< Psalms 66 >

1 To the chief music-maker. A Song. A Psalm. Send up a glad cry to God, all the earth:
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 Make a song in honour of his name: give praise and glory to him.
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 Say to God, How greatly to be feared are your works! because of your great power your haters are forced to put themselves under your feet.
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 Let all the earth give you worship, and make songs to you; let them make songs to your name. (Selah)
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 Come and see the works of God: he is to be feared in all he does to the children of men.
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 The sea was turned into dry land: they went through the river on foot: there did we have joy in him.
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 He is ruling in power for ever; his eyes are watching the nations: may his haters have no strength against him. (Selah)
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 Give blessings to our God, O you peoples, let the voice of his praise be loud;
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
9 Because he gives us life, and has not let our feet be moved.
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 For you, O God, have put us to the test: testing us by fire like silver.
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
11 You let us be put in prison; chains were put on our legs.
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 You let men go driving over our heads; we went through fire and through water; but you took us out into a wide place.
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
13 I will come into your house with burned offerings, I will make payment of my debt to you,
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 Keeping the word which came from my lips, and which my mouth said, when I was in trouble.
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 I will give you burned offerings of fat beasts, and the smoke of sheep; I will make offerings of oxen and goats. (Selah)
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 Come, give ear to me, all you God-fearing men, so that I may make clear to you what he has done for my soul.
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 My voice went up to him, and I was lifted up from the underworld.
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
18 I said in my heart, The Lord will not give ear to me:
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 But truly God's ear has been open; he has give attention to the voice of my prayer.
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 Praise be to God who has not taken away his good faith and his mercy from me.
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!

< Psalms 66 >