< Psalms 45 >
1 For the end, for alternate [strains] by the sons of Core; for instruction, a Song concerning the beloved. My heart has uttered a good matter: I declare my works to the king: my tongue is the pen of a quick writer.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
2 Thou art more beautiful than the sons of men: grace has been shed forth on thy lips: therefore God has blessed thee for ever.
Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
3 Gird thy sword upon thy thigh, O Mighty One, in thy comeliness, and in thy beauty;
Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
4 and bend [thy bow], and prosper, and reign, because of truth and meekness and righteousness; and thy right hand shall guide thee wonderfully.
Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
5 Thy weapons are sharpened, Mighty One, (the nations shall fall under thee) [they are] in the heart of the king's enemies.
Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
6 Thy throne, O God, is for ever and ever: the sceptre of thy kingdom is a sceptre of righteousness.
Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
7 Thou hast loved righteousness, and hated iniquity: therefore God, thy God, has anointed thee with the oil of gladness beyond thy fellows.
Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
8 Myrrh, and stacte, and cassia [are exhaled] from thy garments, [and] out of the ivory palaces,
Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
9 with which kings' daughters have gladdened thee for thine honour: the queen stood by on thy right hand, clothed in vesture wrought with gold, [and] arrayed in divers colours.
Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
10 Hear, O daughter, and see, and incline thine ear; forget also thy people, and thy father's house.
Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
11 Because the king has desired thy beauty; for he is thy Lord.
Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
12 And the daughter of Tyre shall adore him with gifts; the rich of the people of the land shall supplicate thy favour.
Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
13 All her glory [is that] of the daughter of the king of Esebon, robed [as she is] in golden fringed garments,
Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
14 in embroidered [clothing]: virgins shall be brought to the king after her: her fellows shall be brought to thee.
Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
15 They shall be brought with gladness and exultation: they shall be led into the king's temple.
Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
16 Instead of thy fathers children are born to thee: thou shalt make them princes over all the earth.
Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
17 They shall make mention of thy name from generation to generation: therefore shall the nations give thanks to thee for ever, even for ever and ever.
Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.