< Exodus 22 >
1 If a man takes without right another man's ox or his sheep, and puts it to death or gets a price for it, he is to give five oxen for an ox, or four sheep for a sheep, in payment: the thief will have to make payment for what he has taken; if he has no money, he himself will have to be exchanged for money, so that payment may be made.
“Ngati munthu aba ngʼombe kapena nkhosa ndi kuyipha kapena kuyigulitsa, iye abweze ngʼombe zisanu pa ngʼombe imodzi ndi nkhosa zinayi pa nkhosa imodzi.
2 If a thief is taken in the act of forcing his way into a house, and his death is caused by a blow, the owner of the house is not responsible for his blood.
“Ngati mbala ipezeka ikuthyola nyumba ndipo imenyedwa nʼkufa, amene wapha mbalayo sanalakwe.
3 But if it is after dawn, he will be responsible.
Koma akayipha dzuwa litatuluka, woyiphayo ali ndi mlandu wakupha. “Mbala iyenera kubweza ndithu koma ngati ilibe kalikonse igulitsidwe, kulipira zomwe yabazo.
4 If he still has what he had taken, whatever it is, ox or ass or sheep, he is to give twice its value.
“Ngati chiweto chobedwacho chipezeka chamoyo mʼmanja mwake, kaya ndi ngʼombe kapena bulu kapena nkhosa, mbalayo ibwezere ziweto ziwiri pa chiweto chobedwacho.
5 If a man makes a fire in a field or a vine-garden, and lets the fire do damage to another man's field, he is to give of the best produce of his field or his vine-garden to make up for it.
“Ngati munthu alekerera ziweto zake kukalowa mʼmunda wa munthu wina kukadya mbewu zake, munthuyo amubwezere mwini mundawo mbewu zina zabwino kapena mpesa wina wabwino kwambiri.
6 If there is a fire and the flames get to the thorns at the edge of the field, causing destruction of the cut grain or of the living grain, or of the field, he who made the fire will have to make up for the damage.
“Ngati munthu ayatsa moto, motowo ndikukafika mpaka ku munda ndi kuwotcha mulu wa tirigu kapena tirigu wosadula, kapena munda wonse, ndiye kuti munthu amene anayatsa motoyo alipire.
7 If a man puts money or goods in the care of his neighbour to keep for him, and it is taken from the man's house, if they get the thief, he will have to make payment of twice the value.
“Ngati munthu asungitsidwa ndi mnzake ndalama kapena katundu, ndipo zinthu zija nʼkubedwa mʼnyumba mwake, wakubayo ngati agwidwa, ayenera kubwezera kawiri chobedwacho.
8 If they do not get the thief, let the master of the house come before the judges and take an oath that he has not put his hand on his neighbour's goods.
Koma ngati mbalayo sipezeka, mwini nyumbayo ayenera kukaonekera ku bwalo lamilandu kuti akamve ngati anaba katundu wa mnzakeyo.
9 In any question about an ox or an ass or a sheep or clothing, or about the loss of any property which anyone says is his, let the two sides put their cause before God; and he who is judged to be in the wrong is to make payment to his neighbour of twice the value.
Ngati pali kukangana kokhudza ngʼombe, bulu, nkhosa, zovala kapena kanthu kalikonse kotayika, ndipo mmodzi ndikunena kuti chinthucho nʼchake, awiriwo abwere nawo mlandu wawowo pamaso pa Mulungu ndipo amene mlandu umugomere adzayenera kumulipira mnzakeyo kawiri.
10 If a man puts an ass or an ox or a sheep or any beast into the keeping of his neighbour, and it comes to death or is damaged or is taken away, without any person seeing it:
“Ngati munthu wina anasungitsa mnzake bulu, ngʼombe, nkhosa, kapena chiweto chilichonse ndipo chiweto chija nʼkufa kapena kupweteka kapena kutengedwa popanda wina kuona,
11 If he takes his oath before the Lord that he has not put his hand to his neighbour's goods, the owner is to take his word for it and he will not have to make payment for it.
ndiye kuti anthu awiriwo ayenera kulumbira pamaso pa Mulungu kuti asatenge chinthu cha mnzake. Zikatero mwini katundu uja avomereze zimenezi ndipo asabwezeredwe kanthu.
12 But if it is taken from him by a thief, he is to make up for the loss of it to its owner.
Koma ngati chiwetocho chinabedwa, iye ayenera kubwezera mwini wakeyo.
13 But if it has been damaged by a beast, and he is able to make this clear, he will not have to make payment for what was damaged.
Ngati chinagwidwa ndi zirombo, iye ayenera kubweretsa zotsalira ngati umboni ndipo sadzalipira kanthu.
14 If a man gets from his neighbour the use of one of his beasts, and it is damaged or put to death when the owner is not with it, he will certainly have to make payment for the loss.
“Ngati munthu abwereka chiweto cha mnzake ndipo chiweto chija nʼkuvulala kapena kufa chikanali ndi iyebe, wobwerekayo ayenera kulipira.
15 If the owner is with it, he will not have to make payment: if he gave money for the use of it, the loss is covered by the payment.
Koma ngati mwini wakeyo ali ndi chiwetocho, wobwerekayo sadzalipira. Ngati anapereka ndalama pobwereka chiwetocho, ndalama anaperekazo zilowa mʼmalo mwa chiweto chakufacho.
16 If a man takes a virgin, who has not given her word to another man, and has connection with her, he will have to give a bride-price for her to be his wife.
“Ngati munthu anyenga namwali wosadziwa mwamuna amene sanapalidwe ubwenzi ndi kugona naye, munthuyo ayenera kulipira malowolo ndipo adzakhala mkazi wake.
17 If her father will not give her to him on any account, he will have to give the regular payment for virgins.
Ngati abambo ake akanitsitsa kwamtuwagalu kumupereka kuti amukwatire, munthuyo aperekebe malowolo woyenera namwaliyo.
18 Any woman using unnatural powers or secret arts is to be put to death.
“Musayilole mfiti yayikazi kuti ikhale ndi moyo.
19 Any man who has sex connection with a beast is to be put to death.
“Aliyense wogonana ndi chiweto ayenera kuphedwa.
20 Complete destruction will come on any man who makes offerings to any other god but the Lord.
“Aliyense wopereka nsembe kwa mulungu wina osati Yehova awonongedwe.
21 Do no wrong to a man from a strange country, and do not be hard on him; for you yourselves were living in a strange country, in the land of Egypt.
“Musazunze mlendo kapena kumuchitira nkhanza, pakuti inu munali alendo mʼdziko la Igupto.
22 Do no wrong to a widow, or to a child whose father is dead.
“Musazunze mkazi wamasiye kapena mwana wamasiye.
23 If you are cruel to them in any way, and their cry comes up to me, I will certainly give ear;
Ngati muwazunza ndipo iwo nʼkulirira kwa Ine, ndidzamva kulira kwawo.
24 And in the heat of my wrath I will put you to death with the sword, so that your wives will be widows and your children without fathers.
Ine ndidzakukwiyirani ndipo ndidzakuphani ndi lupanga. Akazi anu adzakhala amasiye ndiponso ana anu adzakhala wopanda abambo.
25 If you let any of the poor among my people have the use of your money, do not be a hard creditor to him, and do not take interest.
“Ngati mukongoza ndalama kwa mʼbale wanu amene ndi mʼmphawi pakati panu, musadzamuchite monga zimene amachita wokongoza ndalama. Musadzamuyikire chiwongoladzanja.
26 If ever you take your neighbour's clothing in exchange for the use of your money, let him have it back before the sun goes down:
Mukatenga chovala cha mnzanu kuti chikhale chikole mumubwezere dzuwa lisanalowe
27 For it is the only thing he has for covering his skin; what is he to go to sleep in? and when his cry comes up to me, I will give ear, for my mercy is great.
chifukwa chovala chimene amadzifundira nacho nʼchomwecho. Nanga usiku adzafunda chiyani? Tsonotu ngati adzandilirira, Ine ndidzamva pakuti ndine wachifundo.
28 You may not say evil of the judges, or put a curse on the ruler of your people.
“Musachite chipongwe Mulungu wanu kapena kutemberera mtsogoleri wa anthu anu.
29 Do not keep back your offerings from the wealth of your grain and your vines. The first of your sons you are to give to me.
“Musachedwe kupereka kwa Ine zokolola zanu zochuluka ndi vinyo wanu wochuluka. “Mundipatse ana anu achisamba aamuna.
30 In the same way with your oxen and your sheep: for seven days let the young one be with its mother; on the eighth day give it to me.
Muchite chimodzimodzi ndi ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu. Mwana woyamba kubadwa azikhala ndi amayi ake masiku asanu ndi awiri. Koma pa tsiku lachisanu ndi chitatu mwanayo muzimupereka kwa Ine.
31 You are to be holy men to me: the flesh of no animal whose death has been caused by the beasts of the field may be used for your food; it is to be given to the dogs.
“Inu mukhale anthu anga opatulika. Choncho musadye nyama ya chiweto chimene chaphedwa ndi zirombo. Nyamayo muwaponyere agalu.”