< Lamentations 5 >

1 Remember, O Lord, what has befallen us. Consider and look kindly upon our disgrace.
Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
2 Our inheritance has been turned over to foreigners; our houses to outsiders.
Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
3 We have become orphans without a father; our mothers are like widows.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
4 We paid for our drinking water. We acquired our wood for a price.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
5 We were dragged by our necks. Being weary, no rest was given to us.
Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
6 We have given our hand to Egypt and to the Assyrians, so that we may be satisfied with bread.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
7 Our fathers have sinned, and are not. And we have carried their iniquities.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
8 Servants have become rulers over us. There was no one to redeem us from their hand.
Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
9 We obtained our bread at the risk of our lives, before the face of the sword, in the wilderness.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 Our skin was burned, as if by an oven, before the face of the tempest of the famine.
Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 They humiliated the women in Zion and the virgins in the cities of Judah.
Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 The leaders were suspended by their hand. They were not ashamed before the faces of the elders.
Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
13 They have sexually abused the adolescents, and the children were corrupted in the wood.
Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 The elders have ceased from the gates, the youths from the choir of the psalms.
Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 The gladness of our heart has failed, our singing has been turned into mourning.
Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 The crown has fallen from our head. Woe to us, for we have sinned.
Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 Because of this, our heart became gloomy; for this reason, our eyes have been darkened:
Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 because of mount Zion, because it was ruined. Foxes have wandered upon it.
pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
19 But you, O Lord, shall remain for eternity, your throne from generation to generation.
Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Why would you forget us forever? Why would you forsake us for a long time?
Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 Convert us, O Lord, to you, and we shall be converted. Renew our days, as from the beginning.
Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 But you have utterly rejected us; you are vehemently angry against us.
pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.

< Lamentations 5 >