< Amos 6 >
1 Sorrow to those who are resting in comfort in Zion, and to those who have no fear of danger in the mountain of Samaria, the noted men of the chief of the nations, to whom the people of Israel come!
Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni, ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya, inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka, kumene Aisraeli amafikako!
2 Go on to Calneh and see; and from there go to Hamath the great; then go down to Gath of the Philistines: are you better than these kingdoms? or is your land wider than theirs?
Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane; mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja, ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti. Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa? Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
3 You who put far away the evil day, causing the rule of the violent to come near;
Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika, zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
4 Who are resting on beds of ivory, stretched out on soft seats, feasting on lambs from the flock and young oxen from the cattle-house;
Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu, mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu. Mumadya ana ankhosa onona ndi ana angʼombe onenepa.
5 Making foolish songs to the sound of corded instruments, and designing for themselves instruments of music, like David;
Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
6 Drinking wine in basins, rubbing themselves with the best oils; but they have no grief for the destruction of Joseph.
Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri, koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
7 So now they will go away prisoners with the first of those who are made prisoners, and the loud cry of those who were stretched out will come to an end.
Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo; maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.
8 The Lord God has taken an oath by himself, says the Lord, the God of armies: the pride of Jacob is disgusting to me, and I have hate for his great houses: so I will give up the town with everything in it.
Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti, “Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo, ndimadana ndi nyumba zake zaufumu; Ine ndidzawupereka mzindawu pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”
9 Then it will come about that if there are still ten men in a house, death will overtake them.
Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu.
10 And when a man's relation, even the one who is responsible for burning his body, lifting him up to take his bones out of the house, says to him who is in the inmost part of the house, Is there still anyone with you? and he says, No; then he will say, Keep quiet, for the name of the Lord may not be named.
Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”
11 For see, at the order of the Lord the great house will be full of cracks and the little house will be broken.
Pakuti Yehova walamula kuti nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula, ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.
12 Is it possible for horses to go running on the rock? may the sea be ploughed with oxen? for the right to be turned by you into poison, and the fruit of righteousness into a bitter plant?
Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe? Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja? Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
13 You whose joy is in a thing of no value, who say, Have we not taken for ourselves horns by the strength which is ours?
Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”
14 For see, I will send against you a nation, O Israel, says the Lord, the God of armies, ruling you cruelly from the way into Hamath as far as the stream of the Arabah.
Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti, “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu umene udzakuzunzani kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”