< Genesis 20 >

1 Abraham advanced from there into the southern land, and he lived between Kadesh and Shur. And he sojourned in Gerar.
Abrahamu anachokako kumeneko napita ku Negevi ndipo anakakhala ku dziko la Gerari, limene lili pakati pa mzinda wa Kadesi ndi mzinda wa Suri. Anakhala ku Gerari kwa kanthawi,
2 And he said about his wife Sarah: “She is my sister.” Therefore, Abimelech, the king of Gerar, sent for her and took her.
ndipo Abrahamu ankawawuza za Sara kuti, “Iyeyu ndi mlongo wanga.” Choncho Abimeleki, mfumu wa ku Gerari anamutenga Sara uja.
3 Then God came to Abimelech through a dream in the night, and he said to him: “Lo, you shall die because of the woman that you have taken. For she has a husband.”
Koma usiku, Mulungu anafika kwa Abimeleki kutulo nati, “Ufatu iwe chifukwa cha mkazi amene watengayu popeza ndi wokwatiwa.”
4 In truth, Abimelech had not touched her, and so he said: “Lord, would you put to death a people, ignorant and just?
Nthawi imeneyi nʼkuti Abimeleki asanamukhudze mkaziyo, kotero kuti anati, “Ambuye, kodi mudzawonongadi mtundu wolungama?
5 Did he not say to me, ‘She is my sister,’ and did she not say, ‘He is my brother?’ In the sincerity of my heart and the purity of my hands, I have done this.”
Kodi Abrahamu sanandiwuze kuti iyeyu ndi mlongo wake? Ndiponso mkaziyu ankanena kuti Abrahamu ndi mlongo wake. Choncho ine pochita izi, ndinkachita moona mtima ndiponso mopanda chinyengo.”
6 And God said to him: “And I know that you have acted with a sincere heart. And therefore I kept you from sinning against me, and I did not release you to touch her.
Tsono kumaloto komweko Mulungu anati kwa iye, “Inde ndikudziwa kuti wachita izi moona mtima, ndipo Ine sindinafune kuti undichimwire. Nʼchifukwa chake sindinakulole kuti umukhudze.
7 Now therefore, return his wife to the man, for he is a prophet. And he will pray for you, and you will live. But if you are not willing to return her, know this: you shall die a death, you and all that is yours.”
Tsopano kabwezere mkaziyo kwa mwamuna wake. Iyeyu ndi mneneri, ndipo adzakupempherera kuti ukhale ndi moyo. Koma ukapanda kukamupereka, udziwiretu kuti udzafa pamodzi ndi onse a pa banja pako.”
8 And immediately Abimelech, rising up in the night, called all his servants. And he spoke all these words in their hearing, and all the men were very afraid.
Mmamawa mwake Abimeleki anayitanitsa akuluakulu ake onse, ndipo atawafotokozera zimene zinachitika, iwo aja anachita mantha kwambiri.
9 Then Abimelech called also for Abraham, and he said to him: “What have you done to us? How have we sinned against you, so that you would bring so great a sin upon me and upon my kingdom? You have done to us what you ought not to have done.”
Kenaka Abimeleki anayitana Abrahamu ndipo anati, “Kodi wachita chiyani? Ndakulakwira chiyani kuti undibweretsere ine pamodzi ndi anthu anga chilango chachikulu chotere? Wandichitira zinthu zimene sizinayenera kuchitika.”
10 And remonstrating him again, he said, “What did you see, so that you would do this?”
Ndipo Abrahamu anafunsa Abimeleki kuti, “Chifukwa chiyani wachita zimenezi?”
11 Abraham responded: “I thought to myself, saying: Perhaps there is no fear of God in this place. And they will put me to death because of my wife.
Abrahamu anayankha nati, “Ndinkaganiza kuti kuno kulibiretu munthu woopa Mulungu. Ndiye ndimati mwina adzandipha chifukwa cha mkazi wanga.
12 Yet, in another way, she is also truly my sister, the daughter of my father, and not the daughter of my mother, and I took her as a wife.
Komabe kunena zoona, iyeyu ndi mlongo wangadi, mwana wamkazi wa abambo anga ngakhale kuti si ife a mayi mmodzi. Tsono akhoza kukhala mkazi wanga.
13 Then, after God led me out of my father’s house, I said to her: ‘You will show this mercy to me. In every place, to which we will travel, you will say that I am your brother.’”
Ndiye pamene Mulungu anati ndichoke ku nyumba ya abambo anga, ndinawuza mkazi wangayu kuti, ‘Kuti uwonetse kuti ndiwe mkazi wokoma mtima, uziwuza anthu kulikonse kumene tingapite kuti ndine mlongo wako.’”
14 Therefore, Abimelech took sheep and oxen, and men servants and women servants, and he gave them to Abraham. And he returned his wife Sarah to him.
Tsono Abimeleki anapereka nkhosa, ngʼombe ndi antchito aamuna ndi aakazi kwa Abrahamu. Ndipo anamubwezeranso Abrahamu Sara, mkazi wake.
15 And he said, “The land is in your sight. Dwell wherever it will please you.”
Tsono Abimeleki anati kwa Abrahamu, “Dziko langa ndi limene ukulionali; ukhale paliponse pamene ufuna.”
16 Then to Sarah he said: “Behold, I have given your brother one thousand silver coins. This will be for you as a veil for your eyes, to all who are with you and wherever you will travel. And so, remember that you were taken.”
Ndipo kwa Sara, iye anati, “Ndikumupatsa mlongo wakoyu makilogalamu khumi ndi awiri a siliva kutsimikiza kuti iwe ndi wosalakwa pamaso pa onse amene ali ndi iwe; ulibedi mlandu.”
17 Then when Abraham prayed, God healed Abimelech and his wife, and his handmaids, and they gave birth.
Tsono Abrahamu anapemphera kwa Mulungu ndipo Mulunguyo anachiritsa Abimeleki, mkazi wake pamodzi ndi adzakazi ake kuti athenso kubereka ana.
18 For the Lord had closed every womb of the house of Abimelech, because of Sarah, the wife of Abraham.
Paja Yehova nʼkuti atatseka akazi onse a mʼbanja la Abimeleki kuti asabereke ana chifukwa cha Sara, mkazi wa Abrahamu.

< Genesis 20 >