< 1 Samuel 26 >

1 And the Ziphites went to Saul at Gibeah, saying: “Behold, David is hidden on the hill of Hachilah, which is opposite the wilderness.”
Anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ku Gibeya nati, “Davide akubisala ku phiri la Hakila, limene limayangʼanana ndi Yesimoni.”
2 And Saul rose up, and he descended into the desert of Ziph, and with him three thousand elect men of Israel, so that he might seek David in the desert of Ziph.
Choncho Sauli ananyamuka pamodzi ndi ankhondo ake 3,000 napita ku chipululu cha Zifi kukafunafuna Davide ku chipululuko.
3 And Saul encamped at Gibeah on Hachilah, which was opposite the wilderness on the way. But David was living in the desert. Then, seeing that Saul had arrived after him in the wilderness,
Sauli anamanga msasa wake mʼmbali mwa njira yopita ku phiri la Hakila moyangʼanana ndi Yesimoni. Koma Davide anali mʼchipululumo. Davide ataona kuti Sauli amamulondola mpaka kumeneko,
4 he sent explorers, and he learned that he certainly had arrived in that place.
iye anatumiza anthu okazonda ndipo anapeza kuti Sauli wafikadi ndithu.
5 And David rose up secretly, and he went to the place where Saul was. And when he had seen the place where Saul was sleeping, and Abner, the son of Ner, the leader of his military, and Saul sleeping in a tent, and the remainder of the common people all around him,
Tsono Davide ananyamuka napita kumalo kumene Sauli anamanga misasa. Iye anaona pamene Sauli ndi Abineri mwana wa Neri mkulu wa ankhondo anagona. Sauli anagona mʼkati mwa tenti ndipo asilikali anagona momuzungulira.
6 David spoke to Ahimelech, the Hittite, and to Abishai, the son of Zeruiah, the brother of Joab, saying, “Who will descend with me to Saul in the camp?” And Abishai said, “I will descend with you.”
Ndipo Davide anafunsa Ahimeleki Mhiti ndi Abisai mwana wa Zeruya, mʼbale wa Yowabu kuti, “Ndani adzapita nane ku msasa kwa Sauli?” Abisai anayankha kuti, “Ine ndidzapita nanu.”
7 Therefore, David and Abishai went to the people by night, and they found Saul lying down and sleeping in the tent, with his spear fixed in the ground at his head. And Abner and the people were sleeping all around him.
Choncho Davide ndi Abisai anapita ku misasa ya ankhondowo usiku. Atafika anangopeza Sauli ali gone mu msasa wake mkondo wake atawuzika pansi pafupi ndi mutu wake, Abineri ndi ankhondo onse anali atagona momuzungulira.
8 And Abishai said to David: “God has enclosed your enemy this day in your hands. Now therefore, I will pierce him with my lance, through to the ground, once, and there will not need to be a second.”
Abisai anawuza Davide kuti, “Lero Mulungu wapereka mdani wanu mʼmanja mwanu. Tsopano ndiloleni ndimukhomere pansi ndi mkondo wangawu kamodzinʼkamodzi. Sindimulasa kawiri.”
9 And David said to Abishai: “You shall not kill him. For who may extend his hand against the Christ of the Lord, and yet be innocent?”
Koma Davide anamuyankha Abisai kuti, “Usamuphe! Ndani adzapha wodzozedwa wa Yehova ndi kupezeka wosalakwa?
10 And David said: “As the Lord lives, unless the Lord himself will strike him, or unless his day to die will have arrived, or unless, descending into battle, he will perish,
Davide anati, Pali Yehova wamoyo, Yehova mwini ndiye adzamukanthe, mwina tsiku lake lomwalira lidzafika, kapena adzapita ku nkhondo nakaphedwa komweko.
11 may the Lord be gracious to me, so that I may not extend my hand against the Christ of the Lord. Now therefore, take the spear that is at his head, and the cup of water, and let us go.”
Koma Yehova andiletse kuti ndisapweteke wodzozedwa wa Yehova. Tsopano tingotenga mkondo umene uli ku mutu kwakewo ndi botolo la madzilo ndipo tizipita.”
12 And so, David took the spear, and the cup of water that was at Saul’s head, and they went away. And there was no one who saw it, or realized it, or awakened, but they were all sleeping. For a deep sleep from the Lord had fallen over them.
Motero Davide anatenga mkondo ndi botolo lamadzi zimene zinali ku mutu kwa Sauli ndipo anachoka. Palibe amene anaona zimenezi kapena kudziwa, ndipo palibenso amene anadzuka. Onse anali mʼtulo, chifukwa Yehova anawagonetsa tulo tofa nato.
13 And when David had crossed over to the opposite side, and had stood upon the top of the hill far away, so that there was a great interval between them,
Pambuyo pake Davide anadutsa nakakwerera mbali ina ya phiri, ndi kuyimirira pamwamba pa phiri patali. Pakati pawo panali mpata waukulu.
14 David cried out to the people, and to Abner, the son of Ner, saying, “Will you not respond, Abner?” And responding, Abner said, “Who are you, that you would cry out and disquiet the king?”
Davide anayitana gulu lankhondo ndi Abineri mwana wa Neri nawafunsa kuti, “Kodi sundiyankha ine Abineri?” Abineri anayankha kuti, “Ndiwe yani amene ukuyitana mfumu?”
15 And David said to Abner: “Are you not a man? And who else is like you in Israel? Then why have you not guarded your lord the king? For one of the people entered, so that he might kill the king, your lord.
Davide anamufunsa Abineri kuti, “Kodi sindiwe mwamuna? Ndipo wofanana nawe ndani mu Israeli? Nʼchifukwa chiyani sunateteze mbuye wako mfumu? Munthu wina anabwera kumeneko.
16 This is not good, what you have done. As the Lord lives, you are sons of death, because you have not guarded your lord, the Christ of the Lord. Now therefore, where is the king’s spear, and where is the cup of water that was at his head?”
Chimene wachita iwe si chabwino. Pali Yehova wamoyo iwe ndi asilikali ako muyenera kufa chifukwa simunateteze mbuye wanu, wodzozedwa wa Yehova. Tayangʼanayangʼana. Uli kuti mkondo wa mfumu ndi botolo lamadzi zimene zinali kumutu kwa mfumu?”
17 Then Saul recognized the voice of David, and he said, “Is this not your voice, my son David?” And David said, “It is my voice, my lord the king.”
Sauli anazindikira mawu a Davide ndipo anafunsa kuti, “Kodi amenewa ndi mawu ako Davide mwana wanga?” Davide anayankha, “Inde ndi anga, mbuye wanga mfumu.
18 And he said: “For what reason has my lord pursued his servant? What have I done? Or what evil is there in my hand?
Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mukundilonda ine mtumiki wanu? Kodi ine ndachita chiyani ndipo ndapezeka ndi cholakwa chotani?
19 Now therefore, listen, I beg you, my lord the king, to the words of your servant. If the Lord has stirred you up against me, let him make the sacrifice fragrant. But if the sons of men have done so, they are accursed in the sight of the Lord, who has cast me out this day, so that I would not live within the inheritance of the Lord, saying, ‘Go, serve strange gods.’
Tsopano mbuye wanga mfumu tamverani mawu a mtumiki wanu. Ngati ndi Yehova wautsa mtima wanu kuti mundiwukire, ndiye alandire chipepeso. Koma ngati ndi anthu amene achita zimene, ndiye Yehova awatemberere popeza andipirikitsa lero kundichotsa mʼdziko la Yehova, namati, ‘Pita kapembedze milungu ina.’
20 And now, let not my blood be poured out upon the earth before the Lord. For the king of Israel has gone out, so that he might seek a flea, just as the partridge is pursued amid the mountains.”
Tsopano musalole kuti magazi anga akhetsedwe kutali ndi Yehova pakuti mfumu ya Israeli yatuluka kudzafunafuna ine nsabwe, monga mmene munthu asakira nkhwali ku mapiri.”
21 And Saul said: “I have sinned. Return, my son David. For I will never again do evil to you, because my life has been precious in your eyes this day. For it is apparent that I have acted senselessly, and have been ignorant of very many things.”
Ndipo Sauli anati, “Ine ndachimwa. Bwerera mwana wanga Davide. Sindidzakuchitanso choyipa popeza lero wauwona moyo wanga ngati wamtengowapatali. Taona, ndachita zauchitsiru ndipo ndachimwa kwambiri.”
22 And responding, David said: “Behold, the king’s spear. Let one of the servants of the king cross over and take it.
Davide anayankha kuti, “Nawu mkondo wanu, mfumu. Tumani mmodzi wa anyamata anu abwere adzatenge.
23 And the Lord will repay each one according to his justice and faith. For the Lord has delivered you this day into my hand, but I was not willing to extend my hand against the Christ of the Lord.
Yehova amadalitsa munthu aliyense wolungama ndi wokhulupirika. Yehova anakuperekani lero mʼmanja mwanga, koma ine sindinakhudze wodzozedwa wa Yehova.
24 And just as your soul has been magnified this day in my eyes, so let my soul be magnified in the eyes of the Lord, and may he free me from all distress.”
Monga momwe ine lero ndachitira kuwuyesa moyo wanu ngati wamtengowapatali, momwemonso Yehova awuyese moyo wanga wamtengowapatali ndipo andipulumutse mʼmavuto anga onse.”
25 Then Saul said to David: “You are blessed, my son David. And whatever you may do, it shall certainly succeed.” And David departed on his way. And Saul returned to his place.
Ndipo Sauli anawuza Davide kuti, “Yehova akudalitse iwe Davide mwana wanga. Udzachita zinthu zazikulu ndipo udzapambana.” Choncho Davide anayenda njira yake ndipo Sauli anabwerera kwawo.

< 1 Samuel 26 >