< Ecclesiastes 9 >

1 I have drawn all these things through my heart, so that I might carefully understand. There are just men as well as wise men, and their works are in the hand of God. And yet a man does not know so much as whether he is worthy of love or of hatred.
Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani.
2 But all things in the future remain uncertain, because all things happen equally to the just and to the impious, to the good and to the bad, to the pure and to the impure, to those who offer sacrifices and to those who despise sacrifices. As the good are, so also are sinners. As those who commit perjury are, so also are those who swear to the truth.
Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe. Zomwe zimachitikira munthu wabwino, zimachitikiranso munthu wochimwa, zomwe zimachitikira amene amalumbira, zimachitikiranso amene amaopa kulumbira.
3 This is a very great burden among all things that are done under the sun: that the same things happen to everyone. And when the hearts of the sons of men are filled with malice and contempt in their lives, afterwards they shall be dragged down to hell. (questioned)
Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa.
4 There is no one who lives forever, or who even has confidence in this regard. A living dog is better than a dead lion.
Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa!
5 For the living know that they themselves will die, yet truly the dead know nothing anymore, nor do they have any recompense. For the memory of them is forgotten.
Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa, koma akufa sadziwa kanthu; alibe mphotho ina yowonjezera, ndipo palibe amene amawakumbukira.
6 Likewise, love and hatred and envy have all perished together, nor have they any place in this age and in the work which is done under the sun.
Chikondi chawo, chidani chawo ndiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale; sadzakhalanso ndi gawo pa zonse zochitika pansi pano.
7 So then, go and eat your bread with rejoicing, and drink your wine with gladness. For your works are pleasing to God.
Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako.
8 Let your garments be white at all times, and let not oil be absent from your head.
Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse.
9 Enjoy life with the wife whom you love, all the days of your uncertain life which have been given to you under the sun, during all the time of your vanity. For this is your portion in life and in your labor, with which you labor under the sun.
Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano.
10 Whatever your hand is able to do, do it earnestly. For neither work, nor reason, nor wisdom, nor knowledge will exist in death, toward which you are hurrying. (Sheol h7585)
Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru. (Sheol h7585)
11 I turned myself toward another thing, and I saw that under the sun, the race is not to the swift, nor the battle to the strong, nor bread to the wise, nor wealth to the learned, nor grace to the skillful: but there is a time and an end for all these things.
Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano: opambana pa kuthamanga si aliwiro, kapena opambana pa nkhondo si amphamvu, ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru, kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri, kapena okomeredwa mtima si ophunzira; koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake.
12 Man does not know his own end. But, just as fish are caught with a hook, and birds are captured with a snare, so are men seized in the evil time, when it will suddenly overwhelm them.
Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti: monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde, kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha, chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa, pamene tsoka limawagwera mosayembekezera.
13 This wisdom, likewise, I have seen under the sun, and I have examined it intensely.
Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri:
14 There was a small city, with a few men in it. There came against it a great king, who surrounded it, and built fortifications all around it, and the blockade was completed.
Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo.
15 And there was found within it, a poor and wise man, and he freed the city through his wisdom, and nothing was recorded afterward of that poor man.
Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo.
16 And so, I declared that wisdom is better than strength. But how is it, then, that the wisdom of the poor man is treated with contempt, and his words are not heeded?
Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake.
17 The words of the wise are heard in silence, more so than the outcry of a prince among the foolish.
Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambiri kupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru.
18 Wisdom is better than weapons of war. And whoever offends in one thing, shall lose many good things.
Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo, koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.

< Ecclesiastes 9 >