< Leviticus 21 >
1 And the Lord said to Moses, Say to the priests, the sons of Aaron, Let no man make himself unclean for the dead among his people;
Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi ansembe, ana a Aaroni, ndipo uwawuze kuti, ‘Wansembe asadzidetse pokhudza munthu wakufa pakati pa abale ake.
2 But only for his near relations, for his mother or his father, his son or his daughter, and his brother;
Koma akhoza kukhudza thupi lakufa la amayi ake, abambo ake, mwana wake wamwamuna, mwana wake wamkazi, mchimwene wake,
3 And for his sister, a virgin, for she is his near relation and has had no husband, he may make himself unclean.
kapena mlongo wake wosakwatiwa amene amadalira iye chifukwa sanakwatiwe. Iye akhoza kudzidetsa pokhudza thupi lakufa la mchemwali wake wosakwatiwa yekha.
4 But let him, being a chief among his people, not make himself unclean in such a way as to put shame on himself.
Koma wansembe asadzidetse chifukwa cha anthu amene ali nawo pa ubale obwera chifukwa cha ukwati.
5 They are not to have their hair cut off for the dead, or the hair on their chins cut short, or make cuts in their flesh.
“‘Ansembe asamete tsitsi kumutu kwawo kapena mʼmphepete mwa ndevu zawo, kapenanso kudzichekacheka pa thupi lawo.
6 Let them be holy to their God and not make the name of their God common; for the fire offerings of the Lord and the bread of their God are offered by them, and they are to be holy.
Ayenera kukhala oyera pamaso pa Mulungu wawo ndipo asachititse manyazi dzina la Mulungu wawo. Popeza amapereka nsembe zotentha pa moto kwa Yehova, chakudya cha Mulungu wawo, iwo azikhala woyera.
7 They may not take as wife a loose or common woman, or one who has been put away by her husband: for the priest is holy to his God.
“‘Asakwatire akazi amene adzidetsa ndi chiwerewere kapena akazi amene amuna awo awasudzula, chifukwa ansembe ndi oyera pamaso pa Mulungu wawo.
8 And he is to be holy in your eyes, for by him the bread of your God is offered; he is to be holy in your eyes, for I the Lord, who make you holy, am holy.
Iwo akhale oyera chifukwa amapereka nsembe kwa Mulungu wanu. Muziwaona kuti ndi oyera, popeza Ine Yehova amene ndimawayeretsa ndine woyera, nawonso akhale oyera.
9 And if the daughter of a priest makes herself common and by her loose behaviour puts shame on her father, let her be burned with fire.
“‘Ngati mwana wamkazi wa wansembe adziyipitsa pochita zachiwerewere, ndiye kuti iye akuchititsa manyazi abambo ake; mwanayo atenthedwe pa moto.
10 And he who is the chief priest among his brothers, on whose head the holy oil has been put, who is marked out to put on the holy robes, may not let his hair go loose or have his clothing out of order as a sign of sorrow.
“‘Munthu amene ali mkulu wa ansembe pakati pa abale ake, amene anamudzoza pomutsanulira mafuta pamutu pake, ndiponso amene anapatulidwa pomuveka zovala zaunsembe, asalekerere tsitsi lake kapena kungʼamba zovala zake kusonyeza kuti ali pa chisoni.
11 He may not go near any dead body or make himself unclean for his father or his mother;
Asalowe mʼnyumba mmene muli munthu wakufa ngakhale womwalirayo ndi amayi ake kapena abambo ake.
12 He may not go out of the holy place or make the holy place of his God common; for the crown of the holy oil of his God is on him: I am the Lord.
Asadzidetse potulukira kunja kwa malo opatulika popeza mafuta womupatula kukhala wansembe ali pamutu pake. Ine ndine Yehova.
13 And let him take as his wife one who has not had relations with a man.
“‘Iye akwatire namwali wosadziwa mwamuna.
14 A widow, or one whose husband has put her away, or a common woman of loose behaviour, may not be the wife of a priest; but let him take a virgin from among his people.
Asakwatire mkazi wamasiye, mkazi wosudzulidwa, kapena mkazi wachiwerewere, koma akwatire namwali wosadziwa mwamuna pakati pa anthu a mtundu wake,
15 And he may not make his seed unclean among his people, for I the Lord have made him holy.
kuti mtundu wake usakhale wodetsedwa pakati pa abale popeza ndine Yehova, amene ndimamuyeretsa.’”
16 And the Lord said to Moses,
Yehova anawuza Mose kuti,
17 Say to Aaron, If a man of your family, in any generation, is damaged in body, let him not come near to make the offering of the bread of his God.
“Muwuze Aaroni kuti, ‘Munthu aliyense mwa zidzukulu zake ku mibado yawo yonse ikubwera akakhala ndi chilema asabwere kudzapereka nsembe kwa Mulungu wake.
18 For any man whose body is damaged may not come near: one who is blind, or has not the use of his legs, or one who has a broken nose or any unnatural growth,
Munthu aliyense wachilema motere: munthu wakhungu kapena wolumala miyendo, munthu wolumala nkhope kapena waziwalo zambiri,
19 Or a man with broken feet or hands,
munthu wa phazi lolumala kapena dzanja lolumala,
20 Or one whose back is bent, or one who is unnaturally small, or one who has a damaged eye, or whose skin is diseased, or whose sex parts are damaged;
kapena munthu wokhota msana kapena wamfupi kwambiri, kapena wolumala maso, munthu wa nthenda yonyerenyetsa, kapena wamphere, kapenanso wophwanyika mavalo, sayenera kusendera pafupi.
21 No man of the offspring of Aaron whose body is damaged in any way may come near to give the fire offerings of the Lord: he is damaged, he may not come near to make the offerings.
Mdzukulu aliyense wa Aaroni wansembe, amene ali ndi chilema asadzayandikire kukapereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Popeza kuti ali ndi chilema, asayandikire kudzapereka nsembe ya chakudya kwa Mulungu wake.
22 He may take of the bread of God, the holy and the most holy;
Koma iye angathe kudya chakudya chopatulika kwambiri chija, ngakhalenso chakudya chotsala pa nsembe zopatulika.
23 But he may not go inside the veil or come near the altar, because he is damaged; and he may not make my holy places common; for I the Lord have made them holy.
Koma chifukwa cha kulumala kwake, sayenera kuyandikira katani kapena kufika pa guwa kuti angadetse malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.’”
24 These are the words which Moses said to Aaron and to his sons and to all the children of Israel.
Choncho Mose anawuza Aaroni ndi ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse zimenezi.