< Psalms 87 >
1 Of the sons of Korah. A Psalm. A Song. This house is resting on the holy mountain.
Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
2 The Lord has more love for the doors of Zion than for all the tents of Jacob.
Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
3 Noble things are said of you, O town of God. (Selah)
Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
4 Rahab and Babylon will be named among those who have knowledge of me; see, Philistia and Tyre, with Ethiopia; this man had his birth there.
“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
5 And of Zion it will be said, This or that man had his birth there; and the Most High will make her strong.
Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
6 The Lord will keep in mind, when he is writing the records of the people, that this man had his birth there. (Selah)
Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
7 The players on instruments will be there, and the dancers will say, All my springs are in you.
Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”