< 2 Samuel 7 >
1 Now it happened that, when the king had settled in his house, and the Lord had given him rest on every side from all his enemies,
Mfumu itakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, Yehova atayipatsa mpumulo kwa adani ake onse woyizungulira,
2 he said to the prophet Nathan, “Do you not see that I live in a house of cedar, and that the ark of God has been placed in the midst of tent skins?”
mfumuyo inawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Mulungu lili mu tenti.”
3 And Nathan said to the king: “Go, do all that is in your heart. For the Lord is with you.”
Natani anayankha mfumu kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu chifukwa Yehova ali nanu.”
4 But it happened in that night, behold, the word of the Lord came to Nathan, saying:
Usiku umenewo mawu a Yehova anafika kwa Natani ndipo anati,
5 “Go, and say to my servant David: ‘Thus says the Lord: Should you build a house for me as a dwelling place?
“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti: kodi ndiwe amene udzandimangira Ine nyumba yokhalamo?
6 For I have not lived in a house from the day that I led the sons of Israel away from the land of Egypt, even to this day. Instead, I have walked in a tabernacle, and in a tent.
Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda uku ndi uku ndipo mokhala mwanga munali mu tenti.
7 And in all the places that I have crossed through, with all the sons of Israel, did I ever speak a word to anyone from the tribes of Israel, whom I instructed to pasture my people Israel, saying: Why have you not built me a house of cedar?’
Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense atsogoleri awo, amene ndinamulamula kuweta anthu anga Aisraeli kuti, nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
8 And now, so shall you speak to my servant David: ‘Thus says the Lord of hosts: I took you from the pastures, from following the sheep, so that you would be the leader over my people Israel.
“Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
9 And I have been with you everywhere that you walked. And I have slain all your enemies before your face. And I have made you a great name, beside the name of the great ones who are upon the earth.
Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
10 And I will appoint a place for my people Israel, and I will plant them, and they shall live there, and they shall no longer be disturbed. Neither shall the sons of iniquity continue to afflict them as before,
Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja,
11 from the day when I appointed judges over my people Israel. And I will give rest to you from all your enemies. And the Lord foretells to you that the Lord himself will make a house for you.
monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzakupatsaninso mpumulo kwa adani anu onse. “‘Yehova akulengeza kwa iwe kuti Iye mwini adzakhazikitsa banja lako:
12 And when your days will have been fulfilled, and you will sleep with your fathers, I will raise up your offspring after you, who will go forth from your loins, and I will make firm his kingdom.
Masiku ako akadzatha ndipo ukadzakapuma ndi makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, imene idzachokera mʼthupi mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
13 He himself shall build a house to my name. And I will establish the throne of his kingdom, even forever.
Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
14 I will be a father to him, and he shall be a son to me. And if he will commit any iniquity, I will correct him with the rod of men and with the wounds of the sons of men.
Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Akadzachita choyipa, Ineyo ndidzamulanga ndi ndodo ndi zikwapu za anthu.
15 But my mercy I will not take away from him, as I took it away from Saul, whom I removed from before my face.
Koma sindidzasiya kumukonda, monga ndinachitira ndi Sauli, amene ndinamuchotsa iwe usanakhale mfumu.
16 And your house shall be faithful, and your kingdom shall be before your face, for eternity, and your throne shall be secure continuously.’”
Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhala zamuyaya pamaso panga. Mpando wako waufumu udzakhazikika kwamuyaya!’”
17 According to all these words, and according to this entire vision, so did Nathan speak to David.
Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
18 Then king David entered and sat before the Lord, and he said: “Who am I, O Lord God, and what is my house, that you would bring me to this point?
Choncho Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati: “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ine ndine yani, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?”
19 Moreover, this has seemed little in your sight, O Lord God, unless you also will speak about the house of your servant for a long time. For this is the law of Adam, O Lord God.
Ndipo kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Kodi umu ndi mmene mumachitira ndi munthu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse?
20 Therefore, what more will David be able to say to you? For you know your servant, O Lord God.
Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu? Pakuti Inu Ambuye Wamphamvuzonse mukumudziwa mtumiki wanu.
21 Because of your word, and according to your own heart, you have done all these great deeds, so that you would make it known to your servant.
Chifukwa cha mawu anu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwachiwulula kwa mtumiki wanu.
22 For this reason, you are magnified, O Lord God. For there is no one like you. And there is no God except you, in all the things that we have heard with our own ears.
Inu ndinu wamkulu, Yehova Wamphamvuzonse! Palibe wina wofanana nanu, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha, monga tamvera ndi makutu athu.
23 But what nation is there upon the earth like your people Israel, because of whom God went forth, so that he might redeem a people for himself, and establish a name for himself, and accomplish for them great and terrible things upon the earth, before the face of your people, whom you redeemed for yourself away from Egypt, the nations and their gods.
Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
24 For you have secured your people Israel for yourself, as an everlasting people. And you, O Lord God, have become their God.
Inu mwawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
25 Now therefore, O Lord God, raise up forever the word that you have spoken over your servant and over his house. And do just as you have said,
“Ndipo tsopano Yehova Mulungu, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake. Chitani monga mwalonjezera,
26 so that your name may be magnified even forever, and so that it may be said: ‘The Lord of hosts is the God over Israel.’ And the house of your servant David will be established in the sight of the Lord.
kotero dzina lanu lidzakhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
27 For you, O Lord of hosts, God of Israel, have revealed to the ear of your servant, saying, ‘I will build a house for you.’ Because of this, your servant has found it in his heart to pray this prayer to you.
“Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, mwaululira mtumiki wanu ponena kuti, ‘Ine ndidzakumangira iwe nyumba!’ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
28 Now therefore, O Lord God, you are God, and your words shall be true. For you have spoken to your servant these good things.
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, ndinu Mulungu! Mawu anu ndi odalirika, ndipo mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
29 Therefore, begin, and bless the house of your servant, so that it may be forever before you. For you, O Lord God, have spoken. And so, let the house of your servant be blessed with your blessing forever.”
Ndipo tsopano chikukomereni kudalitsa banja la mtumiki wanu, kuti likhale mpaka muyaya pamaso panu. Pakuti Inu, Yehova Wamphamvuzonse, mwayankhula, ndipo ndi mʼdalitso wanu banja la mtumiki wanu lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”