< Job 33 >
1 Therefore, hear my speeches, Job, and listen to all my words.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 Behold, I have opened my mouth; let my tongue speak along with my throat.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 My words are from my simple heart, and my lips will speak a pure judgment.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 The Spirit of God made me, and the breath of the Almighty gave me life.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 If you can, answer me, and oppose me to my face.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Behold, God has made me, just as he also has made you, and I, likewise, have been formed of the same clay.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 So, truly, do not let my wonders terrify you, and do not let my eloquence be burdensome to you.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 For you have spoken in my hearing, and I have heard the voice of your words, saying:
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 “I am clean and without sin; I am immaculate, and there is no iniquity in me.
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Yet he has discovered blame in me, and so he has treated me like his enemy.
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 He has put my feet in fetters; he has kept watch over all my ways.”
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 Therefore, it is for this reason that you have not been justified. For I tell you that God is greater than man.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Do you contend against him because he has not responded to all of your words?
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 God speaks once, and he does not repeat the same thing a second time.
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 Through a dream in a vision of the night, when a deep sleep falls over men, and they are sleeping in their beds,
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 then, he opens the ears of men, and, educating them, he teaches discipline,
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 so that he may divert a man from the things that he is doing, and may free him from pride,
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 rescuing his soul from corruption and his life from passing away by the sword.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 Likewise, he rebukes by sorrow in bed, and he causes all of his bones to become weak.
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 Bread becomes abominable to him in his life, and, to his soul, the meat which before he desired.
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 His body will waste away, and his bones, which had been covered, will be revealed.
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 His soul has approached corruption, and his life has drawn near to what is deadly.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 If there were an angel speaking for him, one among thousands, to declare the fairness of the man,
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 he will have mercy on him, and he will say, “Free him, so that he will not descend to destruction. I have found a reason to be favorable to him.
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 His body is consumed by suffering. Let him return to the days of his youth.”
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 He will beg pardon from God, and he will be soothing to him; and he will look upon his face in jubilation, and he will restore his justice to man.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 He will consider mankind, and he will say: “I have sinned and truly I have offended, yet I was not treated as I deserved.”
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 He has freed his soul from continuing into destruction, so that, in living, it may see the light.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 Behold, all these things God works three times within each one,
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 so that he may revive their souls from corruption and enlighten them with the light of life.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Pay attention Job, and listen to me; and remain silent, while I speak.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Yet, if you have anything to say, answer me and speak, for I want you to be treated justly.
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 But if you do not have anything to say, then listen to me. Be quiet and I will teach you wisdom.
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”