< Numbers 11 >
1 Now the people were saying evil against the Lord; and the Lord, hearing it, was angry and sent fire on them, burning the outer parts of the tent-circle.
Anthu atadandaula kwa Yehova chifukwa cha mavuto awo, Yehovayo anamva ndipo anakwiya kwambiri. Kenaka moto wa Yehova unayaka pakati pawo ndi kutentha zigawo zina za kunja kwa msasa.
2 And the people made an outcry to Moses, and Moses made prayer to the Lord, and the fire was stopped.
Anthuwo analira kwa Mose ndipo Moseyo atapemphera kwa Yehova, motowo unazima.
3 So that place was named Taberah, because of the fire of the Lord which had been burning among them.
Motero malowo anawatcha Tabera, chifukwa moto wa Yehova unayaka pakati pawo.
4 And the mixed band of people who went with them were overcome by desire: and the children of Israel, weeping again, said, Who will give us flesh for our food?
Anthu ena osokoneza amene anali pakati pa Aisraeli anayamba kukhumba chakudya cha ku Igupto ndipo Aisraeli nawonso anayamba kufuwula kwambiri nʼkumati, “Tikanangopeza nyama yoti nʼkudya!
5 Sweet is the memory of the fish we had in Egypt for nothing, and the fruit and green plants of every sort, sharp and pleasing to the taste:
Tikukumbukira nsomba zaulere zimene tinkadya ku Igupto komanso nkhaka, mavwende, anyezi wamitundumitundu ndi adyo.
6 But now our soul is wasted away; there is nothing at all: we have nothing but this manna before our eyes.
Koma tsopano chilakolako chathu chatha. Sitikuona kanthu kena kakudya koma mana basi!”
7 Now the manna was like a seed of grain, like small clear drops.
Mana ankafanana ndi mbewu zamapira ndipo maonekedwe ake anali ngati ulimbo wowuma.
8 The people went about taking it up from the earth, crushing it between stones or hammering it to powder, and boiling it in pots, and they made cakes of it: its taste was like the taste of cakes cooked with oil.
Anthu ankapita kukatola manawo, nʼkumasinja mu mtondo kapena kupera. Ankawaphika mu mʼphika kapena kupanga makeke. Ndipo ankakoma ngati makeke ophikira mafuta a olivi.
9 When the dew came down on the tents at night, the manna came down with it.
Mame akamagwa pa msasawo usiku ankagwera kumodzi ndi manawo.
10 And at the sound of the people weeping, every man at his tent-door, the wrath of the Lord was great, and Moses was very angry.
Mose anamva anthu a banja lililonse akufuwula, banja lililonse pa khomo la tenti yake. Yehova anakwiya kwambiri ndipo Mose anavutikanso mu mtima.
11 And Moses said to the Lord, Why have you done me this evil? and why have I not grace in your eyes, that you have put on me the care of all this people?
Mose anafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani mwabweretsa mavuto otere pa mtumiki wanune? Nʼchiyani chimene ndachita choti sichinakusangalatseni mpaka kundisenzetsa katundu wa anthu onsewa?
12 Am I the father of all this people? have I given them birth, that you say to me, Take them in your arms, like a child at the breast, to the land which you gave by an oath to their fathers?
Kodi Ndine amene ndinatenga pathupi pa anthu onsewa? Kodi ndinawabala ndine? Bwanji mukundiwuza kuti ndiwanyamule mʼmanja mwanga, monga momwe mlezi amanyamulira kamwana, kupita nawo ku malo omwe munalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo?
13 Where am I to get flesh to give to all this people? For they are weeping to me and saying, Give us flesh for our food.
Ndingayipeze kuti nyama yoti anthu onsewa adye? Iwowa akulirira ine kuti, ‘Tipatse nyama tidye!’
14 I am not able by myself to take the weight of all this people, for it is more than my strength.
Sindingathe kusamala anthu onsewa ndekha. Katundu ameneyu ndi wolemera kwambiri kwa ine.
15 If this is to be my fate, put me to death now in answer to my prayer, if I have grace in your eyes; and let me not see my shame.
Ngati umu ndi mmene muzichitira nane, chonde ingondiphani pompano. Koma ngati mwandikomera mtima ndiye ndisaonenso mavutowa.”
16 And the Lord said to Moses, Send for seventy of the responsible men of Israel, who are in your opinion men of weight and authority over the people; make them come to the Tent of meeting and be there with you.
Yehova anawuza Mose kuti, “Undibweretsere anthu 70 ochokera pakati pa akuluakulu a Aisraeli, amene umawadziwa kuti ndiwo atsogoleri komanso akuluakulu a mabanja. Abwere ku tenti ya msonkhano kuti ayime kumeneko pamodzi ndi iwe.
17 And I will come down and have talk with you there: and I will take some of the spirit which is on you and put it on them, and they will take part of the weight of the people off you, so that you do not have to take it by yourself.
Ndidzatsika ndi kuyankhula nawe kumeneko, ndipo ndidzatenga mzimu umene uli pa iwe ndi kuyika pa iwowo. Adzakuthandiza kusenza nkhawa za anthuwa ndipo sudzasenzanso wekha.”
18 And say to the people, Make yourselves clean before tomorrow and you will have flesh for your food: for in the ears of the Lord you have been weeping and saying, Who will give us flesh for food? for we were well off in Egypt: and so the Lord will give you flesh, and it will be your food;
“Uwawuze anthuwo kuti, ‘Mudziyeretse, kukonzekera mawa, pamene mudzadya nyama.’ Yehova anakumvani pamene munkalira kuti, ‘Zikanakhala bwino tikanapeza nyama yoti tidye! Tinkakhala bwino ku Igupto!’ Tsopano Yehova adzakupatsani nyama ndipo mudzayidyadi.
19 Not for one day only, or even for five or ten or twenty days;
Simudzadya tsiku limodzi lokha, kapena masiku awiri, kapena asanu, khumi kapena masiku makumi awiri,
20 But every day for a month, till you are tired of it, turning from it in disgust: because you have gone against the Lord who is with you, and have been weeping before him saying, Why did we come out of Egypt?
koma mwezi wonse, mpaka itakukolani ndi kutopa nayo chifukwa mwakana Yehova yemwe ali pakati panu ndipo mwalira pamaso pake kuti, ‘Bwanji tinachoka ku Igupto?’”
21 Then Moses said, The people, among whom I am, are six hundred thousand men on foot; and you have said, I will give them flesh to be their food for a month.
Koma Mose anati, “Taonani pano ndili pakati pa anthu 600,000 amene ndi kuyenda nawo ndipo Inuyo mukuti, ‘Ndidzawapatsa nyama kuti adye mwezi wathunthu!’
22 Are flocks and herds to be put to death for them? or are all the fish in the sea to be got together so that they may be full?
Kodi ngakhale titapha nkhosa ndi ngʼombe, zingawakwanire? Ngakhale titagwira nsomba zonse za mʼnyanja, kodi zingawakwanire iwowa?”
23 And the Lord said to Moses, Has the Lord's hand become short? Now you will see if my word comes true for you or not.
Yehova anayankha Mose kuti, “Kodi dzanja langa ndi lalifupi? Uwona tsopano ngati zimene ndanenazo zichitike kapena ayi.”
24 And Moses went out and gave the people the words of the Lord: and he took seventy of the responsible men of the people, placing them round the Tent.
Choncho Mose anatuluka nakawuza anthu zomwe Yehova ananena. Anasonkhanitsa pamodzi akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja ndi kuwayimiritsa mozungulira Chihema.
25 Then the Lord came down in the cloud and had talk with him, and put on the seventy men some of the spirit which was on him: now when the spirit came to rest on them, they were like prophets, but only at that time.
Ndipo Yehova anatsika mʼmitambo ndi kuyankhula naye ndipo anatengako mzimu womwe unali pa Mose ndi kuwuyika pa akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja. Pamene mzimuwo unakhazikika pa akuluakuluwo, anayamba kunenera koma sanapitirize.
26 But two men were still in the tent-circle one of them named Eldad and the other Medad: and the spirit came to rest on them; they were among those who had been sent for, but they had not gone out to the Tent: and the prophet's power came on them in the tent-circle.
Koma anthu ena awiri omwe mayina awo anali Elidadi ndi Medadi, anatsalira mu msasa. Anali nawo mʼgulu la olembedwa aja, koma sanapite nawo ku Chihema. Komabe mzimu unakhala pa iwo ndipo ananenera ali mu msasa.
27 And a young man went running to Moses and said, Eldad and Medad are acting as prophets in the tent-circle.
Mnyamata wina anathamanga kudzawuza Mose kuti, “Elidadi ndi Medadi akunenera mu msasa.”
28 Then Joshua, the son of Nun, who had been Moses' servant from the time when he was a child, said, My lord Moses, let them be stopped.
Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Mose kuyambira ubwana wake, anayankha kuti, “Mbuye wanga Mose, aletseni!”
29 And Moses said to him, Are you moved by envy on my account? If only all the Lord's people were prophets, and the Lord might put his spirit on them!
Koma Mose anati, “Kodi ukuchita nsanje chifukwa cha ine? Ndikanakonda kuti anthu onse a Yehova akhale aneneri ndi kuti Yehova ayike mzimu wake pa iwo!”
30 Then Moses, with the responsible men of Israel, went back to the tent-circle.
Mose ndi akuluakulu a Israeli aja anabwerera ku msasa.
31 Then the Lord sent a wind, driving little birds from the sea, so that they came down on the tents, and all round the tent-circle, about a day's journey on this side and on that, in masses about two cubits high over the face of the earth.
Pamenepo Yehova anawutsa mphepo yochokera ku nyanja imene inabweretsa zinziri. Zinzirizo zinagwera pansi kuzungulira msasa, mtunda wa kilomita imodzi mbali zonse ndipo msinkhu wake unali mita imodzi.
32 And all that day and all night and the day after, the people were taking up the birds; the smallest amount which anyone got was ten homers: and they put them out all round the tents.
Tsiku limenelo masana onse mpaka usiku ndiponso tsiku lotsatiralo, anthu anatuluka kunja kukatola zinziri. Palibe amene anasonkhanitsa zochepera makilogalamu 1,000 ndipo anaziyanika kuzungulira msasa wonse.
33 But while the meat was still between their teeth, before it was tasted, the wrath of the Lord was moved against the people and he sent a great outburst of disease on them.
Koma pamene anthuwo ankadya nyamayo, asanayimeze nʼkomwe, ukali wa Yehova unafika pa iwo ndipo Iye anawakantha ndi mliri woopsa.
34 So that place was named Kibroth-hattaavah; because there they put in the earth the bodies of the people who had given way to their desires.
Nʼchifukwa chake malowo anawatcha Kibiroti Hatava chifukwa pamenepo anakwirirapo anthu osusuka aja.
35 From Kibroth-hattaavah the people went on to Hazeroth; and there they put up their tents.
Kuchoka pa Kibiroti Hatava anthuwo anayenda kupita ku Heziroti ndipo anakhala kumeneko kwa kanthawi.