeps covenant and mercy with those who love you and who keep your commandments:
Ndinkati: “Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu.
6 may your ears be attentive, and may your eyes be open, so that you may hear the prayer of your servant, which I am praying before you today, night and day, for the sons of Israel, your servants. And I am confessing the sins of the sons of Israel, which they have sinned against you. We have sinned, I and my father’s house.
Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani.
7 We have been seduced by vanity. And we have not kept your commandments and ceremonies and judgments, which you have instructed to your servant Moses.
Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.
8 Remember the word which you commanded to your servant Moses, saying: ‘When you will have transgressed, I will disperse you among the nations.
“Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina.
9 But if you will return to me, and keep my precepts, and do them, even if you will have been led away to the furthest reaches of the heavens, I will gather you from there, and I will lead you back to the place that I have chosen so that my name would dwell there.’
Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’
10 And these same are your servants and your people, whom you have redeemed by your great strength and by your powerful hand.
“Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
11 I beg you, O Lord, may your ear be attentive to the prayer of your servant, and to the prayer of your servants who are willing to fear your name. And so, guide your servant today, and grant to him mercy before this man.” For I was the cupbearer of the king.
Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.” Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.

< Nehemiah 1 >