< 2 Kings 4 >
1 Now a certain woman, the wife of one of the sons of the prophets, came crying to Elisha and said, Your servant my husband is dead; and to your knowledge he was a worshipper of the Lord; but now, the creditor has come to take my two children as servants in payment of his debt.
Mkazi wa mmodzi mwa ana a aneneri anafuwula kwa Elisa kuti, “Mtumiki wanu, mwamuna wanga wamwalira ndipo inu mukudziwa kuti ankaopa Yehova. Koma tsopano munthu amene mwamuna wanga anakongolako zinthu zake, akubwera kudzatenga ana anga awiri aamuna kuti akhale akapolo ake.”
2 Then Elisha said to her, What am I to do for you? say now, what have you in the house? And she said, Your servant has nothing in the house but a pot of oil.
Elisa anayankha mayiyo kuti, “Kodi ufuna ndikuchitire chiyani? Tandiwuza uli ndi chiyani mʼnyumba mwako?” Mayiyo anayankha kuti, “Mdzakazi wanu alibe kanthu kalikonse koma timafuta pangʼono chabe.”
3 Then he said, Go out to all your neighbours and get vessels, a very great number of them.
Elisa anati, “Pita kabwereke mitsuko yonse yopanda kanthu kwa anzako. Usakabwereke mitsuko yochepa.
4 Then go in, and, shutting the door on yourself and your sons, put oil into all these vessels, putting on one side the full ones.
Kenaka ukalowe mʼnyumba mwako ndi kudzitsekera iwe ndi ana ako. Mukakatero mukakhuthulire mafuta mʼmitsuko yonseyo, ndipo mtsuko uliwonse ukadzaza muzikawuyika pambali.”
5 So she went away, and when the door was shut on her and her sons, they took the vessels to her and she put oil into them.
Mayi uja anachoka kwa Elisa nakadzitsekera ndi ana ake. Anthu anabweretsa mitsuko kwa iye ndipo ankathiramo mafuta.
6 And when all the vessels were full, she said to her son, Get me another vessel. And he said, There are no more. And the flow of oil was stopped.
Mitsuko yonse itadzaza, mayiyo anawuza mwana wake kuti, “Bweretsa mtsuko wina.” Koma iye anayankha kuti, “Mitsuko yonse yatha.” Pamenepo mafuta analeka kutuluka.
7 So she came to the man of God and gave him word of what she had done. And he said, Go and get money for the oil and make payment of your debt, and let the rest be for the needs of yourself and your sons.
Mayiyo anapita nakamuwuza munthu wa Mulungu amene anamuyankha kuti, “Pita, kagulitse mafutawo ndipo ukabweze ngongole ija. Ndalama zotsalazo zikakhale zako ndi ana ako.”
8 Now there came a day when Elisha went to Shunem, and there was a woman of high position living there, who made him come in and have a meal with her. And after that, every time he went by, he went into her house for a meal.
Tsiku lina Elisa anapita ku Sunemu. Kumeneko kunkakhala mayi wina wachuma amene anawumiriza Elisa kuti adye chakudya. Choncho nthawi iliyonse imene Elisa amadutsa kumeneko, ankayima ndi kudya.
9 And she said to her husband, Now I see that this is a holy man of God, who comes by day after day.
Mayiyo anawuza mwamuna wake kuti, “Taonani, ine ndikudziwa kuti munthu amene amadutsa pano nthawi zambiriyu ndi munthu woyera wa Mulungu.
10 So let us make a little room on the wall; and put a bed there for him, and a table and a seat and a light; so that when he comes to us, he will be able to go in there.
Tiyeni timumangire kachipinda kakangʼono pa denga la nyumbayi ndi kumuyikiramo bedi ndi tebulo, mpando ndi nyale. Akabwera kuno azikhala mʼmenemo.”
11 Now one day, when he had gone there, he went into the little room and took his rest there.
Tsiku lina pamene Elisa anafika ku Sunemu, iye anakalowa mʼchipinda chake chija nagona mʼmenemo.
12 And he said to Gehazi, his servant, Send for this Shunammite. So in answer to his voice she came before him.
Iye anati kwa mtumiki wake Gehazi, “Muyitane Msunemuyu.” Ndipo anapita kukamuyitana mayiyo, ndipo anabwera nayima pamaso pa Elisa.
13 And he said to him, Now say to her, See, you have taken all this trouble for us; what is to be done for you? will you have any request made for you to the king or the captain of the army? But she said, I am living among my people.
Elisa anati kwa Gehazi, “Muwuze mayiyo kuti, ‘Wavutika potichitira zonsezi. Nanga tsopano ifeyo tikuchitire chiyani? Kodi ukufuna kuti tikadziwitse mfumu kapena mtsogoleri wa ankhondo zimene watichitirazi?’” Mayiyo anayankha kuti, “Ine ndimakhala mwamtendere pakati pa abale anga.”
14 So he said, What then is to be done for her? And Gehazi made answer, Still there is this, she has no son and her husband is old.
Elisa anafunsanso Gehazi kuti, “Kodi tingamuchitire chiyani?” Gehazi anati, “Ndithu, mayiyu alibe mwana ndipo mwamuna wake ndi wokalamba.”
15 Then he said, Send for her. And in answer to his voice she took her place at the door.
Pamenepo Elisa anati, “Muyitane.” Choncho Gehazi anamuyitana, ndipo iye anabwera nayima pa khomo.
16 And Elisha said, At this time in the coming year you will have a son in your arms. And she said, No, my lord, O man of God, do not say what is false to your servant.
Elisa anati kwa mayiyo, “Nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, udzakhala utanyamula mwana wamwamuna mʼmanja mwako.” Mayiyo anatsutsa zimenezi nanena kuti, “Ayi mbuye wanga. Inu munthu wa Mulungu, musanamize mdzakazi wanu!”
17 Then the woman became with child and gave birth to a son at the time named, in the year after, as Elisha had said to her.
Koma mayi uja anakhala woyembekezera, ndipo chaka chotsatiracho, nthawi ngati yomweyo anabereka mwana wamwamuna monga momwe Elisa anamuwuzira.
18 Now one day, when the child was older, he went out to his father to where the grain was being cut.
Mwana uja anakula, ndipo tsiku lina anapita kwa abambo ake amene anali ndi anthu odula tirigu.
19 And he said to his father, My head, my head! And the father said to a servant, Take him in to his mother.
Mwanayo anafuwula kwa abambo ake kuti, “Mayo! Mutu wanga ine! Mayo! Mutu wanga ine!” Abambo akewo anawuza wantchito wake kuti, “Munyamule ndi kukamupereka kwa amayi ake.”
20 And he took him in to his mother, and she took him on her knees and kept him there till the middle of the day, when his life went from him.
Wantchito uja atamunyamula ndi kumupereka kwa amayi ake. Mwanayo anakhala pa miyendo ya amayi akeyo mpaka masana, ndipo pambuyo pake anamwalira.
21 Then she went up and put him on the bed of the man of God, shutting the door on him, and went out.
Mayiyo ananyamula mwanayo nakamugoneka pa bedi la munthu wa Mulungu uja. Kenaka anatseka chitseko iye nʼkuchokapo.
22 And she said to her husband, Send me one of the servants and one of the asses so that I may go quickly to the man of God and come back again.
Iye anayitanitsa mwamuna wake namuwuza kuti, “Tumizireni wantchito mmodzi ndi bulu mmodzi kuti ndipite mofulumira kwa munthu wa Mulungu nʼkubwererako.”
23 And he said, Why are you going to him today? it is not a new moon or a Sabbath. But she said, It is well.
Mwamuna wakeyo anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani ukupita kwa iyeyo lero? Lero si tsiku la Chikondwerero cha Mwezi Watsopano kapena tsiku la Sabata.” Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”
24 Then she made the ass ready and said to her servant, Keep driving on; do not make a stop without orders from me.
Mayiyo anamangirira chishalo pa bulu ndipo anawuza wantchito wake kuti, “Yendetsa bulu mofulumira. Usachepetse liwiro pokhapokha nditakuwuza.”
25 So she went, and came to Mount Carmel, to the man of God. And when the man of God saw her coming in his direction, he said to Gehazi, his servant, See, there is the Shunammite;
Choncho ananyamuka nakafika kwa munthu wa Mulungu uja ku Phiri la Karimeli. Munthu wa Mulungu ataona mayiyo patali, anawuza mtumiki wake Gehazi kuti, “Taona! Msunemu uyo!
26 Go quickly to her, and on meeting her say to her, Are you well? and your husband and the child, are they well? And she said in answer, All is well.
Thamanga msanga ukakumane naye ndipo ukamufunse kuti, ‘Kodi muli bwino? Kodi mwamuna wanu ali bwino? Kodi mwana wanu ali bwino?’” Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”
27 And when she came to where the man of God was on the hill, she put her hands round his feet; and Gehazi came near with the purpose of pushing her away; but the man of God said, Let her be, for her soul is bitter in her; and the Lord has kept it secret from me, and has not given me word of it.
Atafika kwa munthu wa Mulunguyo pa phiripo, mayiyo anagwira mapazi a Elisa. Gehazi anabwera kuti amukankhe, koma munthu wa Mulungu anati, “Musiye! Iyeyu ali pa mavuto aakulu, koma Yehova wandibisira zimenezi ndipo sanandiwuze chifukwa chake.”
28 Then she said, Did I make a request to my lord for a son? did I not say, Do not give me false words?
Tsono mayiyo anati, “Mbuye wanga, kodi ine ndinakupemphani mwana? Kodi sindinakuwuzeni kuti musandinamize?”
29 Then he said to Gehazi, Make yourself ready, and take my stick in your hand, and go: if you come across anyone on the way, give him no blessing, and if anyone gives you a blessing, give him no answer. And put my stick on the child's face.
Elisa anawuza Gehazi kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga ndodo yanga mʼdzanja lako ndipo thamanga. Ngati ukumana ndi munthu wina aliyense, usamupatse moni, ndipo ngati wina akupatsa moni, usayankhe. Ukagoneke ndodo yanga pa nkhope ya mwanayo.”
30 But the mother of the child said, As the Lord is living and as your soul is living, I will not go back without you. So he got up and went with her.
Koma mayi wake wa mwana uja anati, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Choncho Elisa ananyamuka natsatira mayiyo.
31 And Gehazi went on before them and put the stick on the child's face; but there was no voice, and no one gave attention. So he went back, and meeting him gave him the news, saying, The child is not awake.
Gehazi anatsogola nakagoneka ndodoyo pa nkhope ya mwanayo, koma sipanamveke mawu kapena kugwedezeka kuonetsa kuti ali moyo. Choncho Gehazi anabwerera kukakumana ndi Elisa ndipo anamuwuza kuti, “Mwanayo sanatsitsimuke.”
32 And when Elisha came into the house he saw the child dead, stretched on his bed.
Ndipo Elisa atafika ku nyumbako, taonani, mwanayo anali wakufa atamugoneka pa bedi lake.
33 So he went in, and shutting the door on the two of them, made prayer to the Lord.
Elisa analowa mʼnyumbamo natseka chitseko. Anali awiri okha mʼchipindamo ndipo iye anapemphera kwa Yehova.
34 Then he got up on the bed, stretching himself out on the child, and put his mouth on the child's mouth, his eyes on his eyes and his hands on his hands; and the child's body became warm.
Kenaka anakwera pa bedi ndi kumugonera mwanayo, pakamwa pake panakhudzana ndi pakamwa pa mwanayo, maso ake anakhudzana ndi maso a mwanayo, ndipo manja ake anakhudzana ndi manja a mwanayo. Pamene ankadzitambalitsa yekha pa mwanayo, thupi la mwanayo linayamba kufunda.
35 Then he came back, and after walking once through the house and back, he went up, stretching himself out on the child seven times; and the child's eyes became open.
Elisa anatembenuka nayenda uku ndi uku kamodzi mʼchipindamo ndipo kenaka anakweranso pa bedi nagoneranso mwanayo. Mwanayo anayetsemula kasanu ndi kawiri ndipo anatsekula maso ake.
36 And he gave orders to Gehazi, and said, Send for the Shunammite. And she came in answer to his voice. And he said, Take up your son.
Elisa anayitana Gehazi ndipo anati, “Muyitane Msunemuyo.” Ndipo anaterodi. Mayiyo atabwera, Elisa anati, “Tenga mwana wako.”
37 And she came in, and went down on her face to the earth at his feet; then she took her son in her arms and went out.
Mayiyo analowa, nagwada pa mapazi a Elisa, naweramitsa mutu wake pansi. Kenaka ananyamula mwana wake natuluka.
38 And Elisha went back to Gilgal, now there was very little food in the land; and the sons of the prophets were seated before him. And he said to his servant, Put the great pot on the fire, and make soup for the sons of the prophets.
Elisa anabwerera ku Giligala ndipo ku dera limenelo kunali njala. Elisa akukumana ndi ana a aneneri, anati kwa mtumiki wake, “Ika mʼphika waukulu pa moto ndipo uwaphikire chakudya anthu awa.”
39 And one went out into the field to get green plants and saw a vine of the field, and pulling off the fruit of it till the fold of his robe was full, he came back and put the fruit, cut up small, into the pot of soup, having no idea what it was.
Mmodzi mwa ana aneneriwo anapita kuthengo kukafuna ndiwo ndipo anakapeza mpesa wakuthengo. Iye anathyolako zipatso zake nadzaza nsalu yake. Atabwerera, anazidula zipatsozo naziyika mu mʼphika, ngakhale kuti panalibe amene ankazidziwa.
40 Then they gave the men soup from the pot. And while they were drinking the soup, they gave a cry, and said, O man of God, there is death in the pot; and they were not able to take any more food.
Anawapakulira anthu chakudyacho, koma atayamba kudya, anthuwo anafuwula kuti, “Inu munthu wa Mulungu muli imfa mu mʼphikamu!” Ndipo sakanatha kudya chakudyacho.
41 But he said, Get some meal. And he put it into the pot, and said, Now give it to the people so that they may have food. And there was nothing bad in the pot.
Elisa anati, “Bweretsani ufa.” Iye anathira ufa mu mʼphikamo ndipo anati, “Perekani chakudyachi kwa anthu kuti adye.” Ndipo mu mʼphikamo munalibenso zoopsa.
42 Now a man came from Baal-shalishah with an offering of first-fruits for the man of God, twenty barley cakes and garden fruit in his bag. And he said, Give these to the people for food.
Munthu wina wochokera ku Baala-Salisa anabwera atamutengera munthu wa Mulungu malofu a barele makumi awiri opangidwa kuchokera ku zokolola zoyamba kucha, pamodzinso ndi ngala zatsopano za tirigu. Elisa anati kwa munthuyo, “Apatse anthu kuti adye.”
43 But his servant said, How am I to put this before a hundred men? But he said, Give it to the people for food; for the Lord says, There will be food for them and some over.
Mtumiki wake anafunsa kuti, “Kodi ndikachigawe motani chakudyachi kwa anthu 100?” Koma Elisa anamuwuzanso kuti, “Apatse anthu adye. Pakuti izi ndi zimene Yehova akunena kuti, ‘Iwo adzadya chakudyachi ndipo china chidzatsalako.’”
44 So he put it before them, and they had a meal and there was more than enough, as the Lord had said.
Tsono iye anachipereka kwa anthuwo ndipo anadya china nʼkutsalako, molingana ndi mawu a Yehova.