< Proverbs 19 >
Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
3 The folly of a man spoils his ways: and he blames God in his heart.
Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
4 Wealth acquires many friends; but the poor is deserted even of the friend he has.
Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
5 A false witness shall not be unpunished, and he that accuses unjustly shall not escape.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
6 Many court the favour of kings; but every bad man becomes a reproach to [another] man.
Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
7 Every one who hates [his] poor brother shall also be far from friendship. Good understanding will draw near to them that know it, and a sensible man will find it. He that does much harm perfects mischief; and he that used provoking words shall not escape.
Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
8 He that procures wisdom loves himself; and he that keeps wisdom shall find good.
Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
9 A false witness shall not be unpunished; and whoever shall kindle mischief shall perish by it.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
10 Delight does not suit a fool, nor [is it seemly] if a servant should begin to rule with haughtiness.
Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
11 A merciful man is longsuffering; and his triumph overtakes transgressors.
Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
12 The threatening of a king is like the roaring of a lion; but as dew on the grass, so is his favour.
Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
13 A foolish son is a disgrace to his father: vows [paid out] of the hire of a harlot are not pure.
Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
14 Fathers divide house and substance to [their] children: but a wife is suited to a man by the Lord.
Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
15 Cowardice possesses the effeminate [man]; and the soul of the sluggard shall hunger.
Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
16 He that keeps the commandment keeps his own soul; but he that despises his ways shall perish.
Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
17 He that has pity on the poor lends to the Lord; and he will recompense to him according to his gift.
Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
18 Chasten your son, for so he shall be hopeful; and be not exalted in your soul to haughtiness.
Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
19 A malicious man shall be severely punished, and if he commit injury, he shall also lose his life.
Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
20 Hear, son, the instruction of your father, that you may be wise at your latter end.
Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
21 [There are] many thoughts in a man's heart; but the counsel of the Lord abides for ever.
Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
22 Mercy is a fruit to a man: and a poor man is better than a rich liar.
Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
23 The fear of the Lord is life to a man: and he shall lodge without fear in places where knowledge is not seen.
Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
24 He that unjustly hides his hands in his bosom, will not even [bring] them up to his mouth.
Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
25 When a pestilent character is scourged, a simple man is made wiser: and if you reprove a wise man, he will understand discretion.
Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
26 He that dishonours his father, and drives away his mother, shall be disgraced and shall be exposed to reproach.
Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
27 A son who ceases to attend to the instruction of a father will cherish evil designs.
Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
28 He that becomes surety for a foolish child will despise the ordinance: and the mouth of ungodly men shall drink down judgement.
Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
29 Scourges are preparing for the intemperate, and punishments likewise for fools.
Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.