< Genesis 5 >
1 This is the book of the generations of Adam. In the day when God made man, he made him in the image of God;
Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
2 Male and female he made them, naming them Man, and giving them his blessing on the day when they were made.
Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
3 Adam had been living for a hundred and thirty years when he had a son like himself, after his image, and gave him the name of Seth:
Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
4 And after the birth of Seth, Adam went on living for eight hundred years, and had sons and daughters:
Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
5 And all the years of Adam's life were nine hundred and thirty: and he came to his end.
Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
6 And Seth was a hundred and five years old when he became the father of Enosh:
Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
7 And he went on living after the birth of Enosh for eight hundred and seven years, and had sons and daughters:
Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
8 And all the years of Seth's life were nine hundred and twelve: and he came to his end.
Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
9 And Enosh was ninety years old when he became the father of Kenan:
Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
10 And after the birth of Kenan, Enosh went on living for eight hundred and fifteen years, and had sons and daughters:
Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
11 And all the years of Enosh were nine hundred and five: and he came to his end.
Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
12 And Kenan was seventy years old when he became the father of Mahalalel:
Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
13 And after the birth of Mahalalel, Kenan went on living for eight hundred and forty years, and had sons and daughters:
Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
14 And all the years of Kenan's life were nine hundred and ten; and he came to his end.
Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
15 And Mahalalel was sixty-five years old when he became the father of Jared:
Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
16 And after the birth of Jared, Mahalalel went on living for eight hundred and thirty years, and had sons and daughters:
Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
17 And all the years of Mahalalel's life were eight hundred and ninety-five: and he came to his end.
Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
18 And Jared was a hundred and sixty-two years old when he became the father of Enoch:
Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
19 And Jared went on living after the birth of Enoch for eight hundred years, and had sons and daughters:
Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
20 And all the years of Jared's life were nine hundred and sixty-two: and he came to his end.
Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
21 And Enoch was sixty-five years old when he became the father of Methuselah:
Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
22 And after the birth of Methuselah, Enoch went on in God's ways for three hundred years, and had sons and daughters:
Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
23 And all the years of Enoch's life were three hundred and sixty-five:
Zaka zonse za Enoki zinali 365.
24 And Enoch went on in God's ways: and he was not seen again, for God took him.
Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
25 And Methuselah was a hundred and eighty-seven years old when he became the father of Lamech:
Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
26 And after the birth of Lamech, Methuselah went on living for seven hundred and eighty-two years, and had sons and daughters:
Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
27 And all the years of Methuselah's life were nine hundred and sixty-nine: and he came to his end.
Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
28 And Lamech was a hundred and eighty-two years old when he had a son:
Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
29 And he gave him the name of Noah, saying, Truly, he will give us rest from our trouble and the hard work of our hands, because of the earth which was cursed by God.
Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
30 And after the birth of Noah, Lamech went on living for five hundred and ninety-five years, and had sons and daughters:
Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
31 And all the years of Lamech's life were seven hundred and seventy-seven: and he came to his end.
Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
32 And when Noah was five hundred years old, he became the father of Shem, Ham, and Japheth.
Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.