< Psalms 43 >
1 Be my judge, O God, supporting my cause against a nation without religion; O keep me from the false and evil man.
Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu; ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza; mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
2 You are the God of my strength; why have you put me from you? why do I go in sorrow because of the attacks of my haters?
Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga. Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?
3 O send out your light and your true word; let them be my guide: let them take me to your holy hill, and to your tents.
Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu kuti zinditsogolere; mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera, kumalo kumene inu mumakhala.
4 Then I will go up to the altar of God, to the God of my joy; I will be glad and give praise to you on an instrument of music, O God, my God.
Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa. Ndidzakutamandani ndi zeze, Inu Mulungu wanga.
5 Why are you crushed down, O my soul? and why are you troubled in me? put your hope in God, for I will again give him praise who is my help and my God.
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandabe Iye, Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.