< 2 Samuel 22 >
1 And David made a song to the Lord in these words, on the day when the Lord made him free from the hands of all his haters, and from the hand of Saul:
Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
2 And he said, The Lord is my Rock, my walled town, and my saviour, even mine;
Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
3 My God, my Rock, in him will I put my faith; my breastplate, and the horn of my salvation, my high tower, and my safe place; my saviour, who keeps me safe from the violent man.
Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
4 I will send up my cry to the Lord, who is to be praised; so will I be made safe from those who are against me.
“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
5 For the waves of death came round me, and the seas of evil put me in fear;
“Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
6 The cords of hell were round me: the nets of death came on me. (Sheol )
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
7 In my trouble my voice went up to the Lord, and my cry to my God: my voice came to his hearing in his holy Temple, and my prayer came to his ears.
“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
8 Then the earth was moved with a violent shock; the bases of heaven were moved and shaking, because he was angry.
“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
9 There went up a smoke from his nose, and a fire of destruction from his mouth: coals were lighted by it.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
10 The heavens were bent, so that he might come down; and it was dark under his feet.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
11 And he went through the air, seated on a storm-cloud: going quickly on the wings of the wind.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
12 And he made the dark his tent round him, a mass of waters, thick clouds of the skies.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
13 Before his shining light his dark clouds went past, raining ice and coals of fire.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
14 The Lord made thunder in the heavens, and the voice of the Highest was sounding out.
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
15 And he sent out his arrows, driving them in all directions; by his flames of fire they were troubled.
Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
16 Then the deep beds of the sea were seen, and the bases of the world were uncovered, because of the Lord's wrath, because of the breath of his mouth.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
17 He sent from on high, he took me, pulling me out of great waters.
“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
18 He made me free from my strong hater, from those who were against me, because they were stronger than I.
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
19 They came on me in the day of my trouble: but the Lord was my support.
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
20 He took me out into a wide place; he was my saviour because he had delight in me.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
21 The Lord gives me the reward of my righteousness, because my hands are clean before him.
“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
22 For I have kept the ways of the Lord; I have not been turned away in sin from my God.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
23 For all his decisions were before me, and I did not put away his laws from me.
Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
24 And I was upright before him, and I kept myself from sin.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
25 Because of this the Lord has given me the reward of my righteousness, because my hands are clean in his eyes.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
26 On him who has mercy you will have mercy; to the upright you will be upright;
“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
27 He who is holy will see that you are holy; but to the man whose way is not straight you will be a hard judge.
Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
28 For you are the saviour of those who are in trouble; but your eyes are on men of pride, to make them low.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
29 For you are my light, O Lord; and the Lord will make the dark bright for me.
Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
30 By your help I have made a way through the wall which was shutting me in: by the help of my God I have gone over a wall.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
31 As for God, his way is all good: the word of the Lord is tested; he is a safe cover for all those who put their faith in him.
“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
32 For who is God but the Lord? and who is a Rock but our God?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
33 God puts a strong band about me, guiding me in a straight way.
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
34 He makes my feet like roes' feet, and puts me on high places.
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
35 He makes my hands expert in war, so that a bow of brass is bent by my arms.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
36 You have given me the breastplate of your salvation, and your mercy has made me great.
Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
37 You have made my steps wide under me, so that my feet make no slip.
Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
38 I go after my haters and overtake them; not turning back till they are all overcome.
“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
39 I have sent destruction on them and given them wounds, so that they are not able to get up: they are stretched under my feet.
Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
40 For I have been armed by you with strength for the fight: you have made low under me those who came out against me.
Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
41 By you their backs are turned in flight, so that my haters are cut off.
Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
42 They were crying out, but there was no one to come to their help: even to the Lord, but he gave them no answer.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
43 Then they were crushed as small as the dust of the earth, stamped down under my feet like the waste of the streets.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
44 You have made me free from the fightings of my people; you have made me the head of the nations: a people of whom I had no knowledge will be my servants.
“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
45 Men of other countries will, with false hearts, put themselves under my authority: from the time when my name comes to their ears, they will be ruled by me.
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
46 They will be wasted away, they will come out of their secret places shaking with fear.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
47 The Lord is living; praise be to my Rock, and let the God of my salvation be honoured:
“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
48 It is God who sends punishment on my haters, and puts peoples under my rule.
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
49 He makes me free from my haters: I am lifted up over those who come up against me: you have made me free from the violent man.
amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
50 Because of this I will give you praise, O Lord, among the nations, and will make a song of praise to your name.
Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
51 Great salvation does he give to his king; he has mercy on the king of his selection, David, and on his seed for ever.
“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”