< Deuteronomy 30 >

1 Now when all these things have come on you, the blessing and the curse which I have put before you, if the thought of them comes back to your minds, when you are living among the nations where the Lord your God has sent you,
Madalitso ndi matemberero awa onse amene ndawayika pamaso panu akadzafika pa inu, inu nʼkukumbukira kulikonse kumene Yehova Mulungu wanu wakubalalitsirani pakati pa mitundu ya anthu,
2 And your hearts are turned again to the Lord your God, and you give ear to his word which I give you today, you and your children, with all your heart and with all your soul:
ndipo inu pamodzi ndi ana anu nʼkudzatembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse molingana ndi chilichonse chimene ndakulamulani lero lino,
3 Then the Lord will have pity on you, changing your fate, and taking you back again from among all the nations where you have been forced to go.
pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakukhalitsani monga kale ndi kukuchitirani chifundo, ndipo adzakusonkhanitsani kukuchotsani ku mitundu ina ya anthu kumene anakubalalitsirani.
4 Even if those who have been forced out are living in the farthest part of heaven, the Lord your God will go in search of you, and take you back;
Ngakhale atakupirikitsirani ku malekezero a dziko lapansi, adzakusonkhanitsani kuchokera kumeneko ndi kukubweretsaninso.
5 Placing you again in the land of your fathers as your heritage; and he will do you good, increasing you till you are more in number than your fathers were.
Adzakubweretsani ku dziko limene linali la makolo anu, ndipo lidzakhala lanu. Iye adzakulemeretsani ndi kukuchulukitsani kupambana makolo anu.
6 And the Lord your God will give to you and to your seed a circumcision of the heart, so that, loving him with all your heart and all your soul, you may have life.
Yehova Mulungu wanu adzasintha mitima yanu pamodzi ndi mitima ya zidzukulu zanu, kotero kuti mudzamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, ndipo mudzakhala ndi moyo.
7 And the Lord your God will put all these curses on those who are against you, and on your haters who put a cruel yoke on you.
Yehova Mulungu wanu adzayika matemberero awa onse pa adani anu amene amadana nanu ndi kukuzunzani.
8 And you will again give ear to the voice of the Lord, and do all his orders which I have given you today.
Inu mudzamveranso Yehova ndi kutsatira malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino.
9 And the Lord your God will make you fertile in all good things, blessing the work of your hands, and the fruit of your body, and the fruit of your cattle, and the fruit of your land: for the Lord will have joy in you, as he had in your fathers:
Pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakulemeretsani pa zochita zanu zonse ndipo adzakupatsani ana ambiri, zoweta zambiri, ndiponso mudzakhala ndi zokolola zambiri za mʼdziko lanu. Yehova adzakondwera nanunso ndi kukulemeretsani monga momwe anakondwera ndi makolo anu,
10 If you give ear to the voice of the Lord your God, keeping his orders and his laws which are recorded in this book of the law, and turning to the Lord your God with all your heart and with all your soul.
ngati mudzamvera Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ake ndi mawu ake amene alembedwa Mʼbuku ili la Malamulo ndi kutembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
11 For these orders which I have given you today are not strange and secret, and are not far away.
Tsopano zimene ndikukulamulirani leroli sizovuta kapena zapatali.
12 They are not in heaven, for you to say, Who will go up to heaven for us and give us knowledge of them so that we may do them?
Sizili kumwamba, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene akwere kumwamba kuti akazitenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
13 And they are not across the sea, for you to say, Who will go over the sea for us and give us news of them so that we may do them?
Komanso sizili pa tsidya la nyanja, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene adzawoloke nyanja kuti akatenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
14 But the word is very near you, in your mouth and in your heart, so that you may do it.
Ayi, mawu ali pafupi ndi inu; ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu kuti muwamvere.
15 See, I have put before you today, life and good, and death and evil;
Taonani, lero ine ndayika pamaso panu moyo ndi zokoma, imfa ndi chiwonongeko.
16 In giving you orders today to have love for the Lord your God, to go in his ways and keep his laws and his orders and his decisions, so that you may have life and be increased, and that the blessing of the Lord your God may be with you in the land where you are going, the land of your heritage.
Pakuti lero ndikukulamulani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kuti muyende mʼnjira zake, ndi kusunga malamulo ake, malangizo ake. Mukatero mudzakhala ndi moyo ndi kuchulukana, ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene mukulowa kukakhalamo.
17 But if your heart is turned away and your ear is shut, and you go after those who would make you servants and worshippers of other gods:
Koma ngati mtima wanu udzatembenuka, inu nʼkukhala osandimvera, ndipo ngati mudzatengeka ndi kupita kukagwadira milungu ina ndi kuyipembedza,
18 I give witness against you this day that destruction will certainly be your fate, and your days will be cut short in the land where you are going, the land of your heritage on the other side of Jordan.
lero ndikulengeza kwa inu kuti mudzawonongeka ndithu. Simudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukulowamo pamene mukuwoloka Yorodani kuti mulitenge.
19 Let heaven and earth be my witnesses against you this day that I have put before you life and death, a blessing and a curse: so take life for yourselves and for your seed:
Lero kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni zodzakutsutsani pakuti ndayika pamaso panu moyo ndi imfa, madalitso ndi matemberero. Tsopano sankhani moyo kuti inu ndi ana anu mukhale ndi moyo.
20 In loving the Lord your God, hearing his voice and being true to him: for he is your life and by him will your days be long: so that you may go on living in the land which the Lord gave by an oath to your fathers, Abraham, Isaac and Jacob.
Ndi kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kumvera mawu ake, ndi kukhulupirika kwa Iye. Pakuti Yehova ndiye moyo wanu, ndipo mudzakhala zaka zambiri mʼdziko limene analumbira kulipereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo.

< Deuteronomy 30 >