< Genesis 26 >

1 Then came a time of great need in the land, like that which had been before in the days of Abraham. And Isaac went to Abimelech, king of the Philistines, at Gerar.
Tsono kunagwa njala ina mʼdzikomo kuwonjezera pa ija ya poyamba ya nthawi ya Abrahamu ndipo Isake anapita kwa Abimeleki mfumu ya Afilisti ku Gerari.
2 And the Lord came to him in a vision and said, Do not go down to Egypt; keep in the land of which I will give you knowledge:
Yehova anadza kwa Isake nati, “Usapite ku Igupto; koma ukhale mʼdziko limene ndidzakuwuza kuti ukakhalemo.
3 Keep in this land, and I will be with you and give you my blessing; for to you and to your seed will I give all these lands, giving effect to the oath which I made to your father Abraham;
Khala mʼdziko lino ndipo ndidzakhala nawe ndi kukudalitsa. Pakuti kwa iwe ndi zidzukulu zako ndidzapereka mayiko onsewa. Choncho ndidzakwaniritsa pangano limene ndinalumbira kwa Abrahamu, abambo ako.
4 I will make your seed like the stars of heaven in number, and will give them all these lands, and your seed will be a blessing to all the nations of the earth;
Zidzukulu zako ndidzazichulukitsa ngati nyenyezi za mu mlengalenga ndi kuzipatsa mayiko onsewa. Ndiponso anthu onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa zidzukulu zako,
5 Because Abraham gave ear to my voice and kept my words, my rules, my orders, and my laws.
chifukwa Abrahamu anandimvera, nasunga malamulo anga onse.”
6 So Isaac went on living in Gerar;
Choncho Isake anakhala ku Gerari.
7 And when he was questioned by the men of the place about his wife, he said, She is my sister; fearing to say, She is my wife; for, he said, the men of the place may put me to death on account of Rebekah; because she is very beautiful.
Anthu akumaloko atafunsa Isake za mkazi wake, iye anati, “Ndi mlongo wanga ameneyu.” Iye anaopa kunena kuti, “Ndi mkazi wanga ameneyu,” popeza ankaganiza kuti anthu akumeneku akhoza kumupha ndi kukwatira mkazi wake popeza Rebeka anali wokongola.
8 And when he had been there for some time, Abimelech, king of the Philistines, looking through a window, saw Isaac playing with Rebekah his wife.
Isake atakhalako kumeneko nthawi yayitali, Abimeleki mfumu ya Afilisti, anasuzumira pa zenera kuyangʼana kunja, ndipo anaona Isake akugwiragwira Rebeka, mkazi wake.
9 And he said to Isaac, It is clear that she is your wife: why then did you say, She is my sister? And Isaac said, For fear that I might be put to death because of her.
Choncho Abimeleki anamuyitanitsa Isake nati, “Uyu ndi mkazi wako ndithu! Nanga bwanji umati, ‘Ndi mlongo wanga’?” Ndipo Isake anamuyankha kuti, “Ine ndimaganiza kuti ndingataye moyo wanga chifukwa cha iyeyu.”
10 Then Abimelech said, What have you done to us? one of the people might well have had connection with your wife, and the sin would have been ours.
Tsono Abimeleki anati, “Nʼchiyani chimene watichitira? Mmodzi mwa anthuwa anatsala pangʼono kugona ndi mkazi wako ndipo ukanatisandutsa ife kukhala olakwa.”
11 And Abimelech gave orders to his people that anyone touching Isaac or his wife was to be put to death.
Choncho Abimeleki analamula anthu ake onse nati, “Aliyense amene avutitse munthu uyu pamodzi ndi mkazi wake adzaphedwa ndithu.”
12 Now Isaac, planting seed in that land, got in the same year fruit a hundred times as much, for the blessing of the Lord was on him.
Isake anadzala mbewu mʼmunda, ndipo chaka chomwecho anakolola zinthu zambiri chifukwa Yehova anamudalitsa.
13 And his wealth became very great, increasing more and more;
Isake analemera. Chuma chake chinkachulukirachulukira mpaka anasanduka munthu wolemera kwambiri.
14 For he had great wealth of flocks and herds and great numbers of servants; so that the Philistines were full of envy.
Anali ndi nkhosa, ngʼombe ndi antchito ambiri mwakuti Afilisti anamuchitira nsanje.
15 Now all the water-holes, which his father's servants had made in the days of Abraham, had been stopped up with earth by the Philistines.
Nthawi iyi nʼkuti Afilisti atakwirira ndi dothi zitsime zonse zimene antchito abambo ake Abrahamu anakumba mu nthawi ya abambo akewo.
16 And Abimelech said to Isaac, Go away from us, for you are stronger than we are.
Ndipo Abimeleki anati kwa Isake, “Muchoke pakati pathu chifukwa mwasanduka wamphamvu kuposa ife.”
17 So Isaac went away from there, and put up his tents in the valley of Gerar, making his living-place there.
Choncho Isake anachokako kumeneko nakakhala ku chigwa cha Gerari kumene anakhazikikako.
18 And he made again the water-holes which had been made in the days of Abraham his father, and which had been stopped up by the Philistines; and he gave them the names which his father had given them.
Isake anafukulanso zitsime zija zimene zinakumbidwa mu nthawi ya abambo ake Abrahamu. Atamwalira Abrahamu, Afilisti anakwirira zitsimezi. Tsono anazitcha mayina omwewo amene abambo ake anazitcha.
19 Now Isaac's servants made holes in the valley, and came to a spring of flowing water.
Antchito a Isake anakumba mʼchigwamo ndipo anapezamo kasupe wa madzi.
20 But the herdmen of Gerar had a fight with Isaac's herdmen, for they said, The spring is ours: so he gave the spring the name of Esek, because there was a fight about it.
Koma abusa a ku Gerari anakangana ndi abusa a Isake nati, “Madziwa ndi athu.” Motero iye anachitcha chitsimecho Mkangano chifukwa anakangana naye.
21 Then they made another water-hole, and there was a fight about that, so he gave it the name of Sitnah.
Kenaka iwo anakumba chitsime china, koma anakangananso chifukwa cha chitsimecho. Choncho anachitcha dzina lakuti Chidani.
22 Then he went away from there, and made another water-hole, about which there was no fighting: so he gave it the name of Rehoboth, for he said, Now the Lord has made room for us, and we will have fruit in this land.
Anachokapo pamenepo nakakumba china. Koma apa sanakanganiranenso ndi munthu. Iye anachitcha Kutakasuka, nati, “Tsopano Yehova watipatsa ife malo otakasukirako ndipo tilemera muno.”
23 And from there he went on to Beer-sheba.
Kenaka Isake anachoka ku malo kuja kupita ku Beeriseba.
24 That night the Lord came to him in a vision, and said, I am the God of your father Abraham: have no fear for I am with you, blessing you, and your seed will be increased because of my servant Abraham.
Usiku umenewo Yehova anadza kwa Isake nati, “Ine ndine Mulungu wa abambo ako Abrahamu. Usachite mantha popeza Ine ndili ndi iwe. Ndidzakudalitsa ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri chifukwa cha mtumiki wanga Abrahamu.”
25 Then he made an altar there, and gave worship to the name of the Lord, and he put up his tents there, and there his servants made a water-hole.
Isake anamanga guwa lansembe pamenepo ndipo anapembedza Yehova. Pomwepo anamanga tenti yake, ndipo antchito ake anakumba chitsime.
26 And Abimelech had come to him from Gerar, with Ahuzzath his friend and Phicol, the captain of his army.
Abimeleki pamodzi ndi Ahuzati mlangizi wake ndi Fikolo mkulu wa ankhondo ake anabwera kwa Isake kuchokera ku Gerari.
27 And Isaac said to them, Why have you come to me, seeing that in your hate for me you sent me away from you?
Tsopano Isake anawafunsa kuti, “Bwanji mwabwera kwa ine, popeza munandichitira nkhanza ndi kundithamangitsa?”
28 And they said, We saw clearly that the Lord was with you: so we said, Let there be an oath between us and you, and let us make an agreement with you;
Iwo anayankha, “Tsopano tadziwa kuti Yehova anali ndi iwe; ndiye taganiza kuti inu ndi ife tichite lumbiro. Ife tichite pangano ndi inu
29 That you will do us no damage, even as we put no hand on you, and did you nothing but good, and sent you away in peace: and now the blessing of the Lord is on you.
kuti inu simudzatichitira zoyipa monga ifenso sitinakuchitireni nkhondo. Ife tinakuchitirani zabwino zokhazokha, ndipo tinakulolani kuti musamuke kuchoka kwathu mu mtendere. Tsopano Yehova wakudalitsani.”
30 Then he made a feast for them, and they all had food and drink.
Tsono Isake anawakonzera phwando, ndipo anadya ndi kumwa.
31 And early in the morning they took an oath one to the other: then Isaac sent them away and they went on their way in peace.
Mmawa wake aliyense analumbira pangano kwa mnzake. Tsono Isake anawalola kuti anyamuke ndipo anamusiya mu mtendere.
32 And that day Isaac's servants came to him and gave him word of the water-hole which they had made, and said to him, We have come to water.
Tsiku limenelo, antchito a Isake anabwera namuwuza za chitsime chimene anakumba. Iwo anati, “Tawapeza madzi!”
33 And he gave it the name of Shibah: so the name of that town is Beer-sheba to this day.
Iye chitsimecho anachitcha Pangano. Nʼchifukwa chake mzindawu umatchedwa Beeriseba mpaka lero.
34 And when Esau was forty years old, he took as his wives Judith, the daughter of Beeri the Hittite, and Basemath, the daughter of Elon the Hittite:
Pamene Esau anali ndi zaka 40, anakwatira Yuditi mwana wamkazi wa Beeri Mhiti. Anakwatiranso Basemati mwana wa mkazi wa Eloni Mhiti.
35 And Isaac and Rebekah had grief of mind because of them.
Akazi awiriwa anasandutsa Isake ndi Rebeka kukhala ndi moyo wa madandawulo nthawi zonse.

< Genesis 26 >