< Psalms 74 >
1 Maschil. Of Asaph. Of God, why have you put us away from you for ever? why is the fire of your wrath smoking against the sheep who are your care?
Ndakatulo ya Asafu. Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu? Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
2 Keep in mind your band of worshippers, for whom you gave payment in the days which are past, whom you took for yourself as the people of your heritage; even this mountain of Zion, which has been your resting-place.
Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale, fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola, phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
3 Go up and see the unending destruction; all the evil which your haters have done in the holy place;
Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
4 Sending out their voices like lions among your worshippers; they have put up their signs to be seen.
Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe; anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
5 They are cutting down, like a man whose blade is lifted up against the thick trees.
Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo kuti adule mitengo mʼnkhalango.
6 Your doors are broken down with hammers and iron blades.
Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo zonse zimene tinapachika.
7 They have put on fire your holy place; they have made the place of your name unclean, pulling it down to the earth.
Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi; anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
8 They have said in their hearts, Let us put an end to them all together; they have given over to the fire all God's places of worship in the land.
Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.” Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
9 We do not see our signs: there is no longer any prophet, or anyone among us to say how long.
Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa; palibe aneneri amene atsala ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
10 O God, how long will those who are against us say cruel things? will the hater go on looking down on your name for ever?
Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu? Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
11 Why are you keeping back your hand, and covering your right hand in your robe?
Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja? Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
12 For from the past God is my King, working salvation in the earth.
Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale; Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
13 The sea was parted in two by your strength; the heads of the great sea-beasts were broken.
Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu; munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
14 The heads of the great snake were crushed by you; you gave them as food to the fishes of the sea.
Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
15 You made valleys for fountains and springs; you made the ever-flowing rivers dry.
Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje, munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
16 The day is yours and the night is yours: you made the light and the sun.
Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso; Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
17 By you all the limits of the earth were fixed; you have made summer and winter.
Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi; munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
18 Keep this in mind, O Lord, that your haters have said cruel things, and that your name has been looked down on by a people of evil behaviour.
Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
19 O give not the soul of your dove to the hawk; let not the life of the poor go out of your memory for ever.
Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo; nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
20 Keep in mind your undertaking; for the dark places of the earth are full of pride and cruel acts.
Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
21 O let not the crushed be turned back in shame; let the low man and the poor give praise to your name.
Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi; osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
22 Up! O God, be the judge of your cause; keep in mind the bitter things which the man of evil behaviour says against you every day.
Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu; kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
23 Keep in mind the voice of your haters; the outcry of those who come against you goes up every day.
Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.