< 1 Samuel 20 >
1 Then David fled from Naioth, which is in Ramah, and he went and said before Jonathan: “What have I done? What is my iniquity, or what is my sin, against your father, so that he would seek my life?”
Tsono Davide anathawa ku Nayoti ku Rama ndi kupita kwa Yonatani ndipo anamufunsa kuti, “Kodi ine ndinachita chiyani? Kodi ndinalakwa chiyani? Kodi abambo ako ndinawalakwira chiyani kuti azifuna kundipha?”
2 And he said to him: “May this not be! You shall not die. For my father will not do anything, great or small, without first revealing it to me. Therefore, has my father concealed this word solely from me? By no means shall this be!”
Yonatani anayankha kuti, “Sizitheka! Iwe sufa ayi! Taona abambo anga sachita chinthu chilichonse chachikulu kapena chachingʼono wosandiwuza ine. Tsopano abambo anga angandibisire bwanji zimenezi? Sichoncho ayi.”
3 And he swore again to David. And David said: “Your father certainly knows that I have found favor in your sight, and so he will say, ‘Let Jonathan not know this, lest he be saddened.’ So truly, as the Lord lives, and as your soul lives, there is only one step (if I may say it) separating me from death.”
Koma Davide analumbira kuti, “Abambo ako akudziwa bwino lomwe kuti iwe umandikonda ndipo iwo amaganiza kuti, Yonatani sayenera kudziwa zimenezi mwina adzamva chisoni kwambiri. Komabe, pali Yehova ndi pali iwe, imfa sinanditalikire.”
4 And Jonathan said to David, “Whatever your soul will tell me, I will do for you.”
Yonatani anawuza Davide kuti, “Chilichonse chimene iwe ukufuna kuti ndichite, ndidzakuchitira.”
5 Then David said to Jonathan: “Behold, tomorrow is the new moon, and I am accustomed to sit in a seat beside the king to eat. Therefore, permit me that I may be hidden in the field, until the evening of the third day.
Ndipo Davide anati, “Taona mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano, ndipo ine ndiyenera kukadya ndi mfumu. Koma undilole ndipite ndikabisale mʼmunda mpaka mkuja madzulo.
6 If your father, looking around, will seek me, you shall respond to him: ‘David asked me if he may hurry to Bethlehem, his own city. For there are solemn sacrifices in that place for all of his tribe together.’
Ngati abambo ako akafunsa za ine, ukawawuze kuti, ‘Davide anandiwumiriza kuti ndimulole apite msanga kwawo ku Betelehemu, chifukwa akupereka nsembe yapachaka ya banja lonse.’
7 If he will say, ‘It is well,’ then your servant will have peace. But if he will be angry, know that his malice has reached its height.
Akanena kuti, ‘Wachita bwino,’ ndiye kuti zinthu zindiyendera bwino ine mtumiki wako. Koma ngati akapsa mtima, ndiye udziwe kuti iwo atsimikiza zondichita zoyipa.
8 Therefore, show mercy to your servant. For you have brought me, your servant, into a covenant of the Lord with you. But if there is any iniquity in me, you may kill me, and you shall not lead me in to your father.”
Koma undikomere mtima ine mtumiki wako, pakuti unapangana nane pangano pamaso pa Yehova. Ngati ndine wolakwa undiphe ndiwe, koma usandipereke kwa abambo ako.”
9 And Jonathan said: “May this be far from you. For certainly, if I ever realized that any wickedness was determined by my father against you, I would not be able to do anything other than report it to you.”
Yonatani anati, “Sizitheka! Ndikanadziwa kuti abambo anga atsimikiza kuti akuchite choyipa, kodi sindikanakuwuza?”
10 And David responded to Jonathan, “Who will repeat it to me, if your father may perhaps answer you harshly about me?”
Davide anafunsa kuti, “Adzandiwuza ndani ngati abambo ako akuyankhe mwaukali?”
11 And Jonathan said to David, “Come, and let us go out into the field.” And when they both had gone out into the field,
Yonatani anawuza Davide kuti, “Tiyeni tikayende ku mundako.” Ndipo anapita onse awiri.
12 Jonathan said before David: “O Lord, God of Israel, if I will discover a decision by my father, tomorrow, or the day after, and if there will be anything good concerning David, and yet I do not immediately send to you and make it known to you,
Kenaka Yonatani anawuza Davide kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akhale mboni! Ine ndikadzafunsa abambo anga nthawi yonga ino mmawa kapena mkuja, ndipo ndikadzapeza kuti akukufunira zabwino, ine ndidzatuma mawu kuti udziwe.
13 may the Lord do these things to Jonathan, and may he add these other things. But if my father will have persevered in malice against you, I will reveal it to your ear, and I will send you away, so that you may go in peace, and so that the Lord may be with you, just as he was with my father.
Koma ngati abambo anga atsimikiza kukuchita choyipa, Yehova andilange ine Yonatani, ndipotu kwambiri ngati sindidzakudziwitsa ndi kukulola kuti upite mu mtendere. Yehova akhale nawe monga anakhalira ndi abambo anga.
14 And if I live, you shall show the mercy of the Lord to me. Yet truly, if I die,
Ndikakhalabe ndi moyo udzandionetse kukoma mtima monga kwa Yehova nthawi yonse ya moyo wanga, kuti ine ndisaphedwe.
15 you shall not take away your mercy from my house, even forever, when the Lord will have rooted out the enemies of David, each and every one of them, from the earth. May he take Jonathan from his house, and may the Lord require it from the hands of the enemies of David.”
Ndipo usadzaleke kuchitira chifundo banja langa. Pamene Yehova adzawatha adani onse a Davide pa dziko lapansi.”
16 Therefore, Jonathan formed a covenant with the house of David. And the Lord required it from the hands of the enemies of David.
“Dzina la ine Yonatani lisadzafafanizidwe nawo pamodzi. Yehova alange adani onse a Davide.”
17 And Jonathan continued to swear to David, because he loved him. For he loved him like his own soul.
Kenaka Yonatani anamulumbiritsanso Davide kuti asaleke kumukonda, pakuti ankamukonda monga ankadzikondera yekha.
18 And Jonathan said to him: “Tomorrow is the new moon, and you will be sought.
Kenaka Yonatani anawuzanso Davide kuti, “Mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano. Zidzadziwika kuti iwe palibe chifukwa mpando wako udzakhala wopanda munthu.
19 For your seat will be empty until the day after tomorrow. Therefore, you shall descend quickly, and you shall go to the place where you are to be hidden, on a day when it is lawful to work, and you shall remain beside the stone that is called Ezel.
Mkuja adzakufunafuna. Tsono udzapite pamalo pamene unabisala poyamba paja ndipo ukadikire pa mulu wa miyala uli apowo.
20 And I will shoot three arrows near it, and I will cast them as if I were practicing for myself toward a mark.
Ine ndidzaponya mivi itatu pambali pake, ngati ndikulasa chinthu.
21 Also, I will send a boy, saying to him, ‘Go and bring the arrows to me.’
Ndipo ndidzatuma mnyamata ndi kuti, ‘Pita ukatole miviyo!’ Ngati ndidzanena kwa iye kuti, ‘Taona, mivi ili mbali yakuno, kayitole,’ iwe ukatuluke, pakuti ndikulumbira, pali Yehova Wamoyo, ndiye kuti zako zili bwino, palibe choopsa chilichonse.
22 If I will say to the boy, ‘Behold, the arrows are before you, take them up,’ you shall approach before me, because there is peace for you, and there is nothing evil, as the Lord lives. But if I will have spoken to the boy in this way, ‘Behold, the arrows are away from you,’ then you shall go away in peace, for the Lord has released you.
Koma ndikadzati, ‘Taona mivi ili patsogolo pako,’ iwe udzachoke chifukwa Yehova ndiye walola kuti uchokepo.
23 Now about the word that you and I have spoken, may the Lord be between you and me, even forever.”
Tsono zimene tapanganazi Yehova ndiye mboni pakati pa iwe ndi ine mpaka muyaya.”
24 Therefore, David was hidden in the field. And the new moon came, and the king sat down to eat bread.
Choncho Davide anakabisala mʼmunda ndipo nthawi ya chikondwerero cha mwezi watsopano itakwana mfumu Sauli anadzakhala pansi kuti adye.
25 And when the king had sat down on his chair, (according to custom) which was beside the wall, Jonathan rose up, and Abner sat beside Saul, and David’s place appeared empty.
Iye anakhala pa malo ake a nthawi zonse pafupi ndi khoma moyangʼanana ndi Yonatani, ndipo Abineri anakhala moyandikana ndi Sauli, koma pa malo a Davide panalibe munthu.
26 And Saul did not say anything on that day. For he was thinking that perhaps something happened to him, so that he was not clean, or not purified.
Sauli sananene chilichonse tsiku limenelo pakuti ankaganiza kuti “Chilipo chimene chachitika ndi Davide. Mwina mwake ngosayenera za chipembedzo.”
27 And when the second day after the new moon had begun to dawn, David’s place again appeared empty. And Saul said to Jonathan, his son, “Why has the son of Jesse not arrived to eat, neither yesterday, nor today?”
Koma pa tsiku lachiwiri la chikondwerero cha mwezi watsopano pamalo pa Davide panalibenso munthu. Kenaka Sauli anafunsa Yonatani kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwana wa Yese sanabwere kudzadya, dzulo ngakhale lero?”
28 And Jonathan responded to Saul, “He petitioned me earnestly that he might go to Bethlehem,
Yonatani anayankha kuti, “Davide anandiwumiriza kuti ndimulole kuti apite ku Betelehemu.
29 and he said: ‘Permit me. For there is a solemn sacrifice in the city. One of my brothers has summoned me. Now therefore, if I have found favor in your eyes, I will go quickly, and I will see my brothers.’ For this reason, he has not come to the table of the king.”
Anati, ‘Undilole ndipite, chifukwa banja lathu likupereka nsembe mu mzindamo ndipo mʼbale wanga wandiwumiriza kuti ndikakhale nawo. Ngati wandikomera mtima, chonde ndilole ndipite ndikaone abale anga.’ Nʼchifukwa chake sanabwere kudzadya ndi mfumu.”
30 Then Saul, becoming angry against Jonathan, said to him: “You son of a woman wantonly seizing a man! Could I be ignorant that you love the son of Jesse, to your own shame, and to the shame of your disgraceful mother?
Sauli anamupsera mtima Yonatani ndipo namuwuza kuti, “Iwe mwana wobadwa mwa mkazi wamakhalidwe oyipa ndi wowukira! Kodi ukuyesa kuti ine sindikudziwa kuti umagwirizana ndi mwana wa Yese, amene akufuna kukuchititsa manyazi iwe ndi amayi ako?
31 For all the days that the son of Jesse moves upon earth, neither you, nor your kingdom, will be secure. And so, send and bring him to me, here and now. For he is a son of death.”
Mwana wa Yese akakhala ndi moyo pa dziko lapansi lino, iwe sudzakhala mfumu. Tsopano tumiza munthu akamutenge kubwera naye kwa ine, pakuti Davide ayenera kufa basi!”
32 Then Jonathan, answering his father Saul, said: “Why should he die? What has he done?”
Yonatani anafunsa abambo ake kuti, “Nʼchifukwa chiyani mufuna kuti Davide aphedwe? Iye walakwa chiyani?”
33 And Saul picked up a lance, so that he might strike him. And Jonathan understood that it had been decided by his father that David be put to death.
Apo Sauli anamuponyera mkondo wake kuti amuphe. Tsono Yonatani anadziwa kuti abambo ake atsimikiza mtima kuti aphe Davide.
34 Therefore, Jonathan rose up from the table in a rage of anger. And he did not eat bread on the second day after the new moon. For he was saddened over David, because his father had confounded him.
Yonatani anachoka pa tebulopo ali wopsa mtima kwambiri. Tsiku lachiwiri la chikondwererocho Yonatani sanadye chakudya. Iye anawawidwa mtima chifukwa abambo ake anatsimikiza zakupha Davide.
35 And when the morning had begun to dawn, Jonathan went into the field according to the agreement with David, and a young boy was with him.
Tsono mmawa Yonatani anapita ku munda kumene anapangana ndi Davide. Anali ndi mnyamata wake.
36 And he said to his boy, “Go, and bring to me the arrows that I shoot.” And when the boy had run, he shot another arrow away from the boy.
Tsono anawuza mnyamatayo kuti, “Thamanga ukatole muvi umene nditi ndiponye.” Mnyamatayo akuthamanga Yonatani anaponya muvi patsogolo pa mnyamatayo.
37 And so, the boy went to the place of the arrow which Jonathan had shot. And Jonathan cried out, from behind the back of boy, and said: “Behold, the arrow is there, farther away from you.”
Mnyamatayo atafika pamene muvi wa Yonatani unagwera,
38 And Jonathan cried out again, from behind the back of the boy, saying, “Go quickly! Do not stand still!” Then Jonathan’s boy collected the arrows, and he brought them to his lord.
Yonatani anayitananso mnyamatayo kuti, “Fulumira, pita msanga usayime.” Choncho mnyamatayo anatola muvi uja ndi kubwera nayo kwa mbuye wake.
39 And he did not understand at all what was happening. For only Jonathan and David knew the matter.
(Mnyamatayo sanadziwe chimene chimachitika koma Yonatani ndi Davide ndiwo ankadziwa).
40 Then Jonathan gave his weapons to the boy, and he said to him, “Go, and carry them into the city.”
Pambuyo pake Yonatani anapereka zida zake za nkhondo kwa mnyamatayo ndipo anati, “Pita, nyamula ubwerere nazo ku mzinda.”
41 And when the boy had gone away, David rose up from his place, which turned toward the south, and falling prone on the ground, he reverenced three times. And kissing one another, they wept together, but David more so.
Mnyamatayo anapita. Kenaka Davide anatuluka ku mbali ina ya mulu wa miyala uja, nadzigwetsa pansi ndi kugunditsa nkhope yake pansi katatu. Anapsompsona nayamba kulira onse awiri, koma Davide analira kwambiri.
42 Then Jonathan said to David: “Go in peace. And let us both keep all that we have ever sworn in the name of the Lord, saying, ‘May the Lord be between me and you, and between my offspring and your offspring, even forever.’” And David rose up and went away. But Jonathan entered into the city.
Yonatani anawuza Davide kuti, “Pita mu mtendere pakuti ife awiri tinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Yehova ndiye akhale mboni pakati pa iwe ndi ine ndiponso pakati pa zidzukulu zako ndi zidzukulu zanga kwa nthawi yonse.’” Kenaka Davide anachoka, ndipo Yonatani anabwerera ku mzinda kuja.