< Proverbs 8 >
1 Is not wisdom crying out, and the voice of knowledge sounding?
Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
2 At the top of the highways, at the meeting of the roads, she takes her place;
Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
3 Where the roads go into the town her cry goes out, at the doorways her voice is loud:
Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
4 I am crying out to you, O men; my voice comes to the sons of men.
Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
5 Become expert in reason, O you simple ones; you foolish ones, take training to heart.
Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
6 Give ear, for my words are true, and my lips are open to give out what is upright.
Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
7 For good faith goes out of my mouth, and false lips are disgusting to me.
Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
8 All the words of my mouth are righteousness; there is nothing false or twisted in them.
Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
9 They are all true to him whose mind is awake, and straightforward to those who get knowledge.
Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
10 Take my teaching, and not silver; get knowledge in place of the best gold.
Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
11 For wisdom is better than jewels, and all things which may be desired are nothing in comparison with her.
Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
12 I, wisdom, have made wise behaviour my near relation; I am seen to be the special friend of wise purposes.
Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
13 The fear of the Lord is seen in hating evil: pride, a high opinion of oneself, the evil way, and the false tongue, are unpleasing to me.
Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
14 Wise design and good sense are mine; reason and strength are mine.
Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
15 Through me kings have their power, and rulers give right decisions.
Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
16 Through me chiefs have authority, and the noble ones are judging in righteousness.
Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
17 Those who have given me their love are loved by me, and those who make search for me with care will get me.
Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
18 Wealth and honour are in my hands, even wealth without equal and righteousness.
Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
19 My fruit is better than gold, even than the best gold; and my increase is more to be desired than silver.
Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
20 I go in the road of righteousness, in the way of right judging:
Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
21 So that I may give my lovers wealth for their heritage, making their store-houses full.
Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
22 The Lord made me as the start of his way, the first of his works in the past.
“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
23 From eternal days I was given my place, from the birth of time, before the earth was.
Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
24 When there was no deep I was given birth, when there were no fountains flowing with water.
Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
25 Before the mountains were put in their places, before the hills was my birth:
Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
26 When he had not made the earth or the fields or the dust of the world.
lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
27 When he made ready the heavens I was there: when he put an arch over the face of the deep:
Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
28 When he made strong the skies overhead: when the fountains of the deep were fixed:
pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
29 When he put a limit to the sea, so that the waters might not go against his word: when he put in position the bases of the earth:
pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
30 Then I was by his side, as a master workman: and I was his delight from day to day, playing before him at all times;
Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
31 Playing in his earth; and my delight was with the sons of men.
Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
32 Give ear to me then, my sons: for happy are those who keep my ways.
“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
33 Take my teaching and be wise; do not let it go.
Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
34 Happy is the man who gives ear to me, watching at my doors day by day, keeping his place by the pillars of my house.
Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
35 For whoever gets me gets life, and grace from the Lord will come to him.
Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
36 But he who does evil to me, does wrong to his soul: all my haters are in love with death.
Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”