< Ezra 8 >
1 And so these are the leaders of the families, with their genealogy, of those who ascended with me from Babylon, during the reign of king Artaxerxes.
Nawa mayina a atsogoleri a mabanja amene anabwera nane kuchokera ku Babuloni nthawi ya ulamuliro wa mfumu Aritasasita:
2 From the sons of Phinehas, Gershom. From the sons of Ithamar, Daniel. From the sons of David, Hattush.
Geresomu wa fuko la Finehasi; Danieli wa fuko la Itamara; Hatusi
3 From the sons of Shecaniah, the son of Parosh, Zechariah, and one hundred fifty men were numbered with him.
mwana wa Sekaniya wa fuko la Davide; Zekariya wa fuko la Parosi. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwa anthu ena 150;
4 From the sons of Pahath-moab, Eliehoenai, the son of Zerahiah, and two hundred men were with him.
Elihunai mwana wa Zerahiya, wa fuko la Pahati-Mowabu. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu ena 400.
5 From the sons of Shecaniah, the son of Jahaziel, and three hundred men were with him.
Sekaniya, mwana wa Yahazieli wa fuko la Zatu. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwanso anthu 300.
6 From the sons of Adin, Ebed, the son of Jonathan, and fifty men were with him.
Ebedi, mwana wa Yonatani wa fuko la Adini. Pamodzi naye analembedwanso anthu ena makumi asanu.
7 From the sons of Elam, Jeshaiah, the son of Athaliah, and seventy men were with him.
Yesaiya, mwana wa Ataliya wa fuko la Elamu. Pamodzi naye panali anthu ena 70.
8 From the sons of Shephatiah, Zebadiah, the son of Michael, and eighty men were with him.
Zebadiya, mwana wa Mikayeli wa fuko la Sefatiya. Pamodzi naye panalinso anthu 80.
9 From the sons of Joab, Obadiah, the son of Jehiel, and two hundred eighteen men were with him.
Obadiya, mwana wa Yehieli wa fuko la Yowabu. Pamodzi naye panalinso anthu 218.
10 From the sons of Shelomith, the son of Josiphiah, and one hundred sixty men were with him.
Selomiti mwana wa Yosifiya wa fuko la Bani. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu 160.
11 From the sons of Bebai, Zechariah, the son of Bebai, and twenty-eight men were with him.
Zekariya, mwana wa Bebai wa fuko la Babai. Pamodzi naye analembedwanso anthu 28.
12 From the sons of Azgad, Johanan, the son of Hakkatan, and one hundred and ten men were with him.
Yohanani, mwana wa Hakatani wa fuko la Azigadi. Pamodzi naye panalinso anthu 110.
13 From the sons of Adonikam, who were the last, and these were their names: Eliphelet, and Jeuel, and Shemaiah, and sixty men were with them.
Atsogoleri a fuko la Adonikamu, anthu amene anabwera pambuyo pake mayina awo anali Elifeleti, Yeiyeli ndi Semaya. Pamodzi ndi iwowa panalinso anthu 60.
14 From the sons of Bigvai, Uthai and Zaccur, and seventy men were with them.
Atsogoleri a fuko la Bigivai anali Utai ndi Zakuri. Pamodzi ndi iwowa panali anthu 70.
15 Now I gathered them together at the river that runs down to Ahava, and we stayed there for three days. And I sought among the people and among the priests for the sons of Levi, and I found none there.
Anthu onse ndinawasonkhanitsa ku mtsinje umene umapita mpaka ku Ahava, ndipo kumeneko tinagona mʼmisasa masiku atatu. Nditayangʼana pakati pa anthu ndi ansembe, ndinapeza kuti panalibe Alevi.
16 And so I sent Eliezer, and Ariel, and Shemaiah, and Elnathan, and Jarib, and another Elnathan, and Nathan, and Zechariah, and Meshullam, who were leaders, and Joiarib and Elnathan, who were wise.
Choncho ndinayitana atsogoleri awa: Eliezara, Arieli, Semaiya, Elinatani, Yaribu, Elinatani, Natani, Zekariya ndi Mesulamu, pamodzi ndi aphunzitsi awiri, Yoyaribu ndi Elinatani,
17 And I sent them to Iddo, who is first within the place of Casiphia. And I placed in their mouth the words that they should speak to Iddo and his brothers, the temple servants, in the place of Casiphia, so that they would lead to us ministers for the house of our God.
ndipo ndinawatuma kwa Ido, mtsogoleri wa malo otchedwa Kasifiya. Ine ndinawawuza zoti akanene kwa Ido ndi kwa abale ake, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ku Kasifiyako, kuti atitumizire anthu odzatumikira ku Nyumba ya Mulungu.
18 And because the good hand of our God was over us, they led to us a very learned man from the sons of Mahli, the son of Levi, the son of Israel, with Sherebiah, and his sons, and his eighteen brothers,
Chifukwa cha kutikomera mtima kwa Mulungu wathu, Ido anatitumizira munthu wanzeru, Serabiya, wa fuko la Mahili, mwana wa Levi, mwana wa Israeli, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi abale ake, anthu 18.
19 and Hashabiah, and with him Jeshaiah, of the sons of Merari, and his brothers, and his sons, numbering twenty.
Anatitumiziranso Hasabiya ndi Yesaiya wa fuko la Merari pamodzi ndi abale ake ndi adzukulu ake, anthu makumi awiri.
20 And from the temple servants, whom David, and the leaders had provided for the ministry of the Levites, there were two hundred twenty temple servants. All these were called by their names.
Panalinso anthu ena 220 mwa anthu ogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amene Davide ndi nduna zake anawasankha kuti azitumikira Alevi. Anthu onsewa analembedwa potsata mayina awo.
21 And I proclaimed a fast in that place, beside the river Ahava, so that we might afflict ourselves in the sight of the Lord our God, and so that we might request of him the right way for us, and for our sons, and for all our substance.
Ku mtsinje wa Ahava, ndinalengeza kuti anthu onse asale zakudya, adzichepetse pamaso pa Mulungu wathu ndi kupempha kuti atiyendetse bwino ife ndi ana athu, ndi kuteteza katundu wathu yense.
22 For I was ashamed to petition the king for assistance and for horsemen, who would defend us from the enemy along the way. For we had said to the king: “The hand of our God is over all those who seek him in goodness. And his authority, and his strength and fury, is over all those who forsake him.”
Ine ndinali ndi manyazi kupempha mfumu kuti atipatse asilikali oyenda pansi ndi ena okwera pa akavalo kuti atiteteze kwa adani athu pa ulendo wathuwu popeza tinali titawuza kale mfumu kuti “Yehova amateteza aliyense amene amamudalira, koma amakwiyira onse amene amamukana.”
23 And so we fasted and begged our God for this; and as a result, we prospered.
Choncho tinasala zakudya ndi kupemphera kwa Mulungu wathu kuti atiteteze ndipo Iye anamva pemphero lathu.
24 And I separated twelve from among the leaders of the priests: Sherebiah, and Hashabiah, and with them ten of their brothers.
Tsono ndinasankha atsogoleri a ansembe khumi ndi awiri awa, Serebiya, Hasabiya ndi abale awo khumi
25 And I weighed out to them the silver and the gold, and the vessels consecrated to the house of our God, which had been offered by the king, and by his counselors and his leaders, and by all those of Israel who had been found.
ndipo ndinawayezera siliva ndi golide, ndiponso ziwiya ndi zopereka za ku Nyumba ya Mulungu wathu zimene mfumu ndi alangizi ake, nduna zake ndi Aisraeli onse amene anali kumeneko anazipereka.
26 And I weighed out to their hands six hundred fifty talents of silver, and one hundred vessels of silver, and one hundred talents of gold,
Nditayeza zonse, ndinapereka mʼmanja mwawo, matani 22 asiliva, ziwiya zasiliva zolemera makilogalamu 70, ndiponso makilogalamu 3,400 a golide,
27 and twenty gold bowls which had the weight of one thousand coins, and two vessels of the finest shining brass, as beautiful as gold.
mbale zagolide makumi awiri zolemera makilogalamu asanu ndi atatu ndi theka ndiponso ziwiya ziwiri zamkuwa wosalala, wonyezimira bwino ngati golide wamtengowapatali.
28 And I said to them: “You are the holy ones of the Lord, and the vessels are holy, with the silver and the gold, which has been offered freely to the Lord, the God of our fathers.
Kenaka ndinawawuza kuti, “Inu ndi opatulika a Yehova, ndiponso mphatso zonsezi ndi zopatulika. Siliva ndi golideyu ndi zopereka zaufulu kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu.
29 Watch and guard them, until you weigh them out before the leaders of the priests and the Levites, and the rulers of the families of Israel in Jerusalem, into the treasury of the house of the Lord.”
Muzisamale bwino mpaka mutaziyeza pamaso pa atsogoleri a ansembe ndi Alevi ndi akulu a mabanja a Israeli mʼzipinda za mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu.”
30 Then the priests and the Levites received the weight of the silver, and the gold, and the vessels, so that they might carry these to Jerusalem, into the house of our God.
Choncho ansembe ndi Alevi analandira zonse zoyezedwa zija, siliva, golide pamodzi ndi ziwiya kuti apite nazo ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu.
31 Therefore, we set out from the river Ahava, on the twelfth day of the first month, so that we might travel to Jerusalem. And the hand of our God was over us, and he freed us from the hand of the enemy and of those who lay in ambush along the way.
Pa tsiku la khumi ndi chiwiri la mwezi woyamba, tinachoka ku mtsinje wa Ahava kupita ku Yerusalemu. Ndipo Mulungu wathu anali nafe, ndipo anatiteteza kwa adani athu makamaka otibisalira pa njira.
32 And we arrived at Jerusalem, and we stayed there for three days.
Tinafika ku Yerusalemu, komwe tinapumula masiku atatu.
33 Then, on the fourth day, the silver and the gold and the vessels were weighed out in the house of our God, by the hand of Meremoth, the son of Uriah, the priest; and with him was Eleazar, the son of Phinehas, and with them were the Levites, Jozabad, the son of Jeshua, and Noadiah, the son of Binnui.
Pa tsiku la chinayi lake, mʼNyumba ya Mulungu wathu, tinayeza siliva ndi golide ndi ziwiya zija nʼkuzipereka mʼmanja mwa Meremoti mwana wa wansembe Uriya. Pamodzi ndi iyeyo panali Eliezara mwana wa Finehasi ndiponso Alevi awa: Yozabadi mwana wa Yesuwa ndi Nowadiya mwana wa Binuyi.
34 This was done according to the number and weight of everything; and every weight was written down at that time.
Zonsezi anaziwerenga ndi kuziyeza ndipo analemba kulemera kwa chinthu chilichonse.
35 Moreover, those who came from the captivity, the sons of the transmigration, offered holocausts to the God of Israel: twelve calves on behalf of all the people of Israel, ninety-six rams, seventy-seven lambs, and twelve he-goats for sin. All these were a holocaust to the Lord.
Pamenepo anthu amene anatengedwa ukapolo aja anabwerera, anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu wa Israeli: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, kuperekera Aisraeli onse, nkhosa zazimuna 96, ana ankhosa 77, ndiponso mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri ngati nsembe yopepesera machimo. Zonsezi zinali nsembe yopsereza zopereka kwa Yehova.
36 Then they gave the edicts of the king to the rulers who served in the sight of the king, and to the governors beyond the river, and they exalted the people and the house of God.
Iwo anaperekanso chidziwitso cha mfumu chija kwa akuluakulu a mfumu ndi kwa akazembe a mʼdera la Patsidya pa Yufurate. Pamenepo iwo anathandiza Ayuda ndiponso ntchito za pa Nyumba ya Mulungu.