< Exodus 6 >
1 And the Lord said to Moses, Now you will see what I am about to do to Pharaoh; for by a strong hand he will be forced to let them go, driving them out of his land because of my outstretched arm.
Yehova anawuza Mose kuti, “Tsopano udzaona zimene ndimuchite Farao: Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzalola anthu anga kuti atuluke. Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzawatulutsa mʼdziko lake.”
2 And God said to Moses, I am Yahweh:
Mulungu anatinso kwa Mose, “Ine ndine Yehova.
3 I let myself be seen by Abraham, Isaac, and Jacob, as God, the Ruler of all; but they had no knowledge of my name Yahweh.
Ndinaonekera kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo monga Mulungu Wamphamvuzonse, koma sindinawadziwitse dzina langa kuti ndine Yehova.
4 And I made an agreement with them, to give them the land of Canaan, the land of their wanderings.
Ndinakhazikitsa pangano langa ndi iwo kuwalonjeza kuti ndidzawapatsa dziko la Kanaani kumene anakhalako kale ngati alendo.
5 And truly my ears are open to the cry of the children of Israel whom the Egyptians keep under their yoke; and I have kept in mind my agreement.
Ndamvanso kubuwula kwa Aisraeli, amene Aigupto awayesa akapolo ndipo ndakumbukira pangano langa.”
6 Say then to the children of Israel, I am Yahweh, and I will take you out from under the yoke of the Egyptians, and make you safe from their power, and will make you free by the strength of my arm after great punishments.
“Nʼchifukwa chake nena kwa Aisraeli kuti, ‘Ine ndine Yehova, ndipo ndidzakutulutsani mʼgoli la Aigupto. Ndidzakumasulani mu ukapolo, ndidzakuwombolani ndi dzanja langa lotambasuka ndi kuchita ntchito zachiweruzo.
7 And I will take you to be my people and I will be your God; and you will be certain that I am the Lord your God, who takes you out from under the yoke of the Egyptians.
Ndidzakutengani kukhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼgoli la Aigupto.
8 And I will be your guide into the land which I made an oath to give to Abraham, to Isaac, and to Jacob; and I will give it to you for your heritage: I am Yahweh.
Ndipo ndidzakufikitsani ku dziko limene ndinalumbira kuti ndidzalipereka kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo. Ndidzakupatsani dziko limenelo kuti likhale lanu. Ine ndine Yehova.’”
9 And Moses said these words to the children of Israel, but they gave no attention to him, because of the grief of their spirit and the cruel weight of their work.
Mose anawafotokozera Aisraeli zimenezi, koma iwo sanamumvere chifukwa cha kukhumudwa ndi goli lankhanza.
10 And the Lord said to Moses,
Kenaka Yehova anati kwa Mose,
11 Go in and say to Pharaoh, king of Egypt, that he is to let the children of Israel go out of his land.
“Pita ukawuze Farao mfumu ya Igupto kuti awalole Aisraeli atuluke mʼdziko lake.”
12 And Moses, answering the Lord, said, See, the children of Israel will not give ear to me; how then will Pharaoh give ear to me, whose lips are unclean?
Koma Mose ananena kwa Yehova kuti, “Ngati Aisraeli sanandimvere, Farao akandimvera chifukwa chiyani, pajatu sinditha kuyankhula bwino?”
13 And the word of the Lord came to Moses and Aaron, with orders for the children of Israel and for Pharaoh, king of Egypt, to take the children of Israel out of the land of Egypt.
Ndipo Yehova analamula Mose ndi Aaroni kuti awuze Aisraeli ndi Farao mfumu ya Igupto kuti Aisraeli ayenera kutuluka mʼdziko la Igupto.
14 These are the heads of their fathers' families: the sons of Reuben the oldest son of Israel: Hanoch and Pallu, Hezron and Carmi: these are the families of Reuben.
Atsogoleri a mafuko awo anali awa: Ana a Rubeni mwana wachisamba wa Israeli anali Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karimi. Awa anali mafuko a Rubeni.
15 And the sons of Simeon: Jemuel and Jamin and Ohad and Jachin and Zohar and Shaul, the son of a woman of Canaan: these are the families of Simeon.
Ana a Simeoni anali Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Saulo mwana wa kwa mkazi wa Chikanaani. Awa anali mafuko a Simeoni.
16 And these are the names of the sons of Levi in the order of their generations: Gershon and Kohath and Merari: and the years of Levi's life were a hundred and thirty-seven.
Mayina a ana a Levi pamodzi ndi zidzukulu zawo anali awa: Geresoni, Kohati ndi Merari. Levi anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
17 The sons of Gershon: Libni and Shimei, in the order of their families.
Ana a Geresoni, mwa mafuko awo, anali Libini ndi Simei.
18 And the sons of Kohath: Amram and Izhar and Hebron and Uzziel: and the years of Kohath's life were a hundred and thirty-three.
Ana a Kohati anali Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Kohati anakhala ndi moyo zaka 133.
19 And the sons of Merari: Mahli and Mushi: these are the families of the Levites, in the order of their generations.
Ana a Merari anali Mali ndi Musi. Awa anali mafuko a Levi monga mwa mibado yawo.
20 And Amram took Jochebed, his father's sister, as wife; and she gave birth to Aaron and Moses: and the years of Amram's life were a hundred and thirty-seven.
Amramu anakwatira Yokobedi mlongo wa abambo ake, amene anabereka Aaroni ndi Mose. Amramu anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
21 And the sons of Izhar: Korah and Nepheg and Zichri.
Ana a Izihari anali Kora, Nefegi ndi Zikiri.
22 And the sons of Uzziel: Mishael and Elzaphan and Sithri.
Ana a Uzieli anali Misaeli, Elizafani ndi Sitiri.
23 And Aaron took as his wife Elisheba, the daughter of Amminadab, the sister of Nahshon; and she gave birth to Nadab and Abihu, Eleazar and Ithamar.
Aaroni anakwatira Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wa Nasoni ndipo Iye anabereka Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
24 And the sons of Korah: Assir and Elkanah and Abiasaph: these are the families of the Korahites.
Ana a Kora anali Asiri, Elikana ndi Abiasafu. Awa ndiwo mafuko a Kora.
25 And Eleazar, Aaron's son, took as his wife one of the daughters of Putiel; and she gave birth to Phinehas. These are the heads of the families of the Levites, in the order of their families.
Eliezara mwana wa Aaroni anakwatira mmodzi mwa ana aakazi a Putieli, ndipo anabereka Finehasi. Awa anali atsogoleri a mabanja a Levi, monga mwa mafuko awo.
26 These are the same Aaron and Moses to whom the Lord said, Take the children of Israel out of the land of Egypt in their armies.
Aaroni ndi Mose ndi aja amene Yehova anawawuza kuti, “Tulutsani Aisraeli mu Igupto mʼmagulu awo.”
27 These are the men who gave orders to Pharaoh to let the children of Israel go out of Egypt: these are the same Moses and Aaron.
Mose ndi Aaroni ndiwo amene anayankhula ndi Farao mfumu ya Igupto kuti atulutse Aisraeli mu Igupto.
28 And on the day when the word of the Lord came to Moses in the land of Egypt,
Tsopano pamene Yehova anayankhula kwa Mose mu Igupto,
29 The Lord said to Moses, I am the Lord: say to Pharaoh, king of Egypt, everything I am saying to you.
anati, “Ine ndine Yehova. Umuwuze Farao mfumu ya Igupto zonse zimene Ine ndikuwuze iwe.”
30 And Moses said to the Lord, My lips are unclean; how is it possible that Pharaoh will give me a hearing?
Koma Mose anati kwa Yehova, “Farao akandimvera bwanji, pakuti ine sinditha kuyankhula bwino?”