< Isaiah 54 >
1 Give praise, you who are barren and unable to conceive. Sing praise and make a joyful noise, you who have not given birth. For many are the children of the desolate, more so than of her who has a husband, says the Lord.
“Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
2 Enlarge the place of your tent and extend the skins of your tabernacles, unsparingly. Lengthen your cords, and strengthen your stakes.
Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
3 For you shall extend to the right and to the left. And your offspring shall inherit the nations, and you shall inhabit the desolate cities.
Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
4 Do not be afraid! For you will not be confounded, and you will not blush. And you will not be put to shame, because you shall forget the confusion of your youth, and you shall no longer remember the disgrace of your widowhood.
“Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
5 For the One who made you will rule over you. The Lord of hosts is his name. And your Redeemer, the Holy One of Israel, will be called the God of all the earth.
Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
6 For the Lord has called you, like a woman forsaken and mourning in spirit, and like a wife rejected in her youth, said your God.
Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
7 For a brief moment, I have forsaken you, and with great pities, I will gather you.
“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
8 In a moment of indignation, I have hidden my face from you, for a little while. But with everlasting mercy, I have taken pity on you, said your Redeemer, the Lord.
Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
9 For me, it is just as in the days of Noah, to whom I swore that I would no longer bring in the waters of Noah over the earth. Thus have I sworn not to be angry with you, and not to rebuke you.
“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
10 For the mountains will be moved, and the hills will tremble. But my mercy will not depart from you, and the covenant of my peace will not be shaken, said the Lord, who has compassion on you.
Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
11 O poor little ones, convulsed by the tempest, away from any consolation! Behold, I will set your stones in order, and I will lay your foundation with sapphires,
“Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
12 and I will make your ramparts out of jasper, and your gates out of sculpted stones, and all your borders out of desirable stones.
Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
13 All your children will be taught by the Lord. And great will be the peace of your children.
Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
14 And you will be founded in justice. Depart far from oppression, for you will not be afraid. And depart from terror, for it will not approach you.
Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
15 Behold, a settler will arrive, who was not with me, a certain new arrival will be joined to you.
Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
16 Behold, I created the smith who fans the coals of the fire and produces an object by his work, and I have created the slayer who destroys.
“Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
17 No object which has been formed to use against you will succeed. And every tongue that resists you in judgment, you shall judge. This is the inheritance of the servants of the Lord, and this is their justice with me, says the Lord.
palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.