< Job 7 >

1 Has not man his ordered time of trouble on the earth? and are not his days like the days of a servant working for payment?
“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
2 As a servant desiring the shades of evening, and a workman looking for his payment:
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
3 So I have for my heritage months of pain to no purpose, and nights of weariness are given to me.
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
4 When I go to my bed, I say, When will it be time to get up? but the night is long, and I am turning from side to side till morning light.
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
5 My flesh is covered with worms and dust; my skin gets hard and then is cracked again.
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
6 My days go quicker than the cloth-worker's thread, and come to an end without hope.
“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
7 O, keep in mind that my life is wind: my eye will never again see good.
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
8 The eye of him who sees me will see me no longer: your eyes will be looking for me, but I will be gone.
Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
9 A cloud comes to an end and is gone; so he who goes down into the underworld comes not up again. (Sheol h7585)
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol h7585)
10 He will not come back to his house, and his place will have no more knowledge of him.
Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
11 So I will not keep my mouth shut; I will let the words come from it in the pain of my spirit, my soul will make a bitter outcry.
“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 Am I a sea, or a sea-beast, that you put a watch over me?
Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
13 When I say, In my bed I will have comfort, there I will get rest from my disease;
Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 Then you send dreams to me, and visions of fear;
ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 So that a hard death seems better to my soul than my pains.
kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 I have no desire for life, I would not be living for ever! Keep away from me, for my days are as a breath.
Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
17 What is man, that you have made him great, and that your attention is fixed on him,
“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
18 And that your hand is on him every morning, and that you are testing him every minute?
kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 How long will it be before your eyes are turned away from me, so that I may have a minute's breathing-space?
Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 If I have done wrong, what have I done to you, O keeper of men? why have you made me a mark for your blows, so that I am a weariness to myself?
Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 And why do you not take away my sin, and let my wrongdoing be ended? for now I go down to the dust, and you will be searching for me with care, but I will be gone.
Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”

< Job 7 >