< Deuteronomy 26 >
1 “And when you will have entered into the land which the Lord your God will give to you to possess, and when you will have obtained it and are living within it:
Mukalowa ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu,
2 you shall take the first of all your crops, and place them in a basket, and you shall travel to the place which the Lord your God will choose, so that his name may be invoked there.
mutengeko zina mwa zipatso zoyamba pa zonse zimene mudzakola mʼnthaka ya dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ndi kuziyika mʼdengu. Mukatero mupite kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzakhazikitsako dzina lake
3 And you shall approach the priest who will be in those days, and you shall say to him: ‘I profess this day, before the Lord your God, that I have entered into the land about which he swore to our fathers that he would give it to us.’
ndipo mudzamuwuze wansembe amene ali pa ntchito pa nthawiyo kuti, “Ndikunenetsa lero kwa Yehova Mulungu wanu kuti ndabwera ku dziko limene Yehova analumbirira makolo athu kuti adzatipatsa ife.”
4 And the priest, taking up the basket from your hand, shall place it before the altar of the Lord your God.
Wansembe adzatenga dengulo mʼmanja mwanu ndi kuliyika pansi patsogolo pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
5 And you shall say, in the sight of the Lord your God: ‘The Syrian pursued my father, who descended into Egypt, and he sojourned there in a very small number, and he increased into a great and strong nation and into an innumerable multitude.
Ndipo mudzanenetsa pamaso pa Yehova Mulungu wanu kuti, “Abambo anga anali Mwaramu woyendayenda, anapita ku Igupto ndi anthu ochepa nakhala kumeneko. Pambuyo pake anakhala mtundu waukulu, wamphamvu ndi wochuluka.
6 And the Egyptians afflicted us, and they persecuted us, imposing upon us the most grievous burdens.
Koma Aigupto anatisautsa natizunza, kumatigwiritsa ntchito yakalavulagaga.
7 And we cried out to the Lord, the God of our fathers. He heard us, and he looked with favor upon our humiliation, and hardship, and distress.
Kenaka tinafuwulira Yehova, Mulungu wa makolo athu ndipo Yehova anamva mawu athu ndi kuona kusauka, kuvutika ndi kuponderezedwa kwathu.
8 And he led us away from Egypt, with a strong hand and an outstretched arm, with a mighty terror, with signs and wonders.
Kotero Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndi mkono wotambasuka ndi zoopsa zazikulu ndi zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa.
9 And he led us into this place, and he delivered to us the land flowing with milk and honey.
Iye anatibweretsa ku malo ano natipatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi lino.
10 And because of this, I now offer the first fruits of the land which the Lord has given to me.’ And you shall leave them in the sight of the Lord your God, and you shall adore the Lord your God.
Ndipo tsopano ndikubweretsa zipatso zoyamba zimene inu Yehova mwandipatsa.” Ikani dengulo pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kuwerama mopereka ulemu pamaso pake.
11 And you shall feast on all the good things which the Lord your God will give to you and to your house: you, and the Levite, and the new arrival who is with you.
Ndipo inu ndi Alevi pamodzi ndi alendo okhala pakati panu mudzakondwera mʼzinthu zonse zabwino zimene Yehova Mulungu wanu wakupatsani, inu ndi a pa banja panu.
12 When you will have completed the tithing of all your crops, in the third year of tithes, you shall give it to the Levite, and to the new arrival, and to the orphan, and to the widow, so that they may eat within your gates and be satisfied.
Mukatha kupatula chakhumi pa zonse zimene mwakolola mʼchaka chachitatu chimene ndi chaka chakhumi, muzichipereka kwa wansembe, mlendo, ana ndi akazi amasiye, kuti pamenepo adye mʼmizinda yanu nakhuta.
13 And you shall say, in the sight of the Lord your God: ‘I have taken what was sanctified from my house, and I have given it to the Levite, and to the new arrival, and to the orphan and the widow, just as you have commanded me. I have not transgressed your commandments, nor have I forgotten your precepts.
Kenaka munene kwa Yehova Mulungu wanu kuti “Ndatulutsamo mʼnyumba mwanga gawo lopatulika ndipo ndalipereka kwa Mlevi, mlendo, ana ndi akazi amasiye, monga mwa zonse zimene munalamula. Sindinapatuke pa zimene munalamula kapena kuyiwala ndi chimodzi chomwe.
14 I have not eaten from these things in my grief, nor have I separated them due to any kind of uncleanness, nor have I expended any of these things in funerals. I have obeyed the voice of the Lord my God, and I have done all things just as you have instructed me.
Sindinadye kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndimalira maliro kapena kuchotsapo kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndinali wodetsedwa, kapena kuperekako nsembe kwa akufa kalikonse ka gawoli. Ine ndamvera Yehova Mulungu wanga, ndachita chilichonse chimene inu munandilamula.
15 Look with favor from your sanctuary and from your lofty habitation amid the heavens, and bless your people Israel and the land which you have given to us, just as you swore to our fathers, a land flowing with milk and honey.’
Yangʼanani pa dziko kuchokera kumwamba, ku malo anu wopatulika, ndi kudalitsa anthu anu Aisraeli ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi limene mwatipatsa ife monga momwe munalonjezera pa malumbiro anu kwa makolo athu.”
16 Today the Lord your God has instructed you to carry out these commandments and judgments, and to keep and fulfill them, with all your heart and with all your soul.
Yehova Mulungu wanu akukulamulani lero lino kuti mutsate malangizo ndi malamulo ake ndipo muwasunge mosamalitsa ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
17 Today, you have chosen the Lord to be your God, so that you may walk in his ways, and keep his ceremonies and commandments and judgments, and obey his command.
Mwanena motsimikiza lero lino kuti Yehova ndiye Mulungu wanu ndi kuti mudzayenda mʼnjira zake, kusunga malangizo, malamulo ndi zonse akukulamulani ndi kutinso mudzamumvera.
18 Today, the Lord has chosen you, so that you may be his particular people, just as he has spoken to you, and so that you may keep all his precepts,
Ndipo Yehova wanenetsa lero lino kuti inu ndinu anthu ake, chuma chake chamtengowapatali monga momwe analonjezera, ndipo mukuyenera kusunga malamulo ake onse.
19 and so that he may cause you to be more exalted than all the nations which he has created, for the sake of his own praise and name and glory, in order that you may be a holy people for the Lord your God, just as he has spoken.”
Iye wanenetsa kuti adzakuyikani kukhala oyamikika, otchuka ndi olemekezeka koposa mitundu yonse imene anayilenga. Komanso mudzakhala anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu monga momwe analonjezera.