< Nehemiah 8 >
1 And when the seventh month came, the children of Israel were in their towns. And all the people came together like one man into the wide place in front of the water-doorway; and they made a request to Ezra the scribe that he would put before them the book of the law of Moses which the Lord had given to Israel.
Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
2 And Ezra the priest put the law before the meeting of the people, before the men and women and all those who were able to take it in, on the first day of the seventh month.
Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
3 He was reading it in the wide place in front of the water-doorway, from early morning till the middle of the day, in the hearing of all those men and women whose minds were able to take it in; and the ears of all the people were open to the book of the law.
Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
4 And Ezra the scribe took his place on a tower of wood which they had made for the purpose; and by his side were placed Mattithiah and Shema and Anaiah and Uriah and Hilkiah and Maaseiah on the right; and on the left, Pedaiah and Mishael and Malchijah and Hashum and Hashbaddanah, Zechariah and Meshullam.
Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
5 And Ezra took the book, opening it before the eyes of all the people (for he was higher than the people); and when it was open, all the people got to their feet:
Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
6 And Ezra gave praise to the Lord, the great God. And all the people in answer said, So be it, so be it; lifting up their hands; and with bent heads they gave worship to the Lord, going down on their faces to the earth.
Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
7 And Jeshua and Bani and Sherebiah and Jamin, Akkub, Shabbethai, Hodiah, Maaseiah, Kelita, Azariah, Jozabad, Hanan, Pelaiah, and the Levites made the law clear to the people: and the people kept in their places.
Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
8 And they gave out the words of the book the law of God, clearly, and gave the sense of it, so that their minds were able to take it in.
Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
9 And Nehemiah, who was the Tirshatha, and Ezra, the priest and scribe, and the Levites who were the teachers of the people, said to all the people, This day is holy to the Lord your God; let there be no sorrow or weeping; for all the people were weeping on hearing the words of the law.
Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
10 Then he said to them, Go away now, and take the fat for your food and the sweet for your drink, and send some to him for whom nothing is made ready: for this day is holy to our Lord: and let there be no grief in your hearts; for the joy of the Lord is your strong place.
Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
11 So the Levites made all the people quiet, saying, Be quiet, for the day is holy; and do not give way to grief.
Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
12 And all the people went away to take food and drink, and to send food to others, and to be glad, because the words which were said to them had been made clear.
Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
13 And on the second day the heads of families of all the people and the priests and the Levites came together to Ezra the scribe, to give attention to the words of the law.
Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
14 And they saw that it was recorded in the law that the Lord had given orders by Moses, that the children of Israel were to have tents for their living-places in the feast of the seventh month:
Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
15 And that they were to give out an order, and make it public in all their towns and in Jerusalem, saying, Go out to the mountain and get olive branches and branches of field olives and of myrtle, and palm branches and branches of thick trees, to make tents, as it says in the book.
Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
16 And the people went out and got them and made themselves tents, every one on the roof of his house, and in the open spaces and in the open squares of the house of God, and in the wide place of the water-doorway, and the wide place of the doorway of Ephraim.
Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
17 All the people who had been prisoners and had come back, made tents and were living in them: for from the time of Jeshua, the son of Nun, till that day, the children of Israel had not done so. And there was very great joy.
Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
18 And day by day, from the first day till the last, he was reading from the book of the law of God. And they kept the feast for seven days: and on the eighth day there was a holy meeting, as it is ordered in the law.
Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.