< Isaiah 31 >
1 Woe to those who descend into Egypt for assistance, hoping in horses, and putting their trust in four-horse chariots because they are many, and in horsemen because they are exceedingly strong. And they have not believed in the Holy One of Israel, and they have not sought the Lord.
Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
2 Therefore, being wise, he has permitted harm, and he has not removed his words, and he will rise up against the house of the wicked and against those who assist the workers of iniquity.
Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
3 Egypt is man, and not God. And their horses are flesh, and not spirit. And so, the Lord will reach down his hand, and the helper will fall, and the one who was being helped will fall, and they will all be consumed together.
Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
4 For the Lord says this to me: In the same way that a lion roars, and a young lion is over his prey, and though a multitude of shepherds may meet him, he will not dread their voice, nor be afraid of their number, so will the Lord of hosts descend in order to battle upon mount Zion and upon its hill.
Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
5 Like birds flying, so will the Lord of hosts protect Jerusalem, protecting and freeing, passing over and saving.
Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
6 Be converted to the same depth that you have drawn away, O sons of Israel.
Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
7 For in that day, a man will cast away his idols of silver and his idols of gold, which your hands have made for you unto sin.
Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
8 And Assur will fall by a sword not of man, and a sword not of man will devour him. And he will not flee from the face of the sword, and his young men will be subject to a penalty.
“Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
9 And his strength will pass away in terror, and his princes will flee in fear. The Lord has said it. His fire is in Zion, and his furnace is at Jerusalem.
Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.