< Amos 2 >

1 Thus says the Lord: For three wicked deeds of Moab, and for four, I will not convert him, in so far as he has burned the bones of the king of Idumea, all the way to ashes.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
2 And I will send a fire onto Moab, and it will devour the buildings of Kerioth. And Moab will die with a noise, with the blare of a trumpet.
Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
3 And I will destroy the judge in their midst, and I will execute all his leaders with him, says the Lord.
Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
4 Thus says the Lord: For three wicked deeds of Judah, and for four, I will not convert him, in so far as he has rejected the law of the Lord and has not kept his commandments. For their idols, which their fathers followed, have deceived them.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
5 And I will send a fire onto Judah, and it will devour the buildings of Jerusalem.
Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
6 Thus says the Lord: For three wicked deeds of Israel, and for four, I will not convert him, in so far as he has sold the just for silver and the poor for shoes.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
7 They grind the heads of the poor into the dust of the earth, and they divert the way of the humble. And the son, as well as his father, have gone to the same girl, so that they outrage my holy name.
Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
8 And they have lain on garments taken in pledge next to every altar. And they drank the wine of the damned in the house of their God.
Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
9 Yet I exterminated the Amorites before their face, whose height was like the height of cedars, and whose strength was like the oak. And I crushed his fruit from above and his roots below.
“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
10 It is I who caused you to ascend from the land of Egypt, and I led you in the wilderness for forty years, so that you might possess the land of the Amorite.
“Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
11 And I stirred up prophets from your sons, and Nazirites from your young men. Is it not so, sons of Israel, says the Lord?
Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
12 Yet you would offer wine to the Nazirites, and you would command the prophets, saying: “Do not prophesy.”
“Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
13 Behold, I will creak under you, just as a wagon creaks that is laden with hay.
“Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
14 And flight will perish from the swift, and the strong will not maintain his strength, and the healthy will not save his life.
Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
15 And one holding the bow will not stand firm, and the swift of foot will not be saved, and the rider on the horse will not save his life.
Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
16 And the stout of heart among the strong will flee away naked in that day, says the Lord.
Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.

< Amos 2 >