< Nehemiah 11 >

1 And the rulers of the people were living in Jerusalem: the rest of the people made selection, by the decision of chance, of one out of every ten to be living in Jerusalem, the holy town; the other nine to go to the other towns.
Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo.
2 And the people gave a blessing to all the men who were freely offering to take up their places in Jerusalem.
Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.
3 Now these are the chiefs of the divisions of the country who were living in Jerusalem: but in the towns of Judah everyone was living on his heritage in the towns, that is, Israel, the priests, the Levites, the Nethinim, and the children of Solomon's servants.
Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu.
4 And in Jerusalem there were living certain of the children of Judah and of Benjamin. Of the children of Judah: Athaiah, the son of Uzziah, the son of Zechariah, the son of Amariah, the son of Shephatiah, the son of Mahalalel, of the children of Perez;
Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini. Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa: Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi.
5 And Maaseiah, the son of Baruch, the son of Col-hozeh, the son of Hazaiah, the son of Adaiah, the son of Joiarib, the son of Zechariah, the son of the Shilonite.
Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni.
6 All the sons of Perez living in Jerusalem were four hundred and sixty-eight men of good position.
Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.
7 And these are the sons of Benjamin: Sallu, the son of Meshullam, the son of Joed, the son of Pedaiah, the son of Kolaiah, the son of Maaseiah, the son of Ithiel, the son of Jeshaiah.
Nazi zidzukulu za Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya.
8 And after him Gabbai, Sallai, nine hundred and twenty-eight.
Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928.
9 And Joel, the son of Zichri, was their overseer; and Judah, the son of Hassenuah, was second over the town.
Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.
10 Of the priests: Jedaiah, the son of Joiarib, Jachin,
Ansembe anali awa: Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini;
11 Seraiah, the son of Hilkiah, the son of Meshullam, the son of Zadok, the son of Meraioth, the son of Ahitub, the ruler of the house of God,
Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu,
12 And their brothers who did the work of the house, eight hundred and twenty-two; and Adaiah, the son of Jeroham, the son of Pelaliah, the son of Amzi, the son of Zechariah, the son of Pashhur, the son of Malchijah,
ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya,
13 And his brothers, heads of families, two hundred and forty-two; and Amashsai, the son of Azarel, the son of Ahzai, the son of Meshillemoth, the son of Immer,
ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri
14 And their brothers, men of war, a hundred and twenty-eight; and their overseer was Zabdiel, the son of Haggedolim.
ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.
15 And of the Levites: Shemaiah, the son of Hasshub, the son of Azrikam, the son of Hashabiah, the son of Bunni,
Alevi anali awa: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni.
16 And Shabbethai and Jozabad, of the chiefs of the Levites, who were responsible for the outside business of the house of God;
Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
17 And Mattaniah, the son of Mica, the son of Zabdi, the son of Asaph, who had to give the first note of the song of praise in prayer, and Bakbukiah, the second among his brothers, and Abda, the son of Shammua, the son of Galal, the son of Jeduthun.
Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.
18 All the Levites in the holy town were two hundred and eighty-four.
Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.
19 In addition the door-keepers, Akkub, Talmon, and their brothers who kept watch at the doors, were a hundred and seventy-two.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.
20 And the rest of Israel, of the priests, the Levites, were in all the towns of Judah, every one in his heritage.
Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.
21 But the Nethinim were living in the Ophel; and Ziha and Gishpa were over the Nethinim.
Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.
22 And the overseer of the Levites at Jerusalem was Uzzi, the son of Bani, the son of Hashabiah, the son of Mattaniah, the son of Mica, of the sons of Asaph, the music-makers, who was over the business of the house of God.
Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu.
23 For there was an order from the king about them and a regular amount for the music-makers, for their needs day by day.
Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.
24 And Pethahiah, the son of Meshezabel, of the sons of Zerah, the son of Judah, was the king's servant in everything to do with the people.
Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.
25 And for the daughter-towns with their fields, some of the men of Judah were living in Kiriath-arba and its daughter-towns, and in Dibon and its daughter-towns, and in Jekabzeel and its daughter-towns,
Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake,
26 And in Jeshua, and in Moladah, and Beth-pelet,
ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti,
27 And in Hazar-shual, and in Beer-sheba and its daughter-towns,
Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo.
28 And in Ziklag, and in Meconah and its daughter-towns,
Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo,
29 And in En-rimmon, and in Zorah, and in Jarmuth,
ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti,
30 Zanoah, Adullam and their daughter-towns, Lachish and its fields, Azekah and its daughter-towns. So they were living from Beer-sheba to the valley of Hinnom.
Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.
31 And the children of Benjamin were living from Geba, at Michmash and Aija, and at Beth-el and its daughter-towns,
Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake,
32 At Anathoth, Nob, Ananiah,
ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya,
33 Hazor, Ramah, Gittaim,
ku Hazori, Rama ndi Gitaimu,
34 Hadid, Zeboim, Neballat,
ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati,
35 Lod and Ono, the valley of expert workers.
ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.
36 And of the Levites, certain divisions in Judah were joined to Benjamin.
Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.

< Nehemiah 11 >