< Leviticus 25 >
1 And the Lord spoke to Moses on mount Sinai, saying:
Yehova anawuza Mose pa phiri la Sinai kuti,
2 Speak to the sons of Israel, and you shall say to them: When you will have entered into the land which I will give to you, rest on the Sabbath of the Lord.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukadzalowa mʼdziko limene ndikukupatsani, nthakayo iyenera kumakasunga Sabata la Yehova.
3 For six years you shall sow your field, and for six years you shall care for your vineyard, and you shall gather its fruits.
Pa zaka zisanu ndi chimodzi muzikalima minda yanu, ndipo kwa zaka zisanu ndi chimodzi muzikasadza mitengo yanu ya mpesa ndi kuthyola zipatso zake.
4 But in the seventh year, there shall be a Sabbath of the land, a resting of the Lord. You shall not sow your field, and you shall not care for your vineyard.
Koma chaka chachisanu ndi chiwiri ndi chaka choti nthaka ipume, chaka cha Sabata la Yehova. Musalime mʼminda yanu kapena kusadza mitengo yanu ya mpesa.
5 What the soil shall spontaneously produce, you shall not harvest. And you shall not gather the grapes of the first-fruits as a crop. For it is a year of rest for the land.
Musakolole zimene zinamera zokha mʼmunda mwanu. Musakakolole kapena kuthyola mphesa za mʼmitengo imene simunasadze. Chaka chimenechi nʼchoti nthaka ipumule.
6 But these shall be yours for food, for you and for your men and women servants, and for your hired hands, and for the newcomers who sojourn with you:
Chaka chimene nthakayo ipumula mudzakhala ndi chakudya chokwanira inuyo, akapolo anu aamuna ndi aakazi, antchito ndi alendo okhala nanu.
7 all that grows on its own shall provide food for your beasts and cattle.
Ziweto zanu pamodzi ndi nyama za mʼdziko lanu zizidzadya zipatso za mʼnthaka.
8 You shall also number for yourselves seven weeks of years, that is, seven times seven, which together makes forty-nine years.
“‘Muzichotsera Masabata asanu ndi awiri a zaka, ndi kuchulukitsa zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawirinso kuti Masabata asanu ndi awiri a zakawo akwane zaka 49.
9 And you shall sound the trumpet in the seventh month, on the tenth day of the month, at the time of the atonement, throughout all your land.
Ndipo pa tsiku la khumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri mulize lipenga mofuwula. Tsiku lochita mwambo wopepesera machimo muziliza lipenga mʼdziko lanu lonse.
10 And you shall sanctify the fiftieth year, and you shall proclaim a remission for all the inhabitants of your land: for the same is the Jubilee. A man shall return to his possession, and each one shall go back to his original family,
Mupatule chaka cha makumi asanu, ndipo mulengeze kuti pakhale ufulu mʼdziko lonse kwa onse amene ali mʼmenemo. Kwa inu chakachi chidzakhala choyimba lipenga la chikondwerero. Aliyense wa inu adzayenera kubwerera pa munda wake, ndipo aliyense wa inu adzabwerera ku fuko lake.
11 for it is the Jubilee and the fiftieth year. You shall not sow, and you shall not reap what grows in the field of its own accord, and you shall not gather the first-fruits of the crop,
Kwa inu chakachi chidzakhaladi chaka choyimba lipenga kukondwerera zaka makumi asanu. Pa chaka chimenechi musadzale kanthu ndipo musakolole mbewu zomera zokha kapenanso kuthyola mphesa pa mitengo yosasadzira.
12 due to the sanctification of the Jubilee. But you shall eat them as they present themselves.
Chimenechi ndi chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Choncho chikhale chaka chopatulika kwa inu. Muzidya zokhazo zimene zakololedwa mʼminda.
13 In the year of the Jubilee, all shall return to their possessions.
“‘Chaka chimenechi ndi choliza lipenga, kukondwerera zaka makumi asanu, ndipo aliyense abwerere pa malo ake.
14 When you will sell anything to your fellow citizen, or buy anything from him, do not cause your brother grief, but buy from him according to the number of years from the Jubilee,
“‘Ngati unagulitsa kapena kugula malo ako kwa mnzako wa mʼdzikomo, pasakhale kuchenjeretsana.
15 and he shall sell to you according to the computation of the produce.
Ugule kwa mnzako potsata chiwerengero cha zaka zimene zatha kuyambira pa chikondwerero cha chaka cha makumi asanu chapita. Ndipo mnzakoyo akugulitse potsata chiwerengero cha zaka zokolola zomwe zatsala.
16 The more years that will remain after the Jubilee, the more the price shall increase, and the less the time is numbered, so much less shall the purchase price be. For he will sell to you the time for the produce.
Zaka zikakhala zochuluka, uwonjezere mtengo, ndipo zaka zikakhala zochepa, uchepetse mtengo, pakuti chimene iye akukugulitsa ndi zaka zokolola.
17 Do not be willing to afflict your countrymen, but let each one fear his God. For I am the Lord your God.
Musachenjeretsane koma muope Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
18 Accomplish my precepts, and observe my judgments, and complete them, so that you may be able to live in the land without any fear,
“‘Tsatirani malangizo anga ndipo mverani mosamala malamulo anga ndipo mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
19 and so that the soil may produce its fruits for you, from which you may eat, even to fullness, dreading violence by no one.
Ndipo nthaka idzakupatsani zipatso zake. Mudzadya mpaka kukhuta ndiponso mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
20 But if you will say: What shall we eat in the seventh year, if we do not sow and do not gather our produce?
Mwina nʼkafunsa kuti, ‘Kodi chaka chachisanu ndi chiwiri tidzadya chiyani ngati sitidzala kapena kukolola mbewu zathu?’
21 I will give my blessing to you in the sixth year, and it shall yield the produce of three years.
Ine ndidzatumiza madalitso ambiri chaka chachisanu ndi chimodzi moti nthaka yanu idzabala zinthu zokwanira kudya zaka zitatu.
22 And in the eighth year you shall sow, but you shall eat from the old produce, until the ninth year, until what is new matures, you shall eat what is old.
Pamene mukudzala chaka chachisanu ndi chitatu, muzidzadya chakudya chogonera ndipo mudzapitirira kudya mpaka nthawi yokolola mʼchaka chachisanu ndi chinayi.
23 Also, the land shall not be sold in perpetuity, for it is mine, and you are newcomers and settlers to me.
“‘Malo asagulitsidwe mpaka muyaya chifukwa dzikolo ndi langa. Inu ndinu alendo okhala ndi Ine.
24 Therefore, every region of your possession shall be sold under the condition of redemption.
Malo onse amene ali mʼmanja mwanu mudzalole kuti amene anakugulitsani awawombole.
25 If your brother, being in need, will have sold his little possession and his close relative is willing, he is able to redeem what he had sold.
“‘Ngati Mwisraeli mnzanu wasauka nagulitsako gawo lina la malo ake, mʼbale wake wapaphata abwere kudzawombola malo amene mʼbale wakeyo wagulitsa.
26 But if he has no near relative, and he himself is able to find the price to redeem it,
Koma ngati munthuyo alibe wachibale woti nʼkuwombola malowo koma pambuyo pake iye mwini nʼkulemera ndi kupeza zokwanira kuwombolera, awombole malowo.
27 the produce shall be calculated from that time when he sold it. And what is lacking, he shall repay to the buyer, and so he shall receive his possession.
Awerengerane zaka kuyambira pamene anagulitsa mundawo ndipo amubwezere amene anagulayo ndalama zimene akanayenera kuzipereka mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Atatero angathe kubwerera pa malo ake.
28 But if his hand will not have discovered a way to repay the price, the buyer shall have what he bought, until the year of the Jubilee. For in that year all that has been sold shall return to the owner, and to the original possessor.
Koma ngati sakhala nazo zokwanira kuti amubwezere amene anagula malowo, gawo limene anagulitsalo lidzakhala mʼmanja mwa munthu amene anagulayo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Malowo adzabwezedwa chaka chimenechi, ndipo iye adzatha kubwerera pa malo ake.
29 Whoever will have sold a house within the walls of a city shall have the freedom to redeem it, until one year has been completed.
“‘Ngati munthu agulitsa nyumba ya mu mzinda umene uli mu linga, angathe kuyiwombola nyumbayo chisanathe chaka chathunthu chigulitsire. Mu nthawi imeneyi wogulitsayo atha kuyiwombola.
30 If he has not redeemed it, and the year will have turned full circle, the buyer and his posterity shall possess it, in perpetuity, and it is not able to be redeemed, even in the Jubilee.
Ngati nyumbayo siwomboledwa chisanathe chaka chimodzicho, nyumbayo idzakhala ya amene anagulayo ndi zidzukulu zake mpaka muyaya. Sidzabwezedwanso kwa mwini wake mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu.
31 But if the house is in a village, which has no walls, it shall be sold by the law of the fields. If it has not been redeemed beforehand, then in the Jubilee it shall return to the owner.
Koma nyumba za mʼmizinda yosazingidwa ndi linga ziwomboledwe monga mmene achitira ndi minda ya mʼdzikomo.
32 The buildings of the Levites, which are in the cities, are always able to be redeemed.
“‘Alevi ali ndi ufulu owombola nyumba zawo za mʼmidzi yawo nthawi ina iliyonse.
33 If they have not been redeemed, then in the Jubilee they shall return to the owners, for the houses of the cities of the Levites are for their possession among the sons of Israel.
Koma ngati Mlevi sawombola nyumba imene inagulitsidwa mʼmudzi mwake, ndiye kuti idzabwezedwe mʼchaka choliza lipenga pokondwerera zaka makumi asanu, popeza nyumba zimenezi zili mʼmidzi ya Alevi ndi yawo pakati pa Aisraeli.
34 But let not their suburbs be sold, for it is an everlasting possession.
Koma malo owetera ziweto a mʼmidzi yawoyo sayenera kugulitsidwa. Awa ndi malo awo mpaka muyaya.
35 If your brother has become impoverished, or infirm of hand, and you take him in, like a newcomer or a sojourner, and he lives with you,
“‘Ngati mʼbale wako akhala wosauka kuti sangathe kudzisamalira yekha, umuthandize. Ukhale naye ngati mlendo kapena ngati munthu amene ukhala naye kwa kanthawi.
36 do not accept usury from him, nor anything more than what you gave. Fear your God, so that your brother may be able to live with you.
Usalandire chiwongoladzanja chilichonse kuchokera kwa iye kapena kuwonjezerapo kanthu kena, koma uziopa Mulungu kuti mʼbale wakoyo akhale nawe.
37 You shall not give him your money by usury, nor exact from him an overabundance of produce.
Musakongoze mnzanu ndalama kuti mulandire chiwongoladzanja, kapena kumugulitsa chakudya kuti mupeze phindu.
38 I am the Lord your God, who led you away from the land of Egypt, so that I might give to you the land of Canaan, and so that I may be your God.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikupatseni dziko la Kanaani ndi kuti ndikhale Mulungu wanu.
39 If your brother, having been compelled by poverty, will have sold himself to you, you shall not oppress him with the servitude of indentured servants.
“‘Ngati mʼbale wanu asauka ndipo adzigulitsa yekha kwa inu, musamugwiritse ntchito ngati kapolo.
40 But he shall be like a hired hand or a settler; he shall work with you, until the year of the Jubilee.
Akhale ngati wantchito kapena ngati mlendo. Akugwirireni ntchito mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu.
41 And after that, he shall depart with his children, and he shall return to his kindred, to the possession of his fathers.
Kenaka iye ndi ana ake achoke, ndipo apite ku fuko lake ndi kubwerera ku malo a makolo ake.
42 For these are my servants, and I led them away from the land of Egypt; let them not be sold into the condition of servitude.
Chifukwa Aisraeli ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto, asagulitsidwe ngati akapolo.
43 Do not afflict him by power, but be fearful of your God.
Musawalamulire mwankhanza koma wopani Mulungu wanu.
44 Let your male and female servants be from the nations which are all around you,
“‘Kunena za akapolo aamuna ndi aakazi, amenewa mungathe kuwagula kuchokera kwa mitundu ya anthu imene yakuzungulirani.
45 and from the newcomers who sojourn with you, or who have been born from them in your land. These you shall have as servants,
Mungathenso kugula akapolo kuchokera kwa alendo amene akukhala nanu kapena kuchokera ku mabanja amene mukukhala nawo amene ndi mbadwa za mʼdziko lanu. Iwowa akhoza kukhala akapolo anu.
46 and, by the right of inheritance, you shall transmit them to your posterity, and you shall possess them forever. But do not oppress your brothers, the sons of Israel, by power.
Akapolowo mungathe kuwasiya mʼmanja mwa ana anu inu mutafa kuti akhale cholowa chawo moyo wawo wonse. Koma musawalamulire mwankhanza Aisraeli anzanu.
47 If the hand of a newcomer or a sojourner will have grown strong among you, and your brother, having become impoverished, will have sold himself to him, or to any of his stock,
“‘Ngati mlendo kapena munthu amene akukhala nanu kwa kanthawi kochepa alemera ndipo mmodzi wa abale anu amene akukhala naye pafupi nʼkusauka, nadzigulitsa yekha kwa mlendo amene akukhala pakati panuyo kapena kwa mmodzi wa fuko la munthu wongokhala pafupi nayeyo,
48 after the sale, he is able to be redeemed. Whoever is willing among his brothers shall redeem him:
wodzigulitsayo ali ndi ufulu wowomboledwa. Mmodzi mwa abale ake angathe kumuwombola:
49 either the paternal uncle, or the paternal uncle’s son, or his close relative, by blood or by affinity. But if he himself will be able also, he shall redeem himself,
amalume ake kapena mwana wa amalume ake, kapena wachibale wa mu fuko lake. Kapena ngati iye mwini alemera, atha kudziwombola yekha.
50 considering only the years from the time of his selling until the year of the Jubilee, and calculating the money for which he was sold, according to the number of years and the accounting of a hired hand.
Iye pamodzi ndi munthu amene anamugulayo awerengerane kuyambira chaka chimene anadzigulitsa kwa iyeyo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Mtengo wodziwombolera ukhale wofanana ndi zakazo. Ndipo nthawi imene anali ndi mbuye wakeyo iwerengedwe ngati nthawi ya munthu wantchito.
51 If there will have been many years which remain until the Jubilee, according to these shall he also repay the price.
Ngati patsala zaka zambiri, iye ayenera kulipira mtengo woposera umene anamugulira.
52 If few, he shall determine the accounting with him according to the number of years, and he shall repay to the buyer by what is left remaining of the years;
Ngati kwatsala zaka zochepa kuti ifike nthawi ya chaka chokondwerera zaka makumi asanu, iye awerengerane ndi mbuye wake, ndipo apereke ndalama za zowomboledwera molingana ndi zaka zotsalazo.
53 his wages being charged by what served before. He shall not afflict him violently in your sight.
Azikhala naye ngati wantchito wolembedwa chaka ndi chaka. Ndipo muonetsetse kuti mbuye wakeyo sakumulamulira mwankhanza.
54 But if, by these means, he will not be able to be redeemed, then in the year of the Jubilee he shall depart with his children.
“‘Ngakhale munthuyo atapanda kuwomboledwa mwa njira zimenezi, iye ndi ana ake ayenera kumasulidwa mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu,
55 For they are my servants, the sons of Israel, whom I led away from the land of Egypt.
pakuti Aisraeli ndi atumiki anga. Iwo ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.