< Genesis 9 >
1 And God gave his blessing to Noah and his sons, and said, Be fertile, and have increase, and make the earth full.
Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake aamuna nati kwa iwo, “Berekanani ndipo muchulukane ndi kudzaza dziko lapansi.
2 And the fear of you will be strong in every beast of the earth and every bird of the air; everything which goes on the land, and all the fishes of the sea, are given into your hands.
Nyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za mlengalenga, ndi chamoyo chilichonse chokwawa, ndiponso nsomba zonse za ku nyanja; zidzakuopani ndipo ndazipereka kuti muzilamulire.
3 Every living and moving thing will be food for you; I give them all to you as before I gave you all green things.
Tsopano chamoyo chilichonse chidzakhala chakudya chanu. Monga momwe ndinakupatsirani ndiwo zamasamba, tsopano ndikupatsaninso nyama iliyonse.
4 But flesh with the life-blood in it you may not take for food.
“Koma musamadye nyama imene ikanali ndi magazi oyenda.
5 And for your blood, which is your life, will I take payment; from every beast I will take it, and from every man will I take payment for the blood of his brother-man.
Aliyense wopha munthu adzaphedwa, nyama iliyonse yopha munthu idzaphedwa, munthu aliyense wopha munthu mnzake, adzaphedwa.
6 Whoever takes a man's life, by man will his life be taken; because God made man in his image.
“Aliyense wopha munthu, adzaphedwanso ndi munthu; pakuti Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.
7 And now, be fertile and have increase; have offspring on the earth and become great in number.
Inu muberekane ndi kuchulukana kuti mudzaze dziko lonse lapansi ndi kuligonjetsa.”
8 And God said to Noah and to his sons,
Mulungu anawuza Nowa ndi ana ake kuti,
9 Truly, I will make my agreement with you and with your seed after you,
“Tsopano Ine ndapangana ndi iwe ndi zidzukulu zako zamʼtsogolomo,
10 And with every living thing with you, all birds and cattle and every beast of the earth which comes out of the ark with you.
pamodzi ndi zamoyo zonse, mbalame, ziweto ndi nyama zonse za kuthengo, ndi zonse zimene zinatuluka mʼchombo pamodzi ndi iwe.
11 And I will make my agreement with you; never again will all flesh be cut off by the waters; never again will the waters come over all the earth for its destruction.
Pangano langa ndi ili: Ine ndilonjeza kuti sindidzawononganso zamoyo ndi madzi a chigumula. Chigumula sichidzawononganso dziko lapansi.”
12 And God said, This is the sign of the agreement which I make between me and you and every living thing with you, for all future generations:
Ndipo Mulungu anati, “Ine ndikupereka chizindikiro ichi cha pangano langa la pakati pa Ine ndi iwe, ana ako, zamoyo zonse, pamodzi ndi mibado ya mʼtsogolo.
13 I will put my bow in the cloud and it will be for a sign of the agreement between me and the earth.
Ndayika utawaleza wanga mʼmitambo, ndipo chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi dziko lapansi.
14 And whenever I make a cloud come over the earth, the bow will be seen in the cloud,
Nthawi zonse pakakhala mitambo mu mlengalenga ndipo utawaleza uwoneka,
15 And I will keep in mind the agreement between me and you and every living thing; and never again will there be a great flow of waters causing destruction to all flesh.
ndizikumbukira pangano langa pakati pa Ine ndi inu ndi zolengedwa zonse. Madzi sadzakhalanso chigumula chowononga dziko lapansi.
16 And the bow will be in the cloud, and looking on it, I will keep in mind the eternal agreement between God and every living thing on the earth.
Utawaleza ukamadzaoneka mʼmitambo, ndidzawuona ndi kukumbukira pangano losatha pakati pa Mulungu ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
17 And God said to Noah, This is the sign of the agreement which I have made between me and all flesh on the earth.
Choncho Mulungu anati kwa Nowa, “Ichi ndiye chizindikiro cha pangano limene ndalichita pakati pa Ine ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
18 And the sons of Noah who went out of the ark were Shem, Ham, and Japheth; and Ham is the father of Canaan.
Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani.
19 These three were the sons of Noah and from them all the earth was peopled.
Ana aamuna a Nowa amenewa ndiwo anali makolo a anthu onse pa dziko lapansi.
20 In those days Noah became a farmer, and he made a vine-garden.
Nowa anali munthu woyamba kulima munda wamphesa.
21 And he took of the wine of it and was overcome by drink; and he was uncovered in his tent.
Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche.
22 And Ham, the father of Canaan, saw his father unclothed, and gave news of it to his two brothers outside.
Hamu, abambo ake a Kanaani ataona kuti abambo ake ali maliseche anakawuza abale ake awiri aja omwe anali panja.
23 And Shem and Japheth took a robe, and putting it on their backs went in with their faces turned away, and put it over their father so that they might not see him unclothed.
Koma Semu ndi Yafeti anatenga chofunda nachiyika pa mapewa awo; ndipo anayenda chamʼmbuyo naphimba umaliseche wa abambo awo. Anafulatira kuti asaone umaliseche wa abambo awo.
24 And, awaking from his wine, Noah saw what his youngest son had done to him, and he said,
Nowa atadzuka, kuledzera kutatha, ndikudziwa zimene mwana wake wamngʼono wamwamuna uja anamuchitira,
25 Cursed be Canaan; let him be a servant of servants to his brothers.
anati, “Atembereredwe Kanaani! Adzakhala kapolo wa pansi kwenikweni kwa abale ake.”
26 And he said, Praise to the Lord, the God of Shem; let Canaan be his servant.
Anatinso, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Semu! Kanaani akhale kapolo wa Semu.
27 May God make Japheth great, and let his living-place be in the tents of Shem, and let Canaan be his servant.
Mulungu akulitse dziko la Yafeti; Yafeti alandire madalitso pamodzi ndi Semu, ndipo Kanaani akhale kapolo wawo.”
28 And Noah went on living three hundred and fifty years after the great flow of waters;
Chitatha chigumula, Nowa anakhala ndi moyo zaka 350.
29 all the years of his life were nine hundred and fifty: and he came to his end.
Anamwalira ali ndi zaka 950.