< Job 36 >

1 Continuing in a similar manner, Eliu had this to say:
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 Bear with me for a little while and I will show you; for I have still more to say in favor of God.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 I will review my knowledge from the beginning, and I will prove my Maker to be just.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 For truly my words are without any falsehood and perfect knowledge will be proven to you.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 God does not abandon the powerful, for he himself is also powerful.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 But he does not save the impious, though he grants judgment to the poor.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 He will not take his eyes away from the just, and he continually establishes kings on their throne, and they are exalted.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 And, if they are in captivity, or are bound with the chains of poverty,
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 he will reveal to them their works, as well as their sinfulness, in that they were violent.
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 Likewise, he will open their ears to his correction, and he will speak to them, so that they may return from iniquity.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 If they listen and obey, they will fill their days with goodness and complete their years in glory.
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 But if they will not listen, they will pass away by the sword and will be consumed by foolishness.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 The false and the crafty provoke the wrath of God, yet they do not cry out to him when they are chained.
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Their soul will die in a storm, and their life, among the unmanly.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 He will rescue the poor from his anguish, and he will open his ear during tribulation.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 Therefore, he will save you from the narrow mouth very widely, even though it has no foundation under it. Moreover, your respite at table will be full of fatness.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Your case has been judged like that of the impious; you will withdraw your plea and your judgment.
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Therefore, do not let anger overwhelm you so that you oppress another; neither should you allow a multitude of gifts to influence you.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Lay down your greatness without distress, and put aside all of your power with courage.
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Do not prolong the night, even if people rise on their behalf.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Be careful that you do not turn to iniquity; for, after your misery, you have begun to follow this.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 Behold, God is exalted in his strength, and there is no one like him among the law-givers.
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Who is able to investigate his ways? And who can say, “You have done iniquity,” to him?
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Remember that you are ignorant of his work, yet men have sung its praises.
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 All men consider him; and each one ponders from a distance.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 Behold, God is great, defeating our knowledge; the number of his years is inestimable.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 He carries away the drops of rain, and he sends forth showers like a raging whirlpool;
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 they flow from the clouds that are woven above everything.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 If he wills it, he extends the clouds as his tent
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 and shines with his light from above; likewise, he covers the oceans within his tent.
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 For he judges the people by these things, and he gives food to a multitude of mortals.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 Within his hands, he hides the light, and he commands it to come forth again.
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 He announces it to his friend, for it is his possession and he is able to reach out to it.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

< Job 36 >