< Ezekiel 46 >
1 This is what the Lord has said: The doorway of the inner square looking to the east is to be shut on the six working days; but on the Sabbath it is to be open, and at the time of the new moon it is to be open.
“Ambuye Yehova akuti, Chipata chakummawa cha bwalo lamʼkati chizikhala chotseka pa masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito, koma chizitsekulidwa pa tsiku la sabata ndi pa tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano.
2 And the ruler is to go in through the covered way of the outer doorway outside, and take his place by the pillar of the doorway, and the priests will make his burned offering and his peace-offerings and he will give worship at the doorstep of the doorway; then he will go out, and the door will not be shut till the evening.
Mfumu izilowa podzera mʼkhonde la mʼkati la chipata pochokera kunja, nʼkudzayima pafupi ndi nsanamira yapakhomo. Ansembe apereke nsembe yake yopsereza ndi nsembe yake yachiyanjano. Mfumuyo ipembedze pa chiwundo cha pa chipatacho kenaka nʼkutuluka. Koma chipatacho asachitseke mpaka madzulo.
3 And the people of the land are to give worship at the door of that doorway before the Lord on the Sabbaths and at the new moons.
Anthu a mʼdziko azipembedza pamaso pa Yehova pa khomo la chipata chimenechi pa masiku a sabata ndi pa tsiku la mwezi watsopano.
4 And the burned offering offered to the Lord by the ruler on the Sabbath day is to be six lambs without a mark on them and a male sheep without a mark;
Nsembe yopsereza imene mfumu iyenera kupereka kwa Yehova ikhale motere: pa tsiku la Sabata izipereka ana ankhosa aamuna asanu ndi mmodzi wopanda chilema, ndiponso nkhosa yayima yopanda chilema.
5 And the meal offering is to be an ephah for the sheep, and for the lambs whatever he is able to give, and a hin of oil to an ephah.
Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, mfumu izipereka nsembe ya chakudya yokwanira efa imodzi. Pamodzi ndi ana ankhosa, mfumu izipereka monga ikufunira kutero. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse ya tirigu.
6 And at the time of the new moon it is to be a young ox of the herd without a mark on him, and six lambs and a male sheep, all without a mark:
Pa tsiku la mwezi watsopano mfumuyo ipereke mwana wangʼombe wamwamuna, ana ankhosa asanu ndi mmodzi ndiponso nkhosa yayimuna, zonsezi zopanda chilema.
7 And he is to give a meal offering, an ephah for the ox and an ephah for the sheep, and for the lambs whatever he is able to give, and a hin of oil to an ephah.
Ipereke efa imodzi ya tirigu pa ngʼombe yayimuna iliyonse ndiponso efa ina pa nkhosa yayimuna iliyonse. Pa ana ankhosa ipereke tirigu monga ikufunira kutero. Pamodzi ndi efa ya tirigu, ipereke hini imodzi ya mafuta.
8 And when the ruler comes in, he is to go in through the covered way of the doorway, and he is to go out by the same way.
Pamene mfumu ikulowa, izidzera mʼkhonde lamʼkati la chipata chakummawa, izitulukiranso pomwepo.
9 But when the people of the land come before the Lord at the fixed feasts, he who comes in by the north doorway to give worship is to go out by the south doorway; and he who comes in by the south doorway is to go out by the north doorway: he is not to come back by the doorway through which he went in, but is to go straight before him.
“Anthu a mʼdzikomo akabwera kudzapembedza Yehova pa masiku a chikondwerero, ngati munthu alowera pa chipata chakumpoto atulukire chipata chakummwera. Munthu wolowera chipata chakummwera, atulukire chipata chakumpoto. Munthu asatulukire pomwe walowera, koma atulukire pa chipata choyangʼanana nacho.
10 And the ruler, when they come in, is to come among them, and is to go out when they go out.
Mfumu izidzakhala pakati pawo. Anthu akamadzalowa mfumu idzalowa nawo. Anthu akamadzatuluka mfumu idzatuluka nawo.
11 At the feasts and the fixed meetings the meal offerings are to be an ephah for an ox, and an ephah for a male sheep, and for the lambs whatever he is able to give, and a hin of oil to an ephah.
“Pa masiku achikondwerero ndi pa masiku ena osankhidwa, zopereka za chakudya zikhale zokwanira efa imodzi pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, efa imodzinso ndi nkhosa yayimuna, koma pa mwana wankhosa apereke monga angathere. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse.
12 And when the ruler makes a free offering, a burned offering or a peace-offering freely given to the Lord, the doorway looking to the east is to be made open for him, and he is to make his burned offering and his peace-offerings as he does on the Sabbath day: and he will go out; and the door will be shut after he has gone out.
Pamene mfumu ikufuna kupereka chopereka chaufulu kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena zopereka za chiyanjano, ayitsekulire chipata chakummawa. Iyo ipereke nsembe yopsereza kapena zopereka zake za chiyanjano monga imachitira pa tsiku la Sabata. Kenaka ituluke ndipo mfumuyo itatuluka, atseke chitsekocho.
13 And you are to give a lamb a year old without any mark on it for a burned offering to the Lord every day: morning by morning you are to give it.
“Tsiku lililonse nthawi ya mmawa azipereka kwa Yehova mwana wankhosa wa chaka chimodzi.
14 And you are to give, morning by morning, a meal offering with it, a sixth of an ephah and a third of a hin of oil dropped on the best meal; a meal offering offered to the Lord at all times by an eternal order.
Pamodzi ndi nyamayo aziperekanso mmawa uliwonse chopereka cha chakudya chokwanira chimodzi mwa zigawo zisanu ndi chimodzi za efa. Aziperekanso chimodzi mwa zigawo zitatu za hini ya mafuta okandira ufa wosalala. Chopereka cha chakudya chimenechi chiziperekedwa kwa Yehova nthawi zonse mwa lamulo.
15 And they are to give the lamb and the meal offering and the oil, morning by morning, for a burned offering at all times.
Motero azipereka mwana wankhosa ndi chopereka cha chakudya ndi mafuta mmawa uliwonse kuti zikhale nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku.
16 This is what the Lord has said: If the ruler gives a property to any of his sons, it is his heritage and will be the property of his sons; it is theirs for their heritage.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ngati kalonga apereka mphatso chigawo cha cholowa chake kwa mmodzi mwa ana ake, mphatsoyo idzakhala ya ana akewo. Idzakhala yawo chifukwa ndi cholowa chawo.
17 And if he gives a part of his heritage to one of his servants, it will be his till the year of making free, and then it will go back to the ruler; for it is his sons' heritage, and is to be theirs.
Koma ngati ipereka mphatso yotere kuchokera pa cholowa chake kwa mmodzi mwa antchito ake, mphatsoyo idzakhala ya wantchitoyo mpaka chaka chaufulu. Pambuyo pake idzabwereranso kwa kalongayo chifukwa cholowa chake ndi cha ana ake.
18 And the ruler is not to take the heritage of any of the people, driving them out of their property; he is to give a heritage to his sons out of the property which is his: so that my people may not be sent away from their property.
Kalonga asalande cholowa chilichonse cha anthu, kuwachotsa mʼdera lawo la dziko. Iye apereke kwa ana ake cholowa chawo chochokera pa chuma chakechake, kuti pasapezeke ndi mmodzi yemwe mwa anthu anga wolandidwa chuma chake.’”
19 And he took me through by the way in at the side of the doorway into the holy rooms which are the priests', looking to the north: and I saw a place at the side of them to the west.
Kenaka munthu uja anandidzeretsa pa khomo la pambali pa chipata nandilowetsa ku zipinda za ansembe zoyangʼana kumpoto. Ndipo ndinaona kumeneko malo chakumadzulo kwa zipindazo.
20 And he said to me, This is the place where the offering for error and the sin-offering are to be cooked in water by the priests, and where the meal offering is to be cooked in the oven; so that they may not be taken out into the outer square to make the people holy.
Munthuyo anandiwuza kuti, “Awa ndi malo amene ansembe adzaphikirapo nsembe yopepesera kupalamula ndi nsembe yopepesera machimo. Kumenekonso azidzawotcherako chopereka cha chakudya. Sadzatuluka nazo zoyerazi mʼbwalo lakunja kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu ena.”
21 And he took me out into the outer square and made me go by the four angles of the square; and I saw that in every angle of the open square there was a space shut in.
Pambuyo pake anandilowetsa mʼbwalo lakunja napita nane ku ngodya zinayi za bwalolo. Ndipo ndinaona mʼkati mwa ngodya iliyonse bwalo lina.
22 In the four angles there were spaces walled in, forty cubits long and thirty wide; the four were of the same size.
Motero pa ngodya zinayi za bwalo panalinso mabwalo ena angʼonoangʼono. Mabwalo amenewa anali ofanana. Mulitali mwake munali mamita makumi awiri ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi ndi asanu.
23 And there was a line of wall all round inside them, round all four, and boiling-places were made under it all round about.
Kuzungulira mabwalo anayi angʼonoangʼono aja panali mpanda wamiyala, ndi malo asonkhapo moto omangidwa mʼmunsi mwa mpandawo mozungulira.
24 And he said to me, These are the boiling-rooms, where the offering of the people is cooked by the servants of the house.
Munthuyo anandiwuza kuti, “Izi ndi zipinda zophikiramo. Mʼmenemu anthu otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzaphikiramo nyama za nsembe za anthu.”