< Psalms 129 >

1 A Song of the going up. Great have been my troubles from the time when I was young (let Israel now say);
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
2 Great have been my troubles from the time when I was young, but my troubles have not overcome me.
“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
3 The ploughmen were ploughing on my back; long were the wounds they made.
Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
4 The Lord is true: the cords of the evil-doers are broken in two.
Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
5 Let all the haters of Zion be shamed and turned back.
Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
6 Let them be like the grass on the house-tops, which is dry before it comes to full growth.
Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
7 He who gets in the grain has no use for it; and they do not make bands of it for the grain-stems.
sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
8 And those who go by do not say, The blessing of the Lord be on you; we give you blessing in the name of the Lord.
Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”

< Psalms 129 >