< Numbers 33 >

1 These are the journeys of the children of Israel, when they went out of the land of Egypt in their armies, under the direction of Moses and Aaron.
Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
2 And the stages of their journey on their way out were put down in writing by Moses at the order of the Lord: these are the stages of their journey and the way they went.
Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
3 On the fifteenth day of the first month they went out from Rameses; on the day after the Passover the children of Israel went out by the power of the Lord before the eyes of all the Egyptians,
Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
4 While the Egyptians were placing in the earth the bodies of their sons on whom the Lord had sent destruction: and their gods had been judged by him.
pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
5 So the children of Israel went from Rameses and put up their tents in Succoth.
Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
6 And they went on from Succoth and put up their tents in Etham on the edge of the waste land.
Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
7 And from Etham, turning back to Pi-hahiroth which is before Baal-zephon, they put up their tents before Migdol.
Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
8 And journeying on from before Hahiroth, they went through the sea into the waste land: they went three days' journey through the waste land of Etham and put up their tents in Marah.
Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
9 And from Marah they went on to Elim: and in Elim there were twelve water-springs and seventy palm-trees; and they put up their tents there.
Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
10 And they went on from Elim and put up their tents by the Red Sea.
Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
11 Then from the Red Sea they went on and put up their tents in the waste land of Sin.
Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
12 And they went on from the waste land of Sin, and put up their tents in Dophkah.
Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
13 And they went on from Dophkah, and put up their tents in Alush.
Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
14 And they went on from Alush, and put up their tents in Rephidim, where there was no drinking-water for the people.
Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
15 And they went on from Rephidim, and put up their tents in the waste land of Sinai.
Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
16 And they went on from the waste land of Sinai and put up their tents in Kibroth-hattaavah.
Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
17 And they went on from Kibroth-hattaavah, and put up their tents in Hazeroth.
Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
18 And they went on from Hazeroth, and put up their tents in Rithmah.
Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
19 And they went on from Rithmah, and put up their tents in Rimmon-perez.
Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
20 And they went on from Rimmon-perez, and put up their tents in Libnah.
Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
21 And they went on from Libnah, and put up their tents in Rissah.
Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
22 And they went on from Rissah, and put up their tents in Kehelathah.
Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
23 And they went on from Kehelathah, and put up their tents in Mount Shepher.
Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
24 And they went on from Mount Shepher, and put up their tents in Haradah.
Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
25 And they went on from Haradah, and put up their tents in Makheloth.
Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
26 And they went on from Makheloth, and put up their tents in Tahath.
Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
27 And they went on from Tahath, and put up their tents in Terah.
Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
28 And they went on from Terah, and put up their tents in Mithkah.
Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
29 And they went on from Mithkah, and put up their tents in Hashmonah.
Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
30 And they went on from Hashmonah, and put up their tents in Moseroth.
Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
31 And they went on from Moseroth, and put up their tents in Bene-jaakan.
Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
32 And they went on from Bene-jaakan, and put up their tents in Hor-haggidgad.
Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
33 And they went on from Hor-haggidgad, and put up their tents in Jotbathah.
Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
34 And they went on from Jotbathah, and put up their tents in Abronah.
Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
35 And they went on from Abronah, and put up their tents in Ezion-geber.
Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
36 And they went on from Ezion-geber, and put up their tents in the waste land of Zin (which is Kadesh).
Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
37 And they went on from Kadesh, and put up their tents in Mount Hor, on the edge of the land of Edom.
Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
38 And Aaron the priest went up into the mountain at the order of the Lord, and came to his death there, in the fortieth year after the children of Israel had come out of the land of Egypt, in the fifth month, on the first day of the month.
Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
39 Aaron was a hundred and twenty-three years old at the time of his death in Mount Hor.
Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
40 And news of the coming of the children of Israel came to the king of Arad, the Canaanite, who was living in the South in the land of Canaan.
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
41 And from Mount Hor they went on, and put up their tents in Zalmonah.
Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
42 And they went on from Zalmonah, and put up their tents in Punon.
Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
43 And they went on from Punon, and put up their tents in Oboth.
Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
44 And they went on from Oboth, and put up their tents in Iye-abarim at the edge of Moab.
Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
45 And they went on from Iyim, and put up their tents in Dibon-gad.
Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
46 And from Dibon-gad they went on, and put up their tents in Almon-diblathaim.
Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
47 And from Almon-diblathaim they went on, and put up their tents in the mountains of Abarim, before Nebo.
Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
48 And they went on from the mountains of Abarim, and put up their tents in the lowlands of Moab by Jordan at Jericho;
Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
49 Planting their tents by the side of Jordan from Beth-jeshimoth as far as Abel-shittim in the lowlands of Moab.
Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
50 And in the lowlands of Moab by Jordan at Jericho, the Lord said to Moses,
Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
51 Say to the children of Israel, When you go over Jordan into the land of Canaan,
“Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
52 See that all the people of the land are forced out from before you, and put to destruction all their pictured stones, and all their metal images, and all their high places:
mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
53 And take the land for yourselves, for your resting-place: for to you I have given the land as your heritage.
Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
54 And you will take up your heritage in the land by the decision of the Lord, to every family its part; the greater the family the greater its heritage, and the smaller the family the smaller will be its heritage; wherever the decision of the Lord gives to any man his part, that will be his; distribution will be made to you by your fathers' tribes.
Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
55 But if you are slow in driving out the people of the land, then those of them who are still there will be like pin-points in your eyes and like thorns in your sides, troubling you in the land where you are living.
“‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
56 And it will come about that as it was my purpose to do to them, so I will do to you.
Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”

< Numbers 33 >