< Isaiah 11 >

1 And a rod will go forth from the root of Jesse, and a flower will ascend from his root.
Padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese ndipo nthambi idzaphukira kuchokera ku mizu yake.
2 And the Spirit of the Lord will rest upon him: the spirit of wisdom and understanding, the spirit of counsel and fortitude, the spirit of knowledge and piety.
Mzimu wa Yehova udzakhala pa iye Mzimu wanzeru ndi wa kumvetsa zinthu, Mzimu wauphungu ndi wamphamvu, Mzimu wachidziwitso ndi wakuopa Yehova.
3 And he will be filled with the spirit of the fear of the Lord. He will not judge according to the sight of the eyes, nor reprove according to the hearing of the ears.
Ndipo kuopa Yehova ndiye chidzakhale chinthu chomukondweretsa. Iye sadzaweruza potsata zooneka pamaso, kapena kugamula mlandu potsata zakumva;
4 Instead, he will judge the poor with justice, and he will reprove the meek of the earth with fairness. And he will strike the earth with the rod of his mouth, and he will slay the impious with the spirit of his lips.
koma amphawi adzawaweruza mwachilungamo, adzaweruza mwachilungamo mlandu wa anthu osauka a dziko lapansi. Iye adzakantha dziko lapansi ndi mawu ake; atalamula Iyeyu anthu oyipa adzaphedwa.
5 And justice will be the belt around his waist. And faith will be the warrior’s belt at his side.
Chilungamo chidzakhala ngati lamba wake ndipo kukhulupirika kudzakhala ngati chomangira mʼchiwuno mwake.
6 The wolf will dwell with the lamb; and the leopard will lie down with the kid; the calf and the lion and the sheep will abide together; and a little boy will drive them.
Mʼmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa, kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwana wambuzi, mwana wangʼombe ndi mwana wa mkango adzadyera limodzi ndipo mwana wamngʼono adzaziweta.
7 The calf and the bear will feed together; their young ones will rest together. And the lion will eat straw like the ox.
Ngʼombe yayikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi, ana awo adzagona pamodzi, ndipo mkango udzadya udzu ngati ngʼombe.
8 And a breastfeeding infant will play above the lair of the asp. And a child who has been weaned will thrust his hand into the den of the king snake.
Mwana wakhanda adzasewera pa dzenje la mamba, ndipo mwana wamngʼono adzapisa dzanja lake ku phanga la mphiri osalumidwa.
9 They will not harm, and they will not kill, on all my holy mountain. For the earth has been filled with the knowledge of the Lord, like the waters covering the sea.
Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena chowononga pa phiri lopatulika la Yehova, pakuti anthu a dziko lapansi adzadzaza ndi nzeru yotha kudziwa Yehova monga momwe nyanja imadzazira ndi madzi.
10 In that day, the root of Jesse, who stands as a sign among the people, the same the Gentiles shall beseech, and his sepulcher will be glorious.
Tsiku limenelo mfumu yatsopano yochokera pa Muzu wa Yese idzakhala ngati chizindikiro kwa anthu a mitundu yonse. Mitundu ya anthu idzasonkhana kwa Iye, ndipo malo awo okhalapo adzakhala aulemerero.
11 And this shall be in that day: the Lord will send forth his hand a second time to take possession of the remnant of his people who will be left behind: from Assyria, and from Egypt, and from Pathros, and from Ethiopia, and from Elam, and from Shinar, and from Hamath, and from the islands of the sea.
Tsiku limenelo Ambuye adzatambasula dzanja lake kachiwiri kuti awombole anthu ake otsalira ku Asiriya, ku Igupto, ku Patirosi, Kusi, ku Elamu, ku Sinana, ku Hamati ndi pa zilumba za nyanja yamchere.
12 And he will lift up a sign to the nations, and he will gather together the fugitives of Israel, and he will collect the dispersed of Judah from the four regions of the earth.
Adzakwezera mitundu ya anthu mbendera, ndipo adzasonkhanitsa otayika a ku Israeli; Iye adzasonkhanitsa anthu obalalika a ku Yuda kuchokera ku mbali zonse zinayi za dziko lapansi.
13 And the envy of Ephraim will be taken away, and the enemies of Judah will perish. Ephraim will not be a rival to Judah, and Judah will not fight against Ephraim.
Nsanje ya Efereimu idzatha, ndipo adani a Yuda adzatha; Efereimu sadzachitira nsanje Yuda, ngakhale Yuda sadzamuda Efereimu.
14 And they will fly upon the shoulders of the Philistines through the sea; together they will plunder the sons of the east. Idumea and Moab will be under the rule of their hand, and the sons of Ammon will be obedient.
Yuda ndi Efereimu adzathira nkhondo pa Afilisti mbali ya kumadzulo; ndipo onsewo pamodzi adzalanda zinthu za anthu a kummawa. Adzalimbana ndi Edomu ndi Mowabu, ndipo Aamoni adzawagonjera.
15 And the Lord will desolate the tongue of the sea of Egypt. And he will lift up his hand over the river, with the strength of his Spirit; and he will strike it, in its seven streams, so that they may cross through it in their shoes.
Yehova adzaphwetsa mwendo wa nyanja ya Igupto; adzatambasula dzanja lake ndipo adzawombetsa mphepo yotentha pa mtsinje wa Yufurate. Iye adzawugawa mtsinjewo kukhala timitsinje tisanu ndi tiwiri kuti anthu athe kuwoloka powuma atavala nsapato.
16 And there will be a way for the remnant of my people, who will be left behind by the Assyrians: just as there was for Israel in the day that he ascended from the land of Egypt.
Padzakhala msewu waukulu woti ayendepo anthu ake otsalira amene anatsalira ku Asiriya, monga mmene panali msewu waukulu woyendapo Israeli pamene amachokera ku Igupto.

< Isaiah 11 >