< Joel 2 >

1 Blow the trumpet in Zion, wail on my holy mountain, let all the inhabitants of the land be stirred up. For the day of the Lord is on its way; for it is near:
Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
2 a day of darkness and gloom, a day of clouds and whirlwinds. Like the morning reaching over the mountains, they are a numerous and strong people. Nothing like them has existed since the beginning, nor will exist after them, even in the years of generation upon generation.
tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
3 Before their face is a devouring fire, and behind them is a burning flame. The land before them is like a lush garden, and behind them is a desolate desert, and there is no one who can escape them.
Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
4 Their appearance is like the appearance of horses, and they will rush forward like horsemen.
Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
5 Like the sound of a four-horse chariot, they will leap over the tops of the mountains. Like the sound of a burning flame devouring stubble, they are as a strong people prepared for battle.
Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
6 Before their face, the people will be tortured; each one’s appearance will retreat, as if into a jar.
Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
7 They will rush forward, as if they were strong. Like valiant warriors, they will ascend the wall. The men will advance, each one on his own way, and they will not turn aside from their path.
Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
8 And each one will not hem in his brother; every one will walk in his own rough path. Moreover, they will drop through the breach and not be harmed.
Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
9 They will advance into the city; they will rush through the wall. They will scale the houses; they will go in through the windows, like a thief.
Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
10 Before their face, the earth has trembled, the heavens have been moved. The sun and moon have been obscured, and the stars have retracted their splendor.
Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
11 And the Lord has bestowed his voice before the face of his army. For its military camps are very numerous; for they are strong and they carry out his word. For the day of the Lord is great and so very terrible, and who can withstand it?
Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
12 Now, therefore, the Lord says: “Be converted to me with your whole heart, in fasting and weeping and mourning.”
“Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
13 And rend your hearts, and not your garments, and convert to the Lord your God. For he is gracious and merciful, patient and full of compassion, and steadfast despite ill will.
Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
14 Who knows if he might convert and forgive, and bequeath a blessing after him, a sacrifice and a libation to the Lord your God?
Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
15 Blow the trumpet in Zion, sanctify a fast, call an assembly.
Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
16 Gather the people, sanctify the church, unite the elders, gather together the little ones and infants at the breast. Let the bridegroom depart from his bed, and the bride from her bridal chamber.
Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
17 Between the vestibule and the altar, the priests, the ministers of the Lord, will weep, and they will say: “Spare, O Lord, spare your people. And do not bequeath your inheritance into disgrace, so that the nations would rule over them. Why should they say among the peoples, ‘Where is their God?’”
Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
18 The Lord has been zealous for his land, and he has spared his people.
Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
19 And the Lord responded, and he said to his people: “Behold, I will send you grain and wine and oil, and you will again be filled with them. And I will no longer give you disgrace among the Gentiles.
Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
20 And he who is from the North, I will drive far from you. And I will expel him into an impassable land, and into the desert, with his face opposite the Eastern sea, and his furthest part towards the furthest sea. And his stench will ascend, and his rottenness will ascend, because he has acted arrogantly.
“Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
21 Earth, do not be afraid. Exult and rejoice. For the Lord has great esteem for what he has done.
Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
22 Animals of the countryside, do not be afraid. For the beauty of the wilderness has sprung forth. For the tree has borne its fruit. The fig tree and the vine have bestowed their virtue.
Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
23 And you, sons of Zion, exult and rejoice in the Lord your God. For he has given you a teacher of justice, and he will make the early and the late rains descend to you, just as it was in the beginning.
Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
24 And the threshing floors will be filled with grain, and the presses will overflow with wine and oil.
Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
25 And I will repay you for the years which the locust, and the beetle, and the mildew, and the caterpillar consumed: my great strength which I sent upon you.
“Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
26 And you will eat with enjoyment, and you will be satisfied, and you will praise the name of the Lord your God, who has worked miracles with you, and my people will not be confounded forever.
Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
27 And you will know that I am in the midst of Israel, and I am the Lord your God, and there is no other, and my people will not be confounded forever.
Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
28 And after this, it will happen that I will pour out my spirit upon all flesh, and your sons and your daughters will prophesy; your elders will dream dreams, and your youths will see visions.
“Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
29 Moreover, in those days I will pour out my spirit upon my servants and handmaids.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
30 And I will grant wonders in the sky and on earth: blood and fire and the vapor of smoke.
Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
31 The sun will be turned into darkness, and the moon into blood, before the great and terrible day of the Lord shall arrive.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
32 And it will happen that everyone who will call upon the name of the Lord will be saved. For on Mount Zion, and in Jerusalem, and in the remnant whom the Lord will call, there will be salvation, just as the Lord has said.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.

< Joel 2 >