< Leviticus 19 >
1 And the Lord spoke to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Speak to the congregation of the children of Israel, and you shall say to them, You shall be holy; for I the Lord your God [am] holy.
“Uza gulu lonse la Aisraeli kuti, ‘Khalani oyera mtima chifukwa Ine, Yehova Mulungu wanu, ndine Woyera.
3 Let every one of you reverence his father and his mother; and you shall keep my sabbaths: I [am] the Lord your God.
“‘Aliyense mwa inu azilemekeza abambo ake ndi amayi ake. Ndipo muzisunga masabata anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
4 You shall not follow idols, and you shall not make to yourselves molten gods: I [am] the Lord your God.
“‘Musatembenukire ku mafano kapena kudzipangira nokha milungu ya zitsulo zosungunula. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
5 And if you will sacrifice a peace-offering to the Lord, you shall offer it acceptable from yourselves.
“‘Pamene mukupereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, muyipereke mwanjira yoti ilandiridwe.
6 In what day soever you shall sacrifice it, it shall be eaten; and on the following day, and if any of it should be left till the third day, it shall be thoroughly burnt with fire.
Nsembe izidyedwa tsiku lomwe mwayiperekalo kapena mmawa mwake. Chilichonse chotsala mpaka tsiku lachitatu chiyenera kutenthedwa.
7 And if it should be at all eaten on the third day, it is unfit for sacrifice: it shall not be accepted.
Ngati mudya choperekacho tsiku lachitatu, ndiye kuti mwachita chonyansa ndipo chakudyacho sichidzalandiridwa.
8 And he that eats it shall bear his iniquity, because he has profaned the holy things of the Lord; and the souls that eat it shall be destroyed from amongst their people.
Munthu aliyense amene adya chakudyacho adzasenza machimo ake chifukwa wayipitsa chinthu chimene ndi choyera kwa Yehova. Munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.
9 And when you reap the harvest of your land, you shall not complete the reaping of your field with exactness, and you shall not gather that which falls from your reaping.
“‘Pamene mukolola zinthu mʼmunda mwanu musakolole mpaka mʼmphepete mwa munda, ndipo musatole khunkha lake.
10 And you shall not go over the gathering of your vineyard, neither shall you gather the remaining grapes of your vineyard: you shall leave them for the poor and the stranger: I am the Lord your God.
Musakolole mphesa zonse mʼmunda wanu wa mpesa kapena kutola mphesa zakugwa mʼmundamo. Zimenezi muzisiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wako.
11 You shall not steal, you shall not lie, neither shall one bear false witness as an informer against his neighbour.
“‘Musabe. “‘Musamanamizane. “‘Musachitirane zinthu mwachinyengo.
12 And you shall not swear unjustly by my name, and you shall not profane the holy name of your God: I am the Lord your God.
“‘Musalumbire mʼdzina langa monyenga popeza kutero ndi kuyipitsa dzina la Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
13 You shall not injure your neighbour, neither do you rob [him], neither shall the wages of your hireling remain with you until the morning.
“‘Musapsinje mnzanu kapena kumulanda zinthu zake. “‘Musasunge malipiro a munthu wantchito usiku wonse mpaka mmawa.
14 You shall not revile the deaf, neither shall you put a stumbling block in the way of the blind; and you shall fear the Lord your God: I am the Lord your God.
“‘Musatemberere wosamva kapena kuyikira munthu wosaona chinthu choti apunthwe nacho patsogolo pake, koma muziopa Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
15 You shall not act unjustly in judgement: you shall not accept the person of the poor, nor admire the person of the mighty; with justice shall you judge your neighbour.
“‘Musamaweruze mopanda chilungamo. Musachite tsankho pakati pa osauka ndi olemera, koma muweruze mlandu wa mnzanu mwachilungamo.
16 You shall not walk deceitfully amongst your people; you shall not rise up against the blood of your neighbour: I am the Lord your God.
“‘Musamapite uku ndi uku kunena bodza pakati pa anthu anu. “‘Musachite kanthu kalikonse kamene kangadzetse imfa kwa mnzanu. Ine ndine Yehova.
17 You shall not hate your brother in your heart: you shall in any wise rebuke your neighbour, so you shall not bear sin on his account.
“‘Musamude mʼbale wanu mu mtima mwanu. Koma mudzudzuleni mnzanu moona mtima kuti musakhale wolakwa.
18 And your hand shall not avenge you; and you shall not be angry with the children of your people; and you shall love your neighbour as yourself; I am the Lord.
“‘Musamubwezere mnzanu choyipa kapena kumusungira kanthu kunkhosi, koma konda mnansi wako monga iwe mwini. Ine ndine Yehova.
19 You shall observe my law: you shall not let your cattle gender with one of a different kind, and you shall not sow your vineyard with diverse seed; and you shall not put upon yourself a mingled garment woven of two [materials].
“‘Muzisunga malangizo anga. “‘Tsono musamalole kuti ngʼombe zanu zikwerane ndi chiweto cha mtundu wina. “‘Ndiponso musamadzale mbewu za mitundu iwiri mʼmunda umodzi. “‘Musavale chovala chopangidwa ndi nsalu za mitundu iwiri.
20 And if any one lie carnally with a woman, and she should be a home-servant kept for a man, and she has not been ransomed, [and] her freedom has not been given to her, they shall be visited [with punishment]; but they shall not die, because she was not set at liberty.
“‘Ngati munthu agonana ndi kapolo wamkazi amene wafunsidwa mbeta ndi munthu wina, koma sanawomboledwe kapenanso kulandira ufulu wake, alangidwe. Koma onsewa asaphedwe, chifukwa mkaziyo anali asanalandire ufulu wake.
21 And he shall bring for his trespass to the Lord to the door of the tabernacle of witness, a ram for a trespass-offering.
Koma mwamunayo abwere ndi nsembe yopepesera kupalamula kwa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano. Nsembe yake ikhale nkhosa yayimuna
22 And the priest shall make atonement for him with the ram of the trespass-offering, before the Lord, for the sin which he sinned; and the sin which he sinned shall be forgiven him.
ndipo wansembe achite nayo mwambo wopepesera chifukwa cha kupalamula kumene anachita pamaso pa Yehova. Akatero tchimo lake lidzakhululukidwa.
23 And whenever you shall enter into the land which the Lord your God gives you, and shall plant any fruit tree, then shall you purge away its uncleanness; its fruit shall be three years uncleansed to you, it shall not be eaten.
“‘Mukadzalowa mʼdzikomo ndi kudzala mtengo wa mtundu uliwonse wa zipatso, zipatso zakezo mudzaziyese ngati zodetsedwa. Ndiye kuti kwa zaka zitatu zidzakhale zoletsedwa kwa inu. Musadzazidye nthawi imeneyi.
24 And in the fourth year all its fruit shall be holy, a subject of praise to the Lord.
Chaka chachinayi, zipatso zake zonse zidzakhala zopatulika, ndipo zidzakhala chopereka cha matamando kwa Yehova.
25 And in the fifth year you shall eat the fruit, its produce is an increase to you. I am the Lord your God.
Koma chaka chachisanu, mudzatha kudya zipatso zake kuti mitengoyo idzakubalireni zochuluka. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
26 Eat not on the mountains, nor shall you employ auguries, nor divine by inspection of birds.
“‘Musadye nyama ya magazi. “‘Musamawombeze kapena kuchita zamatsenga.
27 You shall not make a round cutting of the hair of your head, nor disfigure your beard.
“‘Musamamete mduliro kapena kumeta mʼmphepete mwa ndevu zanu.
28 And you shall not make cuttings in your body for a [dead] body, and you shall not inscribe on yourselves any marks. I am the Lord your God.
“‘Musadzichekecheke pathupi panu chifukwa cha munthu wakufa kapena kudzitema mphini pa thupi lanu. Ine ndine Yehova.
29 You shall not profane your daughter to prostitute her; so the land shall not go a whoring, and the land be filled with iniquity.
“‘Musamuyipitse mwana wanu wamkazi pomusandutsa mkazi wachiwerewere. Mukatero dziko lidzasanduka la anthu achiwerewere ndi lodzaza ndi zoyipa.
30 You shall keep my sabbaths, and reverence my sanctuaries: I am the Lord.
“‘Muzisunga Masabata anga ndipo muzilemekeza malo anga opatulika. Ine ndine Yehova.
31 You shall not attend to those who have in them divining spirits, nor attach yourselves to enchanters, to pollute yourselves with them: I am the Lord your God.
“‘Musamapite kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kapena kwa owombeza. Musamawafunefune kuti angakuyipitseni. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
32 You shall rise up before the hoary head, and honour the face of the old man, and shall fear your God: I am the Lord your God.
“‘Muzikhala mwa ulemu pamaso pa munthu wachikulire, ndipo muzichitira ulemu munthu wokalamba. Kumeneko ndiye kuopa Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
33 And if there should come to you a stranger in your land, you shall not afflict him.
“‘Pamene mlendo akhala nanu mʼdziko mwanu, musamuzunze.
34 The stranger that comes to you shall be amongst you as the native, and you shall love him as yourself; for you were strangers in the land of Egypt: I am the Lord your God.
Mlendo amene akhala nanu akhale ngati mmodzi mwa mbadwa zanu. Mumukonde monga momwe mumadzikondera inu nomwe. Paja inu munali alendo mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
35 You shall not act unrighteously in judgement, in measures and weights and scales.
“‘Musamachite za chinyengo poweruza mlandu, kapena poyeza utali, kulemera ngakhalenso kuchuluka kwa zinthu.
36 There shall be amongst you just balances and just weights and just liquid measure. I am the Lord your God, who brought you out of the land of Egypt.
Miyeso ya sikelo, miyeso yoyezera kulemera kwa zinthu, miyeso yotchedwa efa ndi miyeso yotchedwa hini zikhale zolungama. Ine ndine Yehova, Mulungu wanu amene ndinakutulutsani ku dziko la Igupto.
37 And you shall keep all my law and all my ordinances, and you shall do them: I am the Lord your God.
“‘Choncho muzisunga malangizo ndi malamulo angawa ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.’”