< Numbers 29 >

1 And in the seventh month, on the first day of the month, there shall be to you a holy convocation: you shall do no servile work: it shall be to you a day of blowing the trumpets.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 And you shall offer whole burnt offerings for a sweet savour to the Lord, one calf of the herd, one ram, seven lambs of a year old without blemish.
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 Their meat-offering shall be fine flour mingled with oil; three tenth deals for one calf, and two tenth deals for one ram:
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 a tenth deal for each several ram, for the seven lambs.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 And one kid of the goats for a sin-offering, to make atonement for you.
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 Beside the whole burnt offerings for the new moon, and their meat-offerings, and their drink-offerings, and their perpetual whole burnt offering; and their meat-offerings and their drink-offerings according to their ordinance for a sweet smelling savour to the Lord.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 And on the tenth of this month there shall be to you a holy convocation; and you shall afflict your souls, and you shall do no work.
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 And you shall bring near whole burnt offerings for a sweet smelling savour to the Lord; burnt sacrifices to the Lord, one calf of the herd, one ram, seven lambs of a year old; they shall be to you without blemish.
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 Their meat-offering shall be fine flour mingled with oil; three tenth deals for one calf, and two tenth deals for one ram.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 A tenth deal for each several lamb, for the seven lambs.
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 And one kid of the goats for a sin-offering, to make atonement for you; beside the sin-offering for atonement, and the continual whole burnt offering, its meat-offering, and its drink-offering according to its ordinance for a smell of sweet savour, a burnt sacrifice to the Lord.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 And on the fifteenth day of this seventh month you shall have a holy convocation; you shall do no servile work; and you shall keep it a feast to the Lord seven days.
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 And you shall bring near whole burnt offerings, a sacrifice for a smell of sweet savour to the Lord, on the first day thirteen calves of the herd, two rams, fourteen lambs of a year old; they shall be without blemish.
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 their meat-offerings [shall be] fine flour mingled with oil; there shall be three tenth deals for one calf, for the thirteen calves; and two tenth deals for one ram, for the two rams.
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 A tenth deal for every lamb, for the fourteen lambs.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 And one kid of the goats for a sin-offering; beside the continual whole burnt offering: there shall be their meat-offerings and their drink-offerings.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 And on the second day twelve calves, two rams, fourteen lambs of a year old without blemish.
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 Their meat-offering and their drink-offering shall be for the calves and the rams and the lambs according to their number, according to their ordinance.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 And one kid of the goats for a sin-offering; beside the perpetual whole burnt offering; their meat-offerings and their drink-offerings.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 On the third day eleven calves, two rams, fourteen lambs of a year old without blemish.
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 Their meat-offering and their drink-offering shall be to the calves and to the rams and to the lambs according to their number, according to their ordinance.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 And one kid of the goats for a sin-offering; beside the continual whole burnt offering; [there shall be] their meat-offerings and their drink-offerings.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 On the fourth day ten calves, two rams, fourteen lambs of a year old without spot.
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 There shall be their meat-offerings and their drink-offerings to the calves and the rams and the lambs according to their number, according to their ordinance.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 And one kid of the goats for a sin-offering; beside the continual whole burnt offering [there shall be] their meat-offerings and their drink-offerings.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 On the fifth day nine calves, two rams, fourteen lambs of a year old without spot.
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 Their meat-offerings and their drink-offerings [shall be] to the calves and the rams and the lambs according to their number, according to their ordinance.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 And one kid of the goats for a sin-offering; beside the perpetual whole burnt offering; [there shall be] their meat-offerings and their drink-offerings.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 On the sixth day eight calves, two rams, fourteen lambs of a year old without blemish.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 There shall be their meat-offerings and their drink-offerings to the calves and rams and lambs according to their number, according to their ordinance.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 And one kid of the goats for a sin-offering; beside the perpetual whole burnt offering; [there shall be] their meat-offerings and their drink-offerings.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 On the seventh day seven calves, two rams, fourteen lambs of a year old without blemish.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 Their meat-offerings and their drink-offerings shall be to the calves and the rams and the lambs according to their number, according to their ordinance.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 And one kid of the goats for a sin-offering; beside the continual whole burnt offering; [there shall be] their meat-offerings and their drink-offerings.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 And on the eighth day there shall be to you a release: you shall do no servile work in it.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 And you shall offer whole burnt offerings [as] sacrifices to the Lord, one calf, one ram, seven lambs of a year old without spot.
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 [There shall be] their meat-offerings and their drink-offerings for the calf and the ram and the lambs according to their number, according to their ordinance.
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 And one kid of the goats for a sin-offering; beside the continual whole burnt offering; [there shall be] their meat-offerings and their drink-offerings.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 These [sacrifices] shall you offer to the Lord in your feasts, besides your vows; and [you shall offer] your free will offerings and your whole burnt offerings, and your meat-offerings and your drink-offerings, and your peace-offerings.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 And Moses spoke to the children of Israel according to all that the Lord commanded Moses.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< Numbers 29 >