< Proverbs 27 >
1 Do not make a noise about tomorrow, for you are not certain what a day's outcome may be.
Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
2 Let another man give you praise, and not your mouth; one who is strange to you, and not your lips.
Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
3 A stone has great weight, and sand is crushing; but the wrath of the foolish is of greater weight than these.
Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
4 Wrath is cruel, and angry feeling an overflowing stream; but who does not give way before envy?
Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
5 Better is open protest than love kept secret.
Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
6 The wounds of a friend are given in good faith, but the kisses of a hater are false.
Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
7 The full man has no use for honey, but to the man in need of food every bitter thing is sweet.
Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
8 Like a bird wandering from the place of her eggs is a man wandering from his station.
Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
9 Oil and perfume make glad the heart, and the wise suggestion of a friend is sweet to the soul.
Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
10 Do not give up your friend and your father's friend; and do not go into your brother's house in the day of your trouble: better is a neighbour who is near than a brother far off.
Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
11 My son, be wise and make my heart glad, so that I may give back an answer to him who puts me to shame.
Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
12 The sharp man sees the evil and takes cover: the simple go straight on and get into trouble.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
13 Take a man's clothing if he makes himself responsible for a strange man, and get an undertaking from him who gives his word for strange men.
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
14 He who gives a blessing to his friend with a loud voice, getting up early in the morning, will have it put to his account as a curse.
Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
15 Like an unending dropping on a day of rain is a bitter-tongued woman.
Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
16 He who keeps secret the secret of his friend, will get himself a name for good faith.
Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
17 Iron makes iron sharp; so a man makes sharp his friend.
Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
18 Whoever keeps a fig-tree will have its fruit; and the servant waiting on his master will be honoured.
Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
19 Like face looking at face in water, so are the hearts of men to one another.
Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
20 The underworld and Abaddon are never full, and the eyes of man have never enough. (Sheol )
Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol )
21 The heating-pot is for silver and the oven-fire for gold, and a man is measured by what he is praised for.
Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
22 Even if a foolish man is crushed with a hammer in a vessel among crushed grain, still his foolish ways will not go from him.
Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
23 Take care to have knowledge about the condition of your flocks, looking well after your herds;
Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
24 For wealth is not for ever, and money does not go on for all generations.
Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
25 The grass comes up and the young grass is seen, and the mountain plants are got in.
Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
26 The lambs are for your clothing, and the he-goats make the value of a field:
ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
27 There will be goats' milk enough for your food, and for the support of your servant-girls.
Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.