< Jezekiel 16 >

1 Moreover the word of the Lord came to me, saying,
Yehova anayankhula nane kuti,
2 Son of man, testify to Jerusalem [of] her iniquities;
“Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa.
3 and thou shalt say, Thus saith the Lord to Jerusalem; Thy root and thy birth are of the land of Chanaan: thy father was an Amorite, and thy mother a Chettite.
Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti.
4 And [as for] thy birth in the day wherein thou wast born, thou didst not bind thy breasts, and thou wast not washed in water, neither wast thou salted with salt, neither wast thou swathed in swaddling-bands.
Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu.
5 Nor did mine eye pity thee, to do for thee one of all these things, to feel at all for thee; but thou wast cast out on the face of the field, because of the deformity of thy person, in the day wherein thou wast born.
Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.
6 And I passed by to thee, and saw thee polluted in thy blood; and I said to thee, [Let there be] life out of thy blood:
“‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’
7 increase; I have made thee as the springing grass of the field. So thou didst increase and grow, and didst enter into great cities: thy breasts were set, and thy hair grew, whereas thou wast naked and bare.
ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.
8 And I passed by thee and saw thee, and, behold, [it was] thy time and a time of resting; and I spread my wings over thee, and covered thy shame, and swear to thee: and I entered into covenant with thee, saith the Lord, and thou becamest mine.
“‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.
9 And I washed thee in water, and washed thy blood from thee, and anointed thee with oil.
“‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta.
10 And I clothed thee with embroidered [garments], and clothed thee beneath with purple, and girded thee with fine linen, and clothed thee with silk,
Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta.
11 and decked thee also with ornaments, and put bracelets on thine hands, and a necklace on thy neck.
Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako,
12 And I put a pendant on thy nostril, and rings in thine ears, and a crown of glory on thine head.
ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako.
13 So thou wast adorned with gold and silver; and thy raiment was of fine linen, and silk, and variegated work: thou didst eat fine flour, and oil, and honey, and didst become extremely beautiful.
Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi.
14 And thy name went forth among the nations for thy beauty: because it was perfected with elegance, [and] in the comeliness which I put upon thee, saith the Lord.
Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.
15 Thou didst trust in thy beauty, and didst go a-whoring because of thy renown, and didst pour out thy fornication on every passer by.
“‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake.
16 And thou didst take of thy garments, and madest to thyself idols of needlework, and didst go a-whoring after them; therefore thou shalt never come in, nor shall [the like] take place.
Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso.
17 And thou tookest thy fair ornaments of my gold and of my silver, of what I gave thee, and thou madest to thyself male images, and thou didst commit whoredom with them.
Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama.
18 And thou didst take thy variegated apparel and didst clothe them, and thou didst set before them mine oil and mine incense.
Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo.
19 And [thou tookest] my bread which I gave thee, ([yea] I fed thee with fine flour and oil and honey) and didst set them before them for a sweet-smelling savour: yea, it was so, saith the Lord.
Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
20 And thou tookest thy sons and thy daughters, whom thou borest, and didst sacrifice [these] to them to be destroyed. Thou didst go a-whoring as [if that were] little,
“‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire
21 and didst slay thy children, and gavest them up in offering them to them for an expiation.
kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo?
22 This is beyond all thy fornication, and thou didst not remember thine infancy, when thou wast naked and bare, [and] didst live [though] defiled in thy blood.
Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.
23 And it came to pass after all thy wickedness, saith the Lord,
“‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse,
24 that thou didst build thyself a house of fornication, and didst make thyself a public place in every street;
wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse.
25 and on the head of every way thou didst set up thy fornications, and didst defile thy beauty, and didst open thy feet to every passer by, and didst multiply thy fornication.
Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo.
26 And thou didst go a-whoring after the children of Egypt thy neighbors, great of flesh; and didst go a-whoring, often to provoke me to anger.
Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako.
27 And if I stretch out my hand against thee, then will I abolish thy statutes, and deliver [thee] up to the wills of them that hate thee, [even to] the daughters of the Philistines that turned thee aside from the way wherein thou sinned.
Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa.
28 And thou didst go a-whoring to the daughters of Assur, and not even thus wast thou satisfied; yea, thou didst go a-whoring, and wast not satisfied.
Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe.
29 And thou didst multiply thy covenants with the land of the Chaldeans; and not even with these wast thou satisfied.
Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.
30 Why should I make a covenant with thy daughter, saith the Lord, while thou doest all these things, the works of a harlot? and thou hast gone a-whoring in a threefold degree with thy daughters.
“‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi.
31 Thou hast built a house of harlotry in every top of a way, and hast set up thine high place in every street; and thou didst become as a harlot gathering hires.
Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.
32 An adulteress resembles thee, taking rewards of her husband.
“‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako!
33 She has even given rewards to all that went a-whoring after her, and thou hast given rewards to all thy lovers, yea, thou didst load them with rewards, that they should come to thee from every side for thy fornication.
Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe.
34 And there has happened in thee perverseness in thy fornication beyond [other] women, and they have committed fornication with thee, in that thou givest hires over and above, and hires were not given to thee; and [thus] perverseness happened in thee.
Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.
35 Therefore, harlot, hear the word of the Lord:
“‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova!
36 Thus saith the Lord, Because thou hast poured forth thy money, therefore thy shame shall be discovered in thy harlotry with thy lovers, and [with] regard to all the imaginations of thine iniquities, and for the blood of thy children which thou hast given to them.
Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano,
37 Therefore, behold, I [will] gather all thy lovers with whom thou hast consorted, and all whom thou hast loved, with all whom thou didst hate; and I will gather them against thee round about, and will expose thy wickedness to them, and they shall see all thy shame.
nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse.
38 And I will be avenged on thee with the vengeance of an adulteress, and I will bring upon thee blood of fury and jealousy.
Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri.
39 And I will deliver thee into their hands, and they shall break down thy house of harlotry, and destroy thine high place; and they shall strip thee of thy garments, and shall take thy proud ornaments, and leave thee naked and bare.
Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa.
40 And they shall bring multitudes upon thee, and they shall stone thee with stones, and pierce thee with their swords.
Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo.
41 And they shall burn thine houses with fire, and shall execute vengeance on thee in the sight of many women: and I will turn thee back from harlotry, and I will no more give [thee] rewards.
Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako.
42 So will I slacken my fury against thee, and my jealousy shall be removed from thee, and I will rest, and be no more careful [for thee].
Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.
43 Because thou didst not remember thine infancy, and thou didst grieve me in all these things; therefore, behold, I have recompensed thy ways upon thine head, saith the Lord: for thus hast thou wrought ungodliness above all thine [other] iniquities.
“‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.
44 These are all the things they have spoken against thee in a proverb, saying,
“‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’
45 As is the mother, so is thy mother's daughter: thou art she that has rejected her husband and her children; and the sisters of thy sisters have rejected their husbands and their children: your mother was a Chettite, and [your] father an Amorite.
Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori.
46 Your elder sister who dwells on thy left hand is Samaria, she and her daughters: and thy younger sister, that dwells on the right hand, is Sodom and her daughters.
Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi.
47 Yet notwithstanding thou hast not walked in their ways, neither hast thou done according to their iniquities within a little, but thou hast exceeded them in all thy ways.
Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo.
48 [As] I live, saith the Lord, this Sodom and her daughters have not done as thou and thy daughters have done.
Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.
49 Moreover this was the sin of thy sister Sodom, pride: she and her daughters lived in pleasure, in fullness of bread [and] in abundance: this belonged to her and her daughters, and they helped not the hand of the poor and needy.
“‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi.
50 And they boasted, and wrought iniquities before me: so I cut them off as I saw [fit].
Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu.
51 Also Samaria has not sinned according to half of thy sins; but thou hast multiplied thine iniquities beyond them, and thou hast justified thy sisters in all thine iniquities which thou hast committed.
Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye.
52 Thou therefore bear thy punishment, for that thou hast corrupted thy sisters by thy sins which thou hast committed beyond them; and thou hast made them [appear] more righteous than thyself: thou therefore be ashamed, and bear thy dishonour, in that thou hast justified thy sisters.
Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.
53 And I will turn their captivity, [even] the captivity of Sodom and her daughters; and I will turn the captivity of Samaria and her daughters; and I will turn thy captivity in the midst of them:
“‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu.
54 that thou mayest bear thy punishment, and be dishonoured for all that thou hast done in provoking me to anger.
Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa.
55 And thy sister Sodom and her daughters shall be restored as they were at the beginning, and thou and thy daughters shall be restored as ye were at the beginning.
Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja.
56 And surely thy sister Sodom was not mentioned by thy mouth in the days of thy pride:
Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu
57 before thy wickedness was discovered, even now thou art the reproach of the daughters of Syria, and of all that are round about her, [even] of the daughters of the Philistines that compass thee round about.
kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza.
58 [As for] thine ungodliness and thine iniquities, thou hast borne them, saith the Lord.
Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.
59 Thus saith the Lord; I will even do to thee as thou hast done, as thou hast dealt shamefully in these things to transgress my covenant.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa.
60 And I will remember my covenant [made] with thee in the days of thine infancy, and I will establish to thee an everlasting covenant.
Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe.
61 Then thou shalt remember thy way, and shalt be utterly dishonoured when thou receivest thine elder sisters with thy younger ones: and I will give them to thee for building up, but not by thy covenant.
Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe.
62 And I will establish my covenant with thee; and thou shalt know that I am the Lord:
Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
63 that thou mayest remember, and be ashamed, and mayest no more be able to open thy mouth for thy shame, when I am reconciled to thee for all that thou hast done, saith the Lord.
Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’”

< Jezekiel 16 >