< 1 Samuel 14 >
1 And it happened that, on a certain day, Jonathan, the son of Saul, said to the youth who bore his armor, “Come, and let us go over to the garrison of the Philistines, which is across from that place.” But he did not reveal this to his father.
Tsiku lina Yonatani mwana wa Sauli anawuza mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka Afilisti tsidya ilo.” Koma iye sanawuze abambo ake.
2 Moreover, Saul was staying in the furthermost part of Gibeah, below the pomegranate tree that was at Migron. And the people with him were about six hundred men.
Sauli ankakhala mʼmalire a Gibeya pa tsinde pa mtengo wamakangadza ku Migironi. Anthu amene anali naye analipo 600.
3 And Ahijah, the son of Ahitub, the brother of Ichabod, the son of Phinehas, who had been born of Eli, the priest of the Lord at Shiloh, wore the ephod. But the people did not know where Jonathan had gone.
Pakati pawo panalinso Ahiya amene ankavala efodi. Iye anali mwana wa Ahitubi, mʼbale wake wa Ikabodi mwana wa Finehasi, mwana wa Eli, wansembe wa Yehova wa ku Silo. Koma palibe amene anadziwa kuti Yonatani wachoka.
4 Now there were, between the ascents along which Jonathan strove to cross to the garrison of the Philistines, rocks projecting from both sides, and, in the manner of teeth, boulders breaking out from one side and the other. The name of one was Shining, and the name of the other was Thorny.
Pa mpata pamene Yonatani ankafuna kudutsa kukafika ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti kunali thanthwe lotsetsereka mbali ina ndi lina lotsetsereka mbali inayo. Thanthwe limodzi linkatchedwa Bozezi ndipo linalo linkatchedwa Seni.
5 One boulder projected toward the north, opposite Michmash, and the other toward the south, opposite Gibeah.
Thanthwe limodzi linali chakumpoto kuyangʼanana ndi Mikimasi, ndipo thanthwe linalo linali chakummwera kuyangʼanana ndi Geba.
6 Then Jonathan said to the youth who bore his armor: “Come, let us go across to the garrison of these uncircumcised. And perhaps the Lord may act on our behalf. For it is not difficult for the Lord to save, either by many, or by few.”
Yonatani anawuza mnyamata wake womunyamulira zida uja kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka anthu osachita mdulidwewo. Mwina Yehova adzatigwirira ntchito. Palibe chomuletsa Yehova kutipulumutsa, ngakhale tikhale ambiri kapena ochepa.”
7 And his armor bearer said to him: “Do all that is pleasing to your soul. Go wherever you wish, and I will be with you, wherever you will choose.”
Mnyamata uja anati, “Chitani chilichonse chimene mtima wanu ukhumba. Ine ndili nanu pamodzi. Chimene mtima wanu ukhumba ndi chomwenso ine ndikhumba.”
8 And Jonathan said: “Behold, we will cross over to these men. And when we will be seen by them,
Yonatani anati, “Tiye tsono tiwoloke kupita kumene kuli anthuwo ndi kukadzionetsa kwa iwo.
9 if they have spoken to us in this way, ‘Stay until we come to you,’ let us stand still in our place, and not ascend to them.
Akatiwuza kuti, ‘Imani pomwepo mpaka tikupezeni,’ ife tikangoyima pomwepo osapita kumene kuli iwoko.
10 But if they will say, ‘Ascend to us,’ let us ascend. For the Lord has delivered them into our hands. This will be the sign to us.”
Koma akadzati, ‘Bwerani kuno,’ ndiye ife tikapitedi, chifukwa ichi chidzakhala chizindikiro chakuti Yehova wapereka mʼmanja mwathu.”
11 And so, both of them appeared before the garrison of the Philistines. And the Philistines said, “See, the Hebrews have come out from the holes in which they had been hiding.”
Choncho awiriwa anadzionetsa ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti. Tsono Afilistiwo anati, “Taonani! Aheberi akutuluka mʼmaenje mʼmene anabisala.”
12 And the men of the garrison spoke to Jonathan and to his armor bearer, and they said, “Ascend to us, and we will show you something.” And Jonathan said to his armor bearer: “Let us ascend. Follow me. For the Lord has delivered them into the hands of Israel.”
Anthu a ku kaboma kaja anafuwula kwa Yonatani ndi mnyamata wake uja kuti, “Bwerani kuno ndipo tikuphunzitsani phunziro.” Ndipo Yonatani anati kwa mnyamata wake. “Nditsate pakuti Yehova wapereka Afilistiwa mʼmanja mwa Aisraeli.”
13 Then Jonathan ascended, crawling on his hands and feet, and his armor bearer after him. And then, some fell before Jonathan, others his armor bearer killed as he was following him.
Choncho Yonatani anakwera mokwawa, ndipo mnyamata wake uja ankamutsata. Tsono Yonatani anathira nkhondo Afilisti aja namawagwetsa, ndipo mnyamata wake uja ankawapha pambuyo pa iyeyo.
14 And the first slaughter was made when Jonathan and his armor bearer struck down about twenty of the men, in the midst of an area of land that a yoke of oxen would usually plow in a day.
Nthawi yoyambayo Yonatani ndi mnyamata wake uja anapha anthu makumi awiri ndipo anawaphera pa malo ochepa okwanira ngati theka la ekala.
15 And a miracle occurred in the camp, out in the fields. And all of the people of their garrison, who had gone out in order to plunder, were stupefied. And the earth trembled. And it happened as a miracle from God.
Tsono gulu lonse la ankhondo, ndiye kuti iwo amene anali mʼmisasa ndi mʼminda ndiponso iwo amene anali ku kaboma ka ankhondo kaja, onse anagwidwa ndi mantha aakulu. Dzikonso linagwedezeka, choncho anthu anachita mantha koopsa.
16 And the watchmen of Saul, who were at Gibeah of Benjamin, looked out, and behold, a multitude was thrown down and dispersed, this way and that.
Alonda a Sauli a ku Gibeya dziko la Benjamini atangomwaza maso anangoona chigulu cha asilikali chikumwazikana uku ndi uku.
17 And Saul said to the people who were with him, “Inquire and see who has gone out from us.” And when they had inquired, it was found that Jonathan and his armor bearer were not present.
Kenaka Sauli anawawuza anthu amene anali naye kuti, “Awerengeni asilikali kuti muona amene wachoka.” Atawawerenga anapeza kuti Yonatani ndi mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo palibe.
18 And Saul said to Ahijah, “Bring the ark of the God.” (For the ark of God was, in that day, with the sons of Israel in that place.)
Tsono Sauli anawuza Ahiya kuti, “Bwera nalo Bokosi la Mulungulo.” (Nthawi imeneyo nʼkuti efodiyo ili ndi Ahiya pamaso pa Aisraeli).
19 And while Saul spoke to the priest, there arose a great tumult in the camp of the Philistines. And it was increasing, little by little, and it was being heard more clearly. And Saul said to the priest, “Withdraw your hand.”
Pamene Sauli amayankhula ndi wansembe, phokoso limanka likulirakulira mu msasa wa Afilisti, Kotero Sauli anati kwa wansembe, “Leka kuwombeza.”
20 Then Saul, and all the people who were with him, cried out together, and they went to the place of the conflict. And behold, each one’s sword had been turned against his neighbor, and there was a very great slaughter.
Ndipo Sauli ndi asilikali onse amene anali naye anasonkhana kupita kukamenya nkhondo, ndipo anangoona chisokonezo chachikulu kwambiri. Afilisti akuphana okhaokha.
21 Moreover, the Hebrews who had been with the Philistines yesterday and the day before, and who had ascended with them into the camp, turned back so that they might be with those of Israel who were with Saul and Jonathan.
Aheberi ena amene kale anali ndi Afilisti mpaka kukakhala ku misasa yawo, iwonso anatembenuka nakhala pamodzi ndi Aisraeli amene ankatsata Sauli ndi Yonatani.
22 Likewise, all the Israelites who had hidden themselves on mount Ephraim, hearing that the Philistines had fled, joined themselves with their own in the battle. And there were with Saul about ten thousand men.
Ngakhale Aisraeli amene ankabisala ku dziko lamapiri la Efereimu atamva kuti Afilisti akuthawa, nawonso anawathamangitsa Afilistiwo nawathira nkhondo.
23 And the Lord saved Israel on that day. But the fight continued as far as Bethaven.
Nkhondo inapitirira mpaka kufika ku Beti-Aveni. Choncho Yehova anapulumutsa Aisraeli tsiku limenelo.
24 And the men of Israel were joined together on that day. And Saul made the people swear, saying, “Cursed be the man who will eat bread, until evening, until I am avenged of my enemies.” And the entire people did not consume bread.
Koma asilikali a Israeli anavutika tsiku limenelo, chifukwa Sauli anawalumbirira Aisraeli kuti, “Wotembereredwa munthu aliyense amene adzadya kusanade, ine ndisanalipsire adani anga!” Kotero palibe wankhondo aliyense amene analawa chakudya.
25 And all the common people went into a forest, in which there was honey on the surface of the field.
Gulu lonse la ankhondo linalowa mʼnkhalango mmene munali uchi.
26 And so the people entered the forest, and there appeared flowing honey, but no one drew his hand near his mouth. For the people were afraid of the oath.
Atalowa mʼnkhalango, anaona uchi ukukha, koma palibe amene anadya, pakuti ankaopa lumbiro lija.
27 But Jonathan had not heard that his father had bound the people to an oath. And so he extended the top of the staff that he was holding in his hand, and he dipped it in a honeycomb. And he turned his hand to his mouth, and his eyes were brightened.
Koma Yonatani sanamve kuti abambo ake anawalumbirira anthu aja choncho anatenga ndodo yake imene inali mʼdzanja lake ndipo anayipisa mu chisa cha njuchi. Choncho iye anadya uchiwo ndipo mʼmaso mwake munayera.
28 And in response, one of the people said, “Your father has bound the people by an oath, saying: ‘Cursed be the man who will eat any bread this day.’” (For the people were faint.)
Kenaka mmodzi mwa Asilikali anamuwuza kuti, “Abambo ako alumbirira anthu nati, ‘Wotembereredwa munthu aliyense amene adye chakudya lero.’ Nʼchifukwa chake anthu alefuka.”
29 And Jonathan said: “My father has troubled the land. You have seen for yourselves that my eyes were brightened, because I tasted a little of this honey.
Yonatani anati, “Abambo anga achita chinthu choyipira dziko. Taonani mʼmaso mwanga mwayera chifukwa ndalawa uchiwu pangʼono.
30 How much more so, if the people had eaten from the plunder that they find with their enemies? Would not a greater slaughter have been accomplished among the Philistines?”
Zikanakhala zabwino kwambiri anthuwa akanadya lero zofunkha za adani awo. Zikanatero tikanapha Afilisti ochuluka.”
31 Therefore, on that day, they struck down the Philistines, from Michmash as far as Aijalon. But the people were exceedingly wearied.
Tsiku limenelo Aisraeli anapha Afilisti kuchokera ku Mikimasi mpaka ku Ayaloni. Koma Aisraeliwo analefuka kwambiri ndi njala.
32 And turning to the spoils, they took sheep, and oxen, and calves, and they slew them on the ground. And the people ate with blood.
Choncho iwo anathamangira pa zofunkha ndipo anatenga nkhosa, ngʼombe ndi ana angʼombe. Iwo anazipha zonsezi nazidya pamodzi ndi magazi omwe.
33 Then they reported to Saul, saying that the people had sinned against the Lord, eating with blood. And he said: “You have transgressed. Roll a great stone to me, here and now.”
Koma anthu ena anawuza Sauli kuti, “Taona anthu akuchimwira Yehova pakudya nyama yomwe ili ndi magazi.” Ndipo Sauli anati, “Mwaonetsa kusakhulupirika. Tsopano gubuduzirani mwala waukulu pano.”
34 And Saul said: “Disperse yourselves among the common people, and tell each one of them to bring to me his ox and his ram, and to slay them upon this stone, and to eat, so that you will not sin against the Lord, in eating with blood.” And so, each one, out of all the people, brought his ox, by his own hand, throughout the night. And they slew them there.
Kenaka Sauli anati, “Mwazikanani pakati pa anthu ndi kukawawuza kuti aliyense abwere ndi ngʼombe yake kapena nkhosa yake, ndipo adzayiphe pomwe pano ndi kuyidya. Musachimwire Yehova pakudya nyama imene ili ndi magazi.” Kotero aliyense anabwera ndi ngʼombe yake usiku womwewo ndi kuyipha pomwepo.
35 Then Saul built an altar to the Lord. And so, it was then that he first began to build an altar to the Lord.
Ndipo Sauli anamangira Yehova guwa. Ili linali guwa loyamba limene Sauli anamangira Yehova.
36 And Saul said: “Let us fall upon the Philistines by night, and lay waste to them even until the morning light. And let us not leave behind a man among them.” And the people said, “Do all that seems good in your eyes.” And the priest said, “Let us draw near to God in this place.”
Sauli anati, “Tiyeni titsatire Afilisti usikuwu ndi kulanda zinthu zawo mpaka mmawa. Tisasiyepo wamoyo ndi mmodzi yemwe.” Ankhondowo anayankha kuti, “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.” Koma wansembe anati, “Tipemphe uphungu kwa Mulungu poyamba.”
37 And Saul consulted the Lord: “Shall I pursue the Philistines? Will you deliver them into the hands of Israel?” And he did not respond to him on that day.
Choncho Sauli anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndiwatsatire Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwathu?” Koma Mulungu sanamuyankhe tsiku limenelo.
38 And Saul said: “Bring here every single leader of the people. And we shall know and see by whom this sin was committed this day.
Choncho Sauli anati, “Bwerani kuno nonse atsogoleri a anthu, ndipo tiyeni tione kuti kodi tchimo limeneli lachitika bwanji lero?
39 As the Lord lives, who is the Savior of Israel, even if it were done by my son Jonathan, without retraction he shall die.” In this, no one among all the people contradicted him.
Pali Yehova amene amapulumutsa Israeli, ngakhale tchimolo litapezeka ndi mwana wanga Yonatani, iye afe ndithu.” Koma palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthuwo amene anamuyankha.
40 And he said to all of Israel, “Separate yourselves on one side, and I, with my son Jonathan, will be on the other side.” And the people responded to Saul, “Do what seems good in your eyes.”
Tsono Sauli anawuza Aisraeli onse kuti, “Inu mukhale mbali imodzi. Ine ndi mwana wanga Yonatani tikhala mbali inayo.” “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.”
41 And Saul said to the Lord, the God of Israel: “O Lord, God of Israel, grant a sign: Why is it that you will not respond to your servant this day? If this iniquity is in me, or in my son Jonathan, grant an indication. Or if this iniquity is in your people, grant a sanctification.” And Jonathan and Saul were discovered, but the people were released.
Ndipo Sauli anapemphera kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, “Chifukwa chiyani simunandiyankhe ine mtumiki wanu lero lino? Ngati tchimoli lipezeka ndi ine kapena ndi Yonatani mwana wanga, Inu Mulungu wa Israeli, aoneke ndi Urimu. Koma ngati wochimwa ndi anthu anu, Aisraeli aoneke Tamimu.” Maere anagwera Sauli ndi Yonatani ndipo anthu anapezeka osalakwa.
42 And Saul said, “Cast lots between myself and Jonathan, my son.” And Jonathan was caught.
Sauli anati, “Chitani maere pakati pa ine ndi Yonatani mwana wanga.” Ndipo maere anagwera Yonatani.
43 Then Saul said to Jonathan, “Tell me what you have done.” And Jonathan revealed to him, and said: “Truly, I tasted a little honey with the top of the staff that was in my hand. And behold, I shall die.”
Kenaka Sauli anati kwa Yonatani, “Ndiwuze chimene wachita.” Ndipo Yonatani anamuwuza kuti, “Ine ndinangolawa uchi pangʼono ndi ndodo yangayi. Ndiye ine ndili wokonzeka kufa.”
44 And Saul said, “May God do these things to me, and may he add these other things, for you shall surely die, Jonathan!”
Sauli anati, “Mulungu andilange ngakhale kufa kumene, ngati sufa iwe Yonatani.”
45 And the people said to Saul: “Why should Jonathan have to die, who has accomplished this great salvation in Israel? This is wrong. As the Lord lives, not one hair of his head should fall to the ground. For he has wrought with God this day.” Therefore, the people freed Jonathan, so that he would not die.
Koma anthuwo anafunsa Saulo kuti, “Kodi Yonatani afe, iye amene wagwira ntchito iyi yayikulu yopulumutsa Aisraeli? Osatheka! Pali Yehova ngakhale tsitsi ndi limodzi lomwe lapamutu pake silidzathothoka, pakuti wachita zimenezi lero ndi thandizo la Mulungu.” Choncho anthuwo anamupulumutsa Yonatani, ndipo sanaphedwe.
46 And Saul withdrew, and he did not pursue the Philistines. And the Philistines went away to their own places.
Pambuyo pake Sauli analeka kulondola Afilisti, kenaka anabwerera ku dziko lawo.
47 And Saul, his kingdom having been confirmed over Israel, was fighting against all his enemies on all sides: against Moab, and the sons of Ammon, and Edom, and the kings of Zobah, and the Philistines. And wherever he turned himself, he was successful.
Sauli ali mtsogoleri wa Israeli, anachita nkhondo ndi adani awa omuzungulira: Mowabu, Amoni, Edomu mafumu a ku Zoba ndi Afilisti. Kulikonse kumene ankapita ankawagonjetsa.
48 And gathering together an army, he struck Amalek. And he rescued Israel from the hand of those who would lay waste to them.
Anachita nkhondo mwamphamvu ndi kugonjetsa Aamaleki. Choncho anapulumutsa Aisraeli mʼmanja mwa anthu amene ankawalanda zinthu zawo.
49 Now the sons of Saul were Jonathan, and Ishvi, and Malchishua. And as for the names of his two daughters: the name of the firstborn daughter was Merab, and the name of the younger one was Michal.
Ana aamuna a Sauli anali Yonatani, Isivi ndi Maliki-Suwa. Analinso ndi ana aakazi awiri, dzina la mwana wake wamkulu wamkazi linali Merabi ndipo la mwana wake wamngʼono wamkazi linali Mikala.
50 And the name of the wife of Saul was Ahinoam, the daughter of Ahimaaz. And the name of the first ruler of his military was Abner, the son of Ner, the first cousin of Saul.
Dzina la mkazi wake linali Ahinoamu. Iyeyu anali mwana wa Ahimaazi. Dzina la mkulu wa ankhondo a Sauli linali Abineri mwana wa Neri, mʼbale wa abambo a Sauli.
51 For Kish was the father of Saul, and Ner was the father of Abner, and the son of Abiel.
Kisi abambo a Sauli ndi Neri abambo a Abineri anali ana a Abieli.
52 Now there was a powerful war against the Philistines during all the days of Saul. And so, whomever Saul had seen to be a strong man, and fit for battle, he joined him to himself.
Pa moyo wake wonse, Sauli ankakhalira kuchita nkhondo pakati pa Israeli ndi Afilisti. Ndipo Sauli ankati akaona munthu aliyense wamphamvu kapena wolimba mtima ankamulemba ntchito mu gulu lake lankhondo.