< Hosea 5 >

1 Hear this, priests, and pay attention, house of Israel, and listen closely, house of the king. For there is a judgment against you, because you have become a trap for those you watched over, and a net stretched out over Tabor.
“Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
2 And you have led astray victims into the depths, though I am the teacher of them all.
Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
3 I know Ephraim, and Israel has not been hidden from me, yet now Ephraim has committed fornication, and Israel has been contaminated.
Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
4 They will not set their thoughts to return to their God, for the spirit of fornication is in the midst of them, and they have not known the Lord.
“Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
5 And the arrogance of Israel will answer to his face. And Israel and Ephraim will fall in their iniquity, and even Judah will fall with them.
Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
6 With their flocks and their herds, they will go to seek the Lord, and they will not find him. He has taken himself away from them.
Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
7 They have sinned against the Lord. For they have conceived sons that are strangers. Now one month will devour them with all their own.
Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
8 Sound the bugle in Gibeah, the trumpet in Ramah. Shout in Bethaven, behind your back, O Benjamin.
“Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
9 Ephraim will be in desolation on the day of correction, for within the tribes of Israel, I have revealed faith.
Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
10 The leaders of Judah have become like those who assume the end. I will pour my wrath over them like water.
Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
11 Ephraim has been enduring malicious slander and broken judgment, because he began to go after filth.
Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
12 And I will be like a moth to Ephraim, and like decay to the house of Judah.
Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
13 And Ephraim saw his own weakness, and Judah his chains. And Ephraim went to Assur, and he sent to the Avenging king. But he will not be able to heal you, nor is he able to release you from your chains.
“Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
14 For I will be like a lioness to Ephraim, and like a lion’s offspring to the house of Judah. I myself will seize and go forth. I will take away, and there is no one who can rescue.
Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
15 I will go and return to my place, until you shall grow faint and seek my face.
Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”

< Hosea 5 >