< Psalms 119 >

1 ALEPH Happy are they who are without sin in their ways, walking in the law of the Lord.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Happy are they who keep his unchanging word, searching after him with all their heart.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 They do no evil; they go in his ways.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 You have put your orders into our hearts, so that we might keep them with care.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 If only my ways were ordered so that I might keep your rules!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Then I would not be put to shame, as long as I have respect for all your teaching.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 I will give you praise with an upright heart in learning your right decisions.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 I will keep your rules: O give me not up completely.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 BETH How may a young man make his way clean? by guiding it after your word.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 I have made search for you with all my heart: O let me not go wandering far from your teaching.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 I have kept your sayings secretly in my heart, so that I might do no sin against you.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Praise be to you, O Lord: give me knowledge of your rules.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 With my lips have I made clear all the decisions of your mouth.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 I have taken as much delight in the way of your unchanging word, as in all wealth.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 I will give thought to your orders, and have respect for your ways.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 I will have delight in your rules; I will not let your word go out of my mind.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 GIMEL Give me, your servant, the reward of life, so that I may keep your word;
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Let my eyes be open to see the wonders of your law.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 I am living in a strange land: do not let your teachings be kept secret from me.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 My soul is broken with desire for your decisions at all times.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Your hand has been against the men of pride, a curse is on those who go wandering out of your way.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Take away from me shame and bitter words; for I have kept your unchanging word in my heart.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Rulers make evil designs against me; but your servant gives thought to your rules.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Your unchanging word is my delight, and the guide of my footsteps.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 DALETH My soul is joined to the dust: O give me life, in keeping with your word.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 I put the record of my ways before you, and you gave me an answer: O give me knowledge of your rules.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Make the way of your orders clear to me; then my thoughts will be ever on your wonders.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 My soul is wasted with sorrow; give me strength again in keeping with your word
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Take from me every false way; and in mercy give me your law.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 I have taken the way of faith: I have kept your decisions before me.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 I have been true to your unchanging word; O Lord, do not put me to shame.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 I will go quickly in the way of your teaching, because you have given me a free heart.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 HE O Lord, let me see the way of your rules, and I will keep it to the end.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Give me wisdom, so that I may keep your law; going after it with all my heart.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Make me go in the way of your teachings; for they are my delight.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Let my heart be turned to your unchanging word, and not to evil desire.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Let my eyes be turned away from what is false; give me life in your ways.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Give effect to your word to your servant, in whose heart is the fear of you.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Take away the shame which is my fear; for your decisions are good.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 See how great is my desire for your orders: give me life in your righteousness.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 VAU Let your mercies come to me, O Lord, even your salvation, as you have said.
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 So that I may have an answer for the man who would put me to shame; for I have faith in your word.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 Take not your true word quite out of my mouth; for I have put my hope in your decisions.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 So that I may keep your law for ever and ever;
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 So that my way may be in a wide place: because my search has been for your orders.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 So that I may give knowledge of your unchanging word before kings, and not be put to shame.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 And so that I may take delight in your teachings, to which I have given my love.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 And so that my hands may be stretched out to you; and I will give thought to your rules.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 ZAIN Keep in mind your word to your servant, for on it has my hope been fixed.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 This is my comfort in my trouble; that your sayings have given me life.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 The men of pride have made great sport of me; but I have not been turned from your law.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 I have kept the memory of your decisions from times past, O Lord; and they have been my comfort.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 I am burning with wrath, because of the sinners who have given up your law.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Your rules have been melodies to me, while I have been living in strange lands.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 I have given thought to your name in the night, O Lord, and have kept your law.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 This has been true of me, that I have kept your orders in my heart.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 CHETH The Lord is my heritage: I have said that I would be ruled by your words.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 I have given my mind to do your pleasure with all my heart; have mercy on me, as you have said.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 I gave thought to my steps, and my feet were turned into the way of your unchanging word.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 I was quick to do your orders, and let no time be wasted.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 The cords of evil-doers are round me; but I have kept in mind your law.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 In the middle of the night I will get up to give you praise, because of all your right decisions.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 I keep company with all your worshippers, and those who have your orders in their memory.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 The earth, O Lord, is full of your mercy: give me knowledge of your rules.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 TETH You have done good to your servant, O Lord, in keeping with your word.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Give me knowledge and good sense; for I have put my faith in your teachings.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Before I was in trouble I went out of the way; but now I keep your word.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 You are good, and your works are good; give me knowledge of your rules.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 The men of pride have said false things about me; but I will keep your orders in my heart.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Their hearts are shut up with fat; but my delight is in your law.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 It is good for me to have been through trouble; so that I might come to the knowledge of your rules.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 The law of your mouth is better to me than thousands of gold and silver.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 JOD Your hands have made me, and given me form: give me wisdom, so that I may have knowledge of your teaching.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Your worshippers will see me and be glad; because my hope has been in your word.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 I have seen, O Lord, that your decisions are right, and that in unchanging faith you have sent trouble on me.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Let your mercy now be my comfort, as you have said to your servant.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Let your gentle mercies come to me, so that I may have life; for your law is my delight.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Let the men of pride be shamed; because they have falsely given decision against me; but I will give thought to your orders.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Let your worshippers be turned to me, and those who have knowledge of your words.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Let all my heart be given to your orders, so that I may not be put to shame.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 CAPH My soul is wasted with desire for your salvation: but I have hope in your word.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 My eyes are full of weariness with searching for your word, saying, When will you give me comfort?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 For I have become like a wine-skin black with smoke; but I still keep the memory of your rules.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 How short is the life of your servant! when will you give your decision against those who are attacking me?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 The men of pride, who are turned away from your law, have put nets for me.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 All your teachings are certain; they go after me with evil design; give me your help.
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 They had almost put an end to me on earth; but I did not give up your orders.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Give me life in your mercy; so that I may be ruled by the unchanging word of your mouth.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 LAMED For ever, O Lord, your word is fixed in heaven.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Your faith is unchanging from generation to generation: you have put the earth in its place, and it is not moved.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 They are ruled this day by your decisions; for all things are your servants.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 If your law had not been my delight, my troubles would have put an end to me.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 I will ever keep your orders in mind; for in them I have life.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 I am yours, O be my saviour; for my desire has been for your rules.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 The sinners have been waiting for me to give me up to destruction; but I will give all my mind to your unchanging ward.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 I have seen that nothing on earth is complete; but your teaching is very wide.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 MEM O what love I have for your law! I give thought to it all the day.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Your teaching has made me wiser than my haters: for it is mine for ever.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 I have more knowledge than all my teachers, because I give thought to your unchanging word.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 I have more wisdom than the old, because I have kept your orders.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 I have kept back my feet from all evil ways, so that I might be true to your word.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 My heart has not been turned away from your decisions; for you have been my teacher.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 How sweet are your sayings to my taste! truly, they are sweeter than honey in my mouth!
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Through your orders I get wisdom; for this reason I am a hater of every false way.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 NUN Your word is a light for my feet, ever shining on my way.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 I have made an oath and kept it, to be guided by your upright decisions.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 I am greatly troubled, O Lord, give me life in keeping with your word.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Take, O Lord, the free offerings of my mouth, and give me knowledge of your decisions.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 My soul is ever in danger; but I still keep the memory of your law.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Sinners have put a net to take me; but I was true to your orders.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 I have taken your unchanging word as an eternal heritage; for it is the joy of my heart.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 My heart is ever ready to keep your rules, even to the end.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 SAMECH I am a hater of men of doubting mind; but I am a lover of your law.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 You are my secret place and my breastplate against danger; my hope is in your word.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Go far from me, you evil-doers; so that I may keep the teachings of my God.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Be my support as you have said, and give me life; let not my hope be turned to shame.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Let me not be moved, and I will be safe, and ever take delight in your rules.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 You have overcome all those who are wandering from your rules; for all their thoughts are false.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 All the sinners of the earth are like waste metal in your eyes; and for this cause I give my love to your unchanging word.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 My flesh is moved for fear of you; I give honour to your decisions.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 AIN I have done what is good and right: you will not give me into the hands of those who are working against me.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Take your servant's interests into your keeping; let me not be crushed by the men of pride.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 My eyes are wasted with desire for your salvation, and for the word of your righteousness.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Be good to your servant in your mercy, and give me teaching in your rules.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 I am your servant; give me wisdom, so that I may have knowledge of your unchanging word.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 It is time, O Lord, for you to let your work be seen; for they have made your law without effect.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 For this reason I have greater love far your teachings than for gold, even for shining gold.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Because of it I keep straight in all things by your orders; and I am a hater of every false way.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 PE Your unchanging word is full of wonder; for this reason my soul keeps it.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 The opening of your words gives light; it gives good sense to the simple.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 My mouth was open wide, waiting with great desire for your teachings.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Let your eyes be turned to me, and have mercy on me, as it is right for you to do to those who are lovers of your name.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Let my steps be guided by your word; and let not sin have control over me.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Make me free from the cruel rule of man; then I will keep your orders.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Let your servant see the shining of your face; give me knowledge of your rules.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Rivers of water are flowing from my eyes, because men do not keep your law.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 TZADE O Lord, great is your righteousness, and upright are your decisions.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 You have given your unchanging word in righteousness, and it is for ever.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 My passion has overcome me; because my haters are turned away from your words.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Your word is of tested value; and it is dear to your servant.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 I am small and of no account; but I keep your orders in mind.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Your righteousness is an unchanging righteousness, and your law is certain.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Pain and trouble have overcome me: but your teachings are my delight.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 The righteousness of your unchanging word is eternal; give me wisdom so that I may have life.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 KOPH I have made my prayer with all my heart; give answer to me, O Lord: I will keep your rules.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 My cry has gone up to you; take me out of trouble, and I will be guided by your unchanging word.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Before the sun is up, my cry for help comes to your ear; my hope is in your words.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 In the night watches I am awake, so that I may give thought to your saying.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Let my voice come to you, in your mercy; O Lord, by your decisions give me life.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Those who have evil designs against me come near; they are far from your law.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 You are near, O Lord; and all your teachings are true.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 I have long had knowledge that your unchanging word is for ever.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 RESH O see my trouble, and be my saviour; for I keep your law in my mind,
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Undertake my cause, and come to my help, give me life, as you have said.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Salvation is far from evil-doers; for they have made no search for your rules.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Great is the number of your mercies, O Lord; give me life in keeping with your decisions.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Great is the number of those who are against me; but I have not been turned away from your unchanging word.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 I saw with hate those who were untrue to you; for they did not keep your saying.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 See how great is my love for your orders: give me life, O Lord, in keeping with your mercy.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Your word is true from the first; and your upright decision is unchanging for ever.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 SHIN Rulers have been cruel to me without cause; but I have the fear of your word in my heart.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 I am delighted by your saying, like a man who makes discovery of great wealth.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 I am full of hate and disgust for false words; but I am a lover of your law.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Seven times a day do I give you praise, because of your upright decisions.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Great peace have lovers of your law; they have no cause for falling.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Lord, my hope has been in your salvation; and I have kept your teachings.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 My soul has kept your unchanging word; great is my love for it.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 I have been ruled by your orders; for all my ways are before you.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 TAU Let my cry come before you, O Lord; give me wisdom in keeping with your word.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Let my prayer come before you; take me out of trouble, as you have said.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Let my lips be flowing with praise, because you have given me knowledge of your rules.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Let my tongue make songs in praise of your word; for all your teachings are righteousness.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Let your hand be near for my help; for I have given my heart to your orders.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 All my desire has been for your salvation, O Lord; and your law is my delight.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Give life to my soul so that it may give you praise; and let your decisions be my support.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 I have gone out of the way like a wandering sheep; make search for your servant; for I keep your teachings ever in mind.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psalms 119 >