< Psalms 88 >

1 A Song. A Psalm. Of the sons of Korah. To the chief music-maker; put to Mahalath Leannoth. Maschil. Of Heman the Ezrahite. O Lord, God of my salvation, I have been crying to you for help by day and by night:
Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
2 Let my prayer come before you; give ear to my cry:
Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
3 For my soul is full of evils, and my life has come near to the underworld. (Sheol h7585)
Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
4 I am numbered among those who go down into the earth; I have become like a man for whom there is no help:
Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
5 My soul is among the dead, like those in the underworld, to whom you give no more thought; for they are cut off from your care.
Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
6 You have put me in the lowest deep, even in dark places.
Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
7 The weight of your wrath is crushing me, all your waves have overcome me. (Selah)
Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
8 You have sent my friends far away from me; you have made me a disgusting thing in their eyes: I am shut up, and not able to come out.
Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
9 My eyes are wasting away because of my trouble: Lord, my cry has gone up to you every day, my hands are stretched out to you.
maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
10 Will you do works of wonder for the dead? will the shades come back to give you praise? (Selah)
Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
11 Will the story of your mercy be given in the house of the dead? will news of your faith come to the place of destruction?
Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
12 May there be knowledge of your wonders in the dark? or of your righteousness where memory is dead?
Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
13 But to you did I send up my cry, O Lord; in the morning my prayer came before you.
Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
14 Lord, why have you sent away my soul? why is your face covered from me?
Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
15 I have been troubled and in fear of death from the time when I was young; your wrath is hard on me, and I have no strength.
Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
16 The heat of your wrath has gone over me; I am broken by your cruel punishments.
Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
17 They are round me all the day like water; they have made a circle about me.
Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
18 You have sent my friends and lovers far from me; I am gone from the memory of those who are dear to me.
Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.

< Psalms 88 >